< Salamo 106 >
1 Treño t’Iehovà; andriaño t’Iehovà, amy te Ie ro soa; nainai’e ty fiferenaiña’e.
Tamandani Yehova. Yamikani Yehova chifukwa ndi wabwino; pakuti chikondi chake ndi chosatha.
2 Ia ty mahatalily o sata fanjaka’ Iehovào? ndra hahafitsey o enge’e iabio?
Ndani angathe kufotokoza za ntchito zamphamvu za Yehova kapena kumutamanda mokwanira?
3 Haha ze mahafiambeñe ty hatò, naho mitolom-panao ty fahiti’e.
Odala ndi amene amasunga chilungamo, amene amachita zolungama nthawi zonse.
4 Tiahio iraho, ry Iehovà, naho isohe’o ondati’oo; itiliho amy fandrombaha’oy.
Mundikumbukire Yehova, pamene mukuonetsa kukoma mtima kwanu kwa anthu anu, bwerani mudzandithandize pamene mukuwapulumutsa iwo,
5 Hahatreavako ty firaoraoa’ o jinobo’oo, hirebeke ami’ty hafalea’ i fifehea’oy, hitrao-pitreñañe amy lova’oy.
kuti ndidzasangalale ndi chuma cha anthu anu osankhika, kuti ndidzakhale nacho chimwemwe cha anthu anu ndi kukhala pamodzi ndi cholowa chanu pa kukutamandani.
6 Nindre nandilatse amo roae’aio zahay; nanao hakeo, nitolon-karatiañe.
Ife tachimwa monga momwe anachitira makolo athu; tachita zolakwa ndipo tachita moyipa.
7 Tsy nihaoñe’ o rae’ay e Mitsraimeo o halatsà’oo; tsy nitiahi’ iereo o fiferenaiña’o vokatseo, te mone niola amy Abo Tiañe, an-dRiake Mena añe.
Pamene makolo athu anali mu Igupto, sanalingalire za zozizwitsa zanu; iwo sanakumbukire kukoma mtima kwanu kochuluka, ndipo anawukira Inu pa Nyanja Yofiira.
8 Fe rinomba’e ty amy tahina’ey, hampaharofoana’e ty haozara’e.
Komabe Iye anawapulumutsa chifukwa cha dzina lake, kuti aonetse mphamvu zake zazikulu.
9 Trinevo’e i Riake Menay, le nimaike, vaho niaoloa’e, nitoañe o lalekeo hoe te fatram-bey.
Anadzudzula Nyanja Yofiira, ndipo inawuma; anawatsogolera mʼnyanja yakuya ngati akuyenda mʼchipululu.
10 Le rinomba’e boak’an-taña’ i malaiñe iareoy, naho jineba’e am-pità’ i rafelahiy.
Anawapulumutsa mʼdzanja la amaliwongo; anawawombola mʼdzanja la mdani.
11 Nopoe’ i ranoy o rafelahi’eo; tsy nanisàñe honka’e.
Madzi anamiza adani awo, palibe mmodzi wa iwo anapulumuka.
12 Aa le natokisa’ iareo o tsara’eo, nisaboeñe ty enge’e.
Kenaka iwo anakhulupirira malonjezo ake ndi kuyimba nyimbo zamatamando.
13 Fe nihaliño’ iereo anianike o sata’eo tsy nahaliñe o famerea’eo.
Koma posachedwa anayiwala zimene Iye anachita, ndipo sanayembekezere uphungu wake.
14 Le niazo’ ty hasiji-mena an-jerezere tane añe; nazizi’ iereo am-babangoañe ao t’i Andrianañahare.
Mʼchipululu, anadzipereka ku zilakolako zawo; mʼdziko lopanda kanthu anayesa Mulungu.
15 Aa le nitolora’e i nihalalie’ iereoy, fe nañiraha’e haborokàñe ty fiai’iereo.
Choncho Iye anawapatsa chimene anapempha, koma anatumiza nthenda yowondetsa.
