< Salamo 145 >
1 Sabo Fibangoañe. A i Davide Honjoneko irehe, ry Andrianañahareko, ry Mpanjaka, hibango ty tahina’o mb’an-jafe’afe’e.
Salimo la matamando la Davide. Ndidzakukwezani Mulungu wanga, Mfumu yanga; ndidzatamanda dzina lanu ku nthawi za nthawi.
2 Handriañeko boak’ andro, le hibango ty tahina’o nainai’e donia.
Ndidzakutamandani tsiku ndi tsiku ndi kulemekeza dzina lanu ku nthawi za nthawi.
3 Hinakinake t’Iehovà, rengèñe añ’abo, tsy taka-tsikaraheñe ty hajabahina’e.
Yehova ndi wamkulu ndi woyenera matamando onse; ukulu wake palibe angawumvetsetse.
4 Ho bangoe’ ty tariratse raik’ ami’ty ila’e o tolon-draha’oo; naho hitaroñe o fitoloña’o jabajabao.
Mʼbado wina udzayamikira ntchito yanu kwa mʼbado wina; Iwo adzafotokoza za machitidwe anu amphamvu.
5 Ty ha’raelahim-bolonahe’ ty enge’o vaho o tolon-draha’o mahalatsao ro fitsakoreako.
Adzayankhula ulemerero wokongola waufumu wanu, ndipo ine ndidzalingalira za ntchito zanu zodabwitsa.
6 Ho talilie’ ondatio ty haozaram-panoe’o mampañeveñe, vaho ho taroñeko ty hajabahina’o.
Iwo adzafotokoza za mphamvu ya ntchito zanu zoopsa kwambiri, ndipo ine ndidzalengeza za ntchito zanu zazikulu.
7 Ho talilie’ iereo ty fitiahiañe o havokaran-kasoa’o; hirebeha’ iereo ty havantaña’o.
Adzakondwerera kuchuluka kwa ubwino wanu, ndi kuyimba mwachimwemwe za chilungamo chanu.
8 Matarike t’Iehovà, naho lifo-tretrè, malaon-kaviñerañe vaho lifo-piferenaiñañe.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo, wosakwiya msanga ndi wodzaza ndi chikondi chosasinthika.
9 Kila hasoà’ Iehovà; ambone’ ze hene anoe’e o fitretreza’eo.
Yehova ndi wabwino kwa onse; amachitira chifundo zonse zimene anazipanga.
10 Fonga handrenge Azo o tolon-draha’oo, ry Iehovà; vaho hañonjoñe Azo o noro’oo.
Zonse zimene munazipanga zidzakutamandani, Inu Yehova; oyera mtima adzakulemekezani.
11 Ho saontsie’ iereo ty volonahem-pifehea’o, vaho hitalily o haozara’oo,
Iwo adzafotokoza za ulemerero wa ufumu wanu ndi kuyankhula za mphamvu yanu,
12 hampandrendreke o ana’ ondatio o fitoloña’e ra’elahio, naho ty hafanjàka’ ty enge’ i fifehea’ey.
kuti anthu onse adziwe za machitidwe anu amphamvu ndi ulemerero wokongola wa ufumu wanu.
13 Fifeheañe tsy modo ty fifehea’o, naho manitsike o tariratse iabio ty fameleha’o.
Ufumu wanu ndi ufumu wamuyaya, ndipo ulamuliro wanu ndi wosatha pa mibado yonse. Yehova ndi wokhulupirika pa malonjezo ake onse ndi wokonda zonse zimene Iye anazipanga.
14 Songa tohaña’ Iehovà o mikorovokeo, sindre atroa’e o mibokok’ ambaneo.
Yehova amagwiriziza onse amene akugwa ndipo amakweza onse otsitsidwa.
15 Kila fihaino miandrandra ama’o, vaho anjotsoa’o mahakama an-tsa’e.
Maso a onse amayangʼana kwa Inu, ndipo Inu mumawapatsa chakudya chawo pa nthawi yoyenera.
16 Manoka-pitàn-drehe mañeneke ty fañiria’ ze hene raha veloñe.
Mumatsekula dzanja lanu ndi kukwaniritsa zokhumba za chamoyo chilichonse.
17 Vantañe amo lala’e iabio t’Iehovà naho matarik’ amy ze hene fitoloña’e.
Yehova ndi wolungama mʼnjira zake zonse, ndi wokonda zonse zimene anazipanga.
18 Marine’ ze mikanjy aze iaby t’Iehovà; ze hene mikanjy aze an-katò.
Yehova ali pafupi ndi onse amene amamuyitana, onse amene amamuyitana Iye mʼchoonadi.
19 Ho henefa’e ty fisalalà’ o mañeveñe ama’eo; ho janjiñe’e ka ty toreo’ iareo vaho ho rombahe’e.
Iye amakwaniritsa zokhumba za iwo amene amamuopa; amamva kulira kwawo ndi kuwapulumutsa.
20 Ambena’ Iehovà ze hene mikoko aze, fe fonga ho rotsahe’e o lo-tserekeo.
Yehova amayangʼana onse amene amamukonda koma adzawononga anthu onse oyipa.
21 Hivolam-pandrengeañe am’ Iehovà ty vavako, le kila nofotse ro hibango ty tahina’e masiñe nainai’e donia.
Pakamwa panga padzayankhula zotamanda Yehova. Cholengedwa chilichonse chitamande dzina lake loyera ku nthawi za nthawi.