< Salamo 94 >

1 O ry Iehovà, Andrianañahare mpamale-fate, ry Andrianañahare, mpañome-to: mireandreaña.
Inu Yehova, ndinu Mulungu wobwezera chilango, Inu Mulungu amene mumabwezera chilango, wonetsani kuwala kwanu.
2 Miongaha, ry Mpizaka’ ty tane toio; lilovo ami’ty fañeva’e o mpirengevokeo.
Nyamukani, Inu woweruza wa dziko lapansi; bwezerani kwa odzikuza zowayenera.
3 Sikal’ ombia o lo-tsere­keo, ry Iehovà: pak’ombia ty mbe hitreña’ o tsivokatseo?
Kodi mpaka liti anthu oyipa Inu Yehova, mpaka liti anthu oyipa adzalumpha ndi chimwemwe?
4 Mifatatiake, manotratsotrake; mijiajia iaby o mpanao ratio.
Amakhuthula mawu onyada; onse ochita zoyipa ndi odzaza ndi kudzikuza.
5 Demohe’ iereo ondati’oo ry Iehovà, volevole’ iereo ty lova’o.
Amaphwanya anthu anu, Inu Yehova; amapondereza cholowa chanu.
6 Vonoe’ iereo ty vantotse naho ty renetane, naho mañoho-doza amo bode-raeo;
Amaphanso amayi a masiye ndi alendo okhala nawo mʼdziko; amapha ana amasiye.
7 vaho manao ti-hoe: Tsy vazoho’ Ià; tsy mañaoñe t’i Andrianañahare’ Iakobe.
Iwo amati, “Yehova sakuona; Mulungu wa Yakobo salabadirako.”
8 Mañaraharà ry borololo am’ ondatio; naho o dagolao, ombia t’ie hahafohiñe?
Samalani, inu anthu opanda nzeru pakati pa anthu; zitsiru inu, kodi mudzakhala liti anzeru?
9 Tsy mahajanjiñe hao i nambole o ravembiaoy? Tsy mahavazoho hao i Mpitsene fihainoy?
Kodi Iye amene anapanga khutu sangathe kumva? Kodi Iye amene anapanga diso sangathe kuona?
10 Tsy hanoro hao i Mpandilo o fifeheañeo? ie mañòke hilala am’ondatio.
Kodi Iye amene amalangiza mitundu ya anthu sangathenso kulanga? Kodi Iye amene amaphunzitsa munthu angasowe nzeru?
11 Arofoana’ Iehovà ty fitsakorea’ ondaty; t’ie kofòke avao.
Yehova amadziwa maganizo a munthu; Iye amadziwa kuti maganizowo ndi achabechabe.
12 Haha t’indaty lilove’o ry Ià, naho i anara’o amy Tsara’oy;
Wodala munthu amene Inu Yehova mumamulangiza, munthu amene mumamuphunzitsa kuchokera mulamulo lanu;
13 homea’o fitofàñe an-tsan-kasotriañe, ampara’ te nihaliañe koboñe o lo-tserekeo.
mumamupumitsa pa nthawi ya mavuto, mpaka woyipa atakumbiridwa dzenje.
14 Tsy ho farie’ Iehovà ondati’eo; tsy haforintse’e i lova’ey.
Pakuti Yehova sadzawakana anthu ake; Iye sadzasiya cholowa chake.
15 Mbe himpoly ami’ty hahiti’e o zakao, le hene hañorik’ aze o vañoñ’ añ’arofoo.
Chiweruzo chidzakhazikikanso pa chilungamo, ndipo onse olungama mtima adzachitsata.
16 Ia ty hitroatse amo tsereheñeo ho ahy? Ia ty hijohañe amo mpanao ratio ho amakoo?
Ndani adzadzuka chifukwa cha ine kulimbana ndi anthu oyipa? Ndani adzayimirira mʼmalo mwanga kulimbana ndi anthu ochita zoyipa?
17 Naho tsy Iehovà ty nañimb’ ahy le ho nitobe am-pitsiñañe ty fiaiko.
Yehova akanapanda kundithandiza, bwenzi nditakakhala msanga ku malo achete a imfa.
18 Ie anoeko ty hoe: Midorasitse ty tomboko; le manozañ’ ahy ty fiferenaiña’o ry Iehovà.
Ndikanena kuti, “Phazi langa likuterereka,” chikondi chanu, Inu Yehova, chimandichirikiza.
19 Ie mañotrotro ty hamahimahin-troke, le mampanintsiñe ty fiaiko o fañohòa’oo.
Pamene nkhawa inakula mʼkati mwanga, chitonthozo chanu chinabweretsa chimwemwe mʼmoyo mwanga.
20 Mete hiharo-rehak’ ama’o hao ty fitobohan-katsivokarañe— ie mikitro-draha hatao’e fañè,
Kodi mpando waufumu woyipa ungathe kugwirizana nanu umene umabweretsa masautso chifukwa cha malamulo ake?
21 naho mirañadrañake hañè-doza ami’ty fiai’ o vañoñeo, vaho mañozoñe ty lio tsy aman-kila.
Iwo amasonkhana pamodzi kulimbana ndi wolungama ndi kugamula kuti wosalakwa aphedwe.
22 Fe haboam-pitsolohako t’Iehovà, vaho lamilamy fipalirako t’i Andrianañahareko.
Koma Yehova wakhala linga langa, ndipo Mulungu ndiye thanthwe limene ndimathawirako.
23 Nampolia’e ty hatsivokara’ iareo, vaho ho mongora’e ty amo fikotriha’iareoo; toe ihañitoa’ Iehovà Andrianañaharentika.
Iye adzawabwezera chifukwa cha machimo awo ndi kuwawononga chifukwa cha kuyipa kwawo; Yehova Mulungu wathu adzawawononga.

< Salamo 94 >