16 Ie nitsikirike i Mosè an-tobe ao, naho i Aharone navahe’ Iehovày,
Mʼmisasa, anachitira nsanje Mose ndi Aaroni, amene Yehova anadzipatulira.
17 le nisokake i taney niteleñe i Datane; naho nandembeke ty fehe’ i Abirame.
Nthaka inatsekuka ndipo inameza Datani; inakwirira gulu la Abiramu.
18 Nisolebare’ ty afo añivo’ i rimboñey; niforototoe’ i firebarebàñey o tsivokatseo.
Moto unayaka pakati pa otsatira awo; lawi lamoto linapsereza anthu oyipa.
19 Nitsene bania e Korebe añe iereo, naho nilokoloko amy sare trinanakey;
Iwo anapanga mwana wangʼombe pa Horebu ndi kulambira fano loyengedwa kuchokera ku chitsulo.
20 aa le natakalo’ iereo sare bania mivazakota ahetse, ty engen’ Añahare.
Anasinthanitsa ulemerero wawo ndi fano la ngʼombe yayimuna imene imadya udzu.
21 Nihaliño’ iereo t’i Andrianañahare mpandrombake iareo, I nanao raha fanjàka e Mitsraimey,
Anayiwala Mulungu amene anawapulumutsa, amene anachita zinthu zazikulu mu Igupto,
22 raha tsitantane an-tane’ i Kame vaho raha naharevendreveñe an-dRiake Mena añe.
zozizwitsa mʼdziko la Hamu ndi machitidwe ake woopsa pa Nyanja Yofiira.
23 Aa le nanao ty hoe t’ie harotsa’e: naho tsy te nijohañe an-jebañe añatrefa’e eo t’i Mosè jinobo’e, nampivioñe i haviñera’ey tsy hanjamana’e.
Choncho Iye anawawuza kuti adzawawononga, pakanapanda Mose, mtumiki wake wosankhidwa, kuyima pamaso pake, ndi kuletsa mkwiyo wake kuti usawawononge.
24 Niheje’ iereo amy zao i tane nirieñey; tsy natokisañe o tsara’eo,
Motero iwo ananyoza dziko lokoma; sanakhulupirire malonjezo ake.
25 f’ie niñeoñeoñe an-kijà ao, tsy hinao’ iereo ty fiarañanaña’ Iehovà.
Anangʼungʼudza mʼmatenti mwawo ndipo sanamvere Yehova.
26 Aa le nifanta te hampikorovohe’e an-jerezere tane ao,
Kotero Iye analumbira atakweza dzanja lake, kuti adzachititsa kuti iwowo afere mʼchipululu,
27 naho havarakai’e amo fifeheañeo ty tarira’ iareo vaho haparatsà’e amo taneo.
kuchititsa kuti zidzukulu zawo zifere pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwabalalitsa mʼdziko lonse.
28 Mbore nireketse amy Baale-Peore iereo vaho nampibotseke haneñe nisoroñañe an-dolo.
Iwo anayamba kupembedza Baala-Peori ndi kudya nsembe zoperekedwa kwa milungu yopanda moyo;
29 Aa le nampiviñere’ iereo amo fitoloña’ iareoo, vaho natorotosi’e an-kiria.
anaputa mkwiyo wa Yehova pa machitidwe awo oyipa, ndipo mliri unabuka pakati pawo.
30 Niongak’ amy zao t’i Pinekase le nijebañe, vaho nisebañeñe i angorosiy.
Koma Finehasi anayimirira ndi kulowererapo, ndipo mliri unaleka.
31 Nivolilien-ko havañonañe ama’e zay. ho a ze hene tarira’e mifandimbeo.
Chimenechi ndicho chinayesedwa chilungamo chake, kwa mibado yosatha imene ikubwera.
32 Nampiviñera’ iareo ka amo rano mpilie-drokoñeo, le niazom-boiñe ty am’iereo t’i Mosè;
Pa madzi a ku Meriba iwo anakwiyitsa Yehova ndipo mavuto anabwera kwa Mose chifukwa cha anthuwo,
33 amy t’ie nikai-jaka amy arofo’ey, le kamaike ty niakatse am-pivimbi’e ao.
pakuti iwowo anawukira mzimu wa Mulungu, ndipo pa milomo ya Mose panatuluka mawu osayenera.
