< Salamo 43 >
1 Meo to, ry Andrianañahare, mañalañalaña ho ahy amy fifeheañe tsy aman-Kàkey; hahao am’ondaty mamañahy naho mengokeo.
Onetsani kusalakwa kwanga Inu Mulungu; ndipo mundinenere mlandu wanga kutsutsana ndi mtundu wosapembedza; mundilanditse mʼmanja mwa achinyengo ndi anthu oyipa.
2 Ihe ro Andrianañaharen-kaozarako; Ino ty nifaria’o ahiko? Ino ty ibokobokoako am-pigoboñañe ao ie forekeken-drafelahy?
Pajatu Inu Mulungu ndinu mphamvu zanga. Nʼchifukwa chiyani mwandikana ine? Nʼchifukwa chiyani ndiyenera kuyenda ndikulira, woponderezedwa ndi mdani?
3 Ahitrifo ty hazavà’o naho ty hatò’o, hiaolo, hanese ahy mb’amy vohi’o miavakey mb’eo, vaho mb’an-kivoho’o mb’eo.
Tumizani kuwunika kwanu ndi choonadi chanu kuti zinditsogolere; mulole kuti zindifikitse ku phiri lanu loyera, kumalo kumene inu mumakhala.
4 Le homb’an-kitrelin’ Añahare mb’eo, mb’aman’Añahare mampinembanembañ’ ahy, vaho ho saboeko ami’ty marovany, t’i Abo-Tia, Andrianañahareko.
Ndipo ndidzapita ku guwa lansembe la Mulungu, kwa Mulungu, chimwemwe changa ndi chikondwerero changa. Ndidzakutamandani ndi zeze, Inu Mulungu wanga.
5 Ino ty mahalonjetse azo ty fiaiko tia? inoñe ty angoihoia’o amako ao? Mitamà an’Andriaenañahare; fa mbe handriañeko, i fandrombaham-piatrefako naho Andrianañaharekoy.
Nʼchifukwa chiyani uli ndi chisoni iwe moyo wanga? Nʼchifukwa chiyani wakhumudwa iwe mʼkati mwanga? Khulupirira Mulungu, pakuti ndidzamutamandabe Iye, Mpulumutsi wanga ndi Mulungu wanga.