< Nehemia 11 >

1 Toe nimoneñe e Ierosalaime ao o mpifehe’ ondatio, le nifanendre an-kitsapake ka ondaty ila’eo, ty haneseañe ty raik’ ami’ty folo ho mpimoneñe e Ierosa­laime an-drova miavak’ ao vaho apok’ amo rova ila’eo ty sive.
Nthawi imeneyo atsogoleri a anthu ankakhala ku Yerusalemu. Tsono anthu ena onse anachita maere kuti apeze munthu mmodzi pa anthu khumi aliwonse kuti azikhala ku Yerusalemu, mzinda wopatulika. Anthu asanu ndi anayi otsalawo ankakhala mʼmidzi yawo.
2 Le nitatàe’ ondaty iabio o lahilahy nanolo-batañe himoneñe e Ierosalaimeo.
Anthu anayamikira onse amene anadzipereka kuti azikhala mu Yerusalemu.
3 Irezao o mpiaolo’ i borizà nimoneñe e Ierosalaimeoy, fe songa nimoneñe am-panaña’e amo rova’ Iehodao o nte-Israeleo, o mpisoroñeo naho o nte-Levio naho o mpitoroñ’ anjombao vaho o anam-pitoro’ i Selomòo.
Aisraeli wamba, ansembe, Alevi, ogwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu ndiponso zidzukulu za antchito a Solomoni ankakhala mʼmidzi yawo, aliyense mu dera lake. Koma atsogoleri a chigawo cha Yuda anali atakhazikika mu Yerusalemu.
4 E Ierosalaime ao ty nimoneña’ ty ila’ o nte-Levio naho o ana’ i Beniamineo. Amo ana’ Iehodao: i Ataià, ana’ i Ozià, ana’ i Zekarià, ana’ i Amarià, ana’ i Sefatià, ana’ i Mahalalile, amo tarira’ i Peretseo;
Ku Yerusalemu kunkakhalanso anthu ena a mafuko a Yuda ndi Benjamini. Ena mwa zidzukulu za Yuda ndi awa: Ataya, mwana wa Uziya, mwana wa Zekariya, mwana wa Amariya mwana wa Sefatiya, mwana wa Mahalaleli. Onsewa anali ana a Perezi.
5 naho i Maaseià, ana’ i Baroke, ana’ i Kolkozè, ana’ i Kazaià, ana’ i Adaià, ana’ Ioroaribe, ana’ i Zekarià, ana’ i nte-Siloney.
Ena ndi awa: Maaseya mwana wa Baruki, mwana wa Koli-Hoze mwana wa Hazaya, mwana wa Adaya, mwana wa Yowaribu, Zekariya mwana wa Msiloni.
6 O hene ana’ i Peretse nimo­neñe e Iero­sa­laimeo: lahilahy maozatse efa-jato-tsi-enempolo-valo’amby.
Zidzukulu zonse za Perezi, anthu amphamvu zawo amene ankakhala ku Yerusalemu analipo anthu okwanira 468.
7 Irezao o ana’ i Beniamineo: i Salò, ana’ i Mesolame, ana’ Ioede, ana’ i Pe­daià, ana’ i Kolaià, ana’ i Maaseià, ana’ Itiele, ana’ Iesaià.
Nazi zidzukulu za Benjamini: Salu mwana wa Mesulamu, mwana wa Yowedi, mwana wa Pedaya, mwana wa Kolaya, mwana wa Maaseiya, mwana wa Itieli, mwana wa Yesaiya.
8 Nanonjohy aze t’i Gabay, i Salay, sivan-jato-tsi-roapolo-valo’ amby.
Abale ake anali Gabayi ndi Salaya. Onse pamodzi anali 928.
9 Le Ioele ana’ i Zikrý ty nimpisary iareo; vaho nimpifehe faharoe’ i rovay t’Ie­hoda ana’ i Hasenoà.
Yoweli mwana wa Zikiri ndiye anali mtsogoleri wawo, ndipo Yuda mwana wa Hasenuya ndiye amayangʼanira chigawo cha chiwiri cha mzinda.