34 Tsy nifongore’ iareo ondatio, amy nandilia’ Iehovà hanoeñey,
Aisraeliwo sanawononge mitundu ya anthu monga momwe Yehova anawalamulira.
35 Te mone nifañaoñe amo kilakila‘ndatio naho nizatse o sata’eo,
Koma anasakanizana ndi anthu a mitundu inayo ndi kuphunzira miyambo yawo.
36 naho nitoroñe o saren-drahare’eo ze nanjare fandrik’ am’ iereo,
Ndipo anapembedza mafano awo, amene anakhala msampha kwa iwowo.
37 naho nasoro’ iereo amo kokolampao o anadahi’iareoo naho o anak’ ampela’iareoo,
Anapereka nsembe ana awo aamuna ndi ana awo aakazi kwa ziwanda.
38 vaho nampiorike lio-maliñe, ty lion’ anadahy naho anak’ampela, ie nasoro’ iereo amo saren-drahare’ i Kanànao, vaho vinetan-dio i taney.
Anakhetsa magazi a anthu osalakwa, magazi a ana awo aamuna ndi a ana awo aakazi, amene anawapereka nsembe kwa mafano a ku Kanaani, ndipo dziko linayipitsidwa ndi magazi awo.
39 Aa le nihativa am-pitoloñañe, nañarapilo amo fisafiria’iareoo.
Iwo anadzidetsa okha ndi zimene anachita; ndi machitidwe awo amakhala ngati munthu wachigololo.
40 Toly ndra niviañe am’ondatio ty haviñera’ Iehovà, vaho niheje’e i lova’ey.
Tsono Yehova anakwiya ndi anthu ake ndipo ananyansidwa ndi cholowa chake.
41 Natolo’e am-pità’ o fifeheañeo iereo, hifehea’ o rafelahi’eo.
Iye anawapereka kwa anthu a mitundu ina, ndipo adani awo anawalamulira.
42 Niforekeke’ o nifankalaiñe am’iereoo le nareke ambane’ fità’iareo.
Adani awo anawazunza ndi kuwakhazika pansi pa mphamvu yawo.
43 Beteke rinomba’e, f’ie nizehatse an-tsafiry, vaho nilempotse an-kakeo.
Iye ankawapulumutsa nthawi zambiri, koma iwo ankatsimikiza za kuwukira ndipo anawonongeka mʼmachimo awo.
44 Ie nivazoho’e ty falovilovi’ iareo, naho jinanji’e o fitoreova’ iareoo,
Koma Iye anaona kuzunzika kwawo pamene anamva kulira kwawo;
45 le nitiahi’e ty am’ iereo i fañina’ey naho niselekaiñe, ty amo hene fiferenaiña’eo;
Chifukwa cha iwo Iye anakumbukira pangano lake ndipo anawalezera mtima chifukwa cha kukula kwa chikondi chake.
46 ie nampitretreze’e amo nanese iareo am-pandrohizañeo.
Iye anachititsa kuti amene anawagwira iwo ukapolo awamvere chisoni.
47 Rombaho zahay ry Iehovà Andrianañahare’ay, vaho atontono boak’ amo fifeheañeo, hañandriaña’ay ty tahina’o masiñe, vaho hitreñe amo enge’oo.
Tipulumutseni Inu Yehova Mulungu wathu, ndipo mutisonkhanitse kuchoka kwa anthu a mitundu ina kuti tithe kuyamika dzina lanu loyera ndi kunyadira mʼmatamando anu.
48 Andriañeñe t’Iehovà, Andrianañahare’ Israele, boak’an-kaehae’e pak’an-kaehae’e; vaho hene hiredoñe ami’ty hoe ondatio: Ie Izay, Treño t’Ià.
Atamandike Yehova, Mulungu wa Israeli, Kuyambira muyaya mpaka muyaya. Anthu onse anene kuti, “Ameni!” Tamandani Yehova.