< Salamo 139 >
1 Ho a i Talè, Sabo’ i Davide. Ry Iehovà, fa nitsikarahe’o iraho, mbore arofoana’o.
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mwandisanthula ndipo mukundidziwa.
2 Arofoana’o ty fitobohako naho ty fiongahako; oni’o ty ereñeren-troko ndra te tsietoitàne añe.
Inu mumadziwa pamene ndikhala pansi ndi pamene ndidzuka; mumazindikira maganizo anga muli kutali.
3 Vandroñe’o o liakoo, naho o fandreakoo; hene arofoana’o o lalakoo.
Mumapenyetsetsa pamene ndikutuluka ndi kugona kwanga; mumadziwa njira zanga zonse.
4 Ie mbe tsy an-delako ao ty fivolako, Hete! ry Iehovà, kila arofoana’o.
Mawu asanatuluke pa lilime langa mumawadziwa bwinobwino, Inu Yehova.
5 Nifahera’o raho— aolo eo naho amboho ao; vaho nisazoha’o fitàñe.
Mumandizinga kumbuyo ndi kutsogolo komwe; mwasanjika dzanja lanu pa ine.
6 Loho fanjàka amako i hilala zay, abo, tsy takako.
Nzeru zimenezi ndi zopitirira nzeru zanga, ndi zapamwamba kuti ine ndizipeze.
7 Aia ty hombako hisitak’ amy Arofo’oy? Aia ty hibotitsihako o lahara’oo?
Kodi ndingapite kuti kufuna kuzemba Mzimu wanu? Kodi ndingathawire kuti kuchoka pamaso panu?
8 Ie mionjom-b’an-dikerañe mb’eo iraho, eo irehe; naho alafiko an-kerakerak’ ao ty fandreako, hehe t’ie eo; (Sheol )
Ndikakwera kumwamba, Inu muli komweko; ndikakagona ku malo a anthu akufa, Inu muli komweko. (Sheol )
9 Ie rambeseko o ela’ i maraiñeio, naho mitoetse añ’ olon-driake tsietoitane añe,
Ngati ndiwulukira kotulukira dzuwa, ngati ndikakhala ku malekezero a nyanja,
10 eo ka ty hitehafam-pità’o ahy, naho hanazok’ ahiko ty fità’o havana.
kumenekonso dzanja lanu lidzanditsogolera, dzanja lanu lamanja lidzandigwiriziza.
11 Ie anoeko ty hoe, Toe hanafotse ahy ty ieñe, vaho hivalike ho haleñe ty hazavàñe amako,
Ndikanena kuti, “Zoonadi, mdima udzandibisa ndithu ndipo kuwunika kukhale mdima mondizungulira,”
12 Fe ndra o hamoromoroñañeo ro tsy maieñe ama’o, mireandreañe hoe i àndroy ty haleñe, hàmbañe ty hazavàñe naho ty ieñe.
komabe mdimawo sudzakhala mdima kwa Inu; usiku udzawala ngati masana, pakuti mdima uli ngati kuwunika kwa Inu.
13 Tsinene’o o añovakoo; nanenoñ’ ahy an-tron-dreneko ao.
Pakuti Inu munalenga za mʼkati mwanga; munandiwumba pamodzi mʼmimba mwa amayi anga.
14 Andriañeko irehe, fa an-karevendreveñañe naho halatsàñe ty nitsene’o ahiko; fanjàka o satam-pità’oo, toe apota’ ty fiaiko.
Ndimakuyamikani chifukwa ndinapangidwa mochititsa mantha ndi modabwitsa; ntchito zanu ndi zodabwitsa, zimenezi ndimazidziwa bwino lomwe.
15 Tsy nietak’ ama’o o taolakoo, ie nanoeñe an-kafitse ao, naho nitseneñe an-kahimbañe an-kalalefan-tane ao,
Mapangidwe anga sanabisike pamaso panu pamene ndimapangidwa mʼmalo achinsinsi, pamene ndinkawumbidwa mwaluso mʼmimba ya amayi anga.
16 Nivazohom-pihaino’o o nanoeñe ahikoo, naho nipatereñe amy boke’oy ze hene andro norizañe ho ahy, ie mboe tsy teo ty raike.
Maso anu anaona thupi langa lisanawumbidwe. Masiku onse amene anapatsidwa kwa ine, analembedwa mʼbuku lanu asanayambe nʼkuwerengedwa komwe.
17 Miheotse amako o fivetsevetse’oo ry Andrianañahare! Mienene t’ie mitraoke!
Zolingalira zanu pa ine ndi zamtengowapatali, Inu Mulungu, ndi zosawerengeka ndithu!
18 Ie imaneako iake, le andikoara’e ty ia’ o faseñeo. ie tsekake, le mbe ama’o eo.
Ndikanaziwerenga, zikanakhala zochuluka kuposa mchenga; pamene ndadzuka, ndili nanube.
19 Ehe ohoño loza o lo-tserekeo, ry Andrianañahare! Mihankàña amako arè, ry ondaty mpampiori-dioo,
Ndi bwino mukanangopha anthu oyipa, Inu Mulungu! Chokereni inu anthu owononga anzanu!
20 Injè’ iareo an-keloke irehe, manoñoñe Azo tsy vente’e o malaiñ’Azoo;
Amayankhula za Inu ndi zolinga zoyipa; adani anu amagwiritsa ntchito dzina lanu molakwika.
21 Tsy hejeko hao o tsy tea azoo, ry Iehovà? Tsy hifangantoreko hao o miatreatre ama’oo?
Kodi ine sindidana nawo amene amakudani, Inu Yehova? Kodi sindinyansidwa nawo amene amakuwukirani?
22 Toe hejeko am-palai-mena; fonga volilieko ho rafelahiko.
Ndimadana nawo kwathunthu; ndi adani anga.
23 Tsikaraho iraho, ry Andrianañahare, arofoano ty troko; tsoho vaho arendreho o fitsakoreakoo.
Santhuleni, Inu Mulungu ndipo mudziwe mtima wanga; Yeseni ndipo mudziwe zolingalira zanga.
24 Vazoho, he amako ao ty fiolañe, vaho iaolò mb’an-dalañe nainai’e mb’eo.
Onani ngati muli mayendedwe aliwonse oyipa mwa ine, ndipo munditsogolere mʼnjira yanu yamuyaya.