10 Amo mpisoroñeo: Iedaià, ana’ Ioiaribe, Iakine,
Ansembe anali awa: Yedaya mwana wa Yowaribu; Yakini;
11 i Seraià, ana’ i Kilkià, ana’ i Mesolame, ana’ i Tsadoke, ana’ i Meraiote, ana’ i Akitobe, mpifehen’ anjomban’ Añahare,
Seraya mwana wa Hilikiya mwana wa Mesulamu, mwana wa Zadoki, mwana wa Merayoti, mwana wa Ahitubi amene anali woyangʼanira Nyumba ya Mulungu,
12 le o rahalahi’ iareo mpitoloñe amy anjombaio: valon-jato-tsi-roapolo-ro’amby; naho Adaià, ana’ Ierokame, ana’ i Pelalià, ana’ i Amtsý, ana’ i Zekarià, ana’ i Paskore, ana’ i Malkiià,
ndi abale awo, amene ankagwira ntchito ku Nyumba ya Mulungu. Onse pamodzi anali 822. Panalinso Adaya mwana wa Yerohamu, mwana wa Pelaliya, mwana wa Amizi, mwana wa Zekariya, mwana wa Pasi-Huri, mwana wa Malikiya,
13 naho o rahalahi’eo, talèn’ anjomban-droae: roan-jato-tsi-efapolo ro’amby naho i Amassay, ana’ i Azarele, ana’ i Akzay, ana’ i Mesilemote, ana’ Imere,
ndi abale ake, amene anali atsogoleri a mabanja. Onse pamodzi anali 242. Kuphatikiza apo panalinso Amasisai mwana wa Azaireli, mwana wa Ahazayi, mwana wa Mesilemoti, mwana wa Imeri
14 naho o rahalahi’e, lahindefo-maozatseo, zato-tsi-roapolo-valo’ amby, nisaria’ i Zabdiele ana’ o Hagadoleo.
ndi abale ake. Onse pamodzi anali 128 ndipo anali anthu olimba mtima kwambiri. Mtsogoleri wawo wamkulu anali Zabidieli mwana wa Hagedolimu.
15 Le amo nte-Levio: i Semaià, ana’ i Kasobe, ana’ i Azrikame, ana’ i Kasabià, ana’ i Boný;
Alevi anali awa: Semaya mwana wa Hasubu, mwana wa Azirikamu, mwana wa Hasabiya, mwana wa Buni.
16 naho i Sabetay naho Ioza­bade, amo mpiaolo nte-Levy mpisary o raha alafe’ i anjomban’Añahareio;
Sabetayi ndi Yozabadi anali atsogoleri amene ankayangʼanira ntchito ya kunja kwa Nyumba ya Mulungu.
17 naho i Matanià, ana’ i Mikà, ana’ i Zabdý, ana’ i Asafe mpiaolo, namototse ty fañandriañañe am-pitalahoañe naho i Bakbokià, ty faharoe amo rahalahi’eo; naho i Abdà, ana’ i Samoà, ana’ i Galale, ana’ Iedotone.
Mataniya mwana wa Mika, mwana wa Zabidi, mwana wa Asafu ndiye anali wotsogolera pa mapemphero achiyamiko. Panalinso Bakibukiya amene anali wachiwiri pakati pa abale ake. Kuwonjezera apo panalinso Abida mwana wa Samuwa, mwana wa Galali, mwana wa Yedutuni.
18 Le o nte-Levy an-drova masiñeo: niroan-jato-tsi-valom-polo-efats’ amby.
Alevi onse amene anali mu mzinda woyera analipo 284.
19 Le o mpañambeñeo, i Akobe, i Talmone naho o rahalahi’e mpigari-lalambeio: zato-tsi-fitompolo-ro’amby.
Alonda a ku Nyumba ya Mulungu anali awa: Akubu, Talimoni ndi abale awo. Onse pamodzi anali 172.
20 Le o sisa’ Israeleo, amo mpisoroñeo, amo nte-Levio, ze hene an-drova’ Iehoda añe, sindre am-panaña’e ao.
Aisraeli ena onse pamodzi ndi ansembe ndi Alevi ankakhala mʼmizinda ya Yuda, ndipo aliyense ankakhala mʼdera la makolo ake.
21 Fe nimoneñe e Ofele ao o mpitoroñ’ anjombao; i Tsikà naho i Gispà ty nimpisary o mpitoroñ’ anjombao.
Koma antchito a ku Nyumba ya Mulungu ankakhala pa phiri la Ofeli, ndipo Ziha ndi Gisipa ndiwo anali kuwayangʼanira.
22 Le ty nimpisari’ o nte-Levy e Ierosalaimeo t’i Ozý ana’ i Baný, ana’ i Kasabià, ana’ i Matanià, ana’ i Mika, amo ana’ i Asafