< Salamo 47 >

1 Mitehafa fitañe, ry hene ondatio; poñafo aman’Añahare ty fiarañanañam-pirebehañe.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la ana a Kora. Ombani mʼmanja, inu anthu onse; fuwulani kwa Mulungu ndi mawu achimwemwe.
2 Mampañeveñe t’Iehovà andindimoneñe ey, ie mpanjaka jabahina’ ty tane toy.
Ndi woopsadi Yehova Wammwambamwamba; Mfumu yayikulu ya dziko lonse lapansi!
3 Ampiambane’e aman-tika ondatio, ze kilakila ondaty ambanem-pandian-tikañ’ ao.
Iye anatigonjetsera mitundu yambirimbiri ya anthu; anayika anthu pansi pa mapazi athu.
4 Ie i nijoboñe lova ho antikañey, ty firengea’ Iakobe kokoa’ey. Selà
Iye anatisankhira cholowa chathu, chonyaditsa cha Yakobo, amene anamukonda. (Sela)
5 Nionjoñe am-pipoñafam-pitreñañe t’i Andrianañahare; ami’ty fivolan’antsiva t’Iehovà.
Mulungu wakwera, anthu akumufuwulira mwachimwemwe, Yehova wakwera, akumuyimbira malipenga.
6 Takasio t’i Andrianañahare, isabo; takasio i mpanjakan-tikañey, isabo.
Imbani matamando kwa Mulungu, imbani matamando; imbani matamando kwa mfumu yathu, imbani matamando.
7 I Andrianañahare ro mpanjaka’ ty tane toy; mitakasia an-tsabo soa arake.
Pakuti Mulungu ndi mfumu ya dziko lonse lapansi; imbirani Iye salimo la matamando.
8 Fehen’ Andrianañahare o fifeheañeo; miambesatse am-piambesa’e masiñe eo t’i Andrianañahare.
Mulungu akulamulira mitundu ya anthu; Mulungu wakhala pa mpando wake waufumu woyera.
9 Mifanontoñe o roandria’ ondatio; ondatin’ Andrianañahare’ i Avrahameo fa an’Andrianañahare o fikalan-defo’ ty tane toio; ie onjoneñ’ an-tiotiotse ey.
Anthu otchuka mwa anthu a mitundu ina asonkhana monga anthu a Mulungu wa Abrahamu, pakuti mafumu a dziko lapansi ndi ake a Mulungu; Iye wakwezedwa kwakukulu.

< Salamo 47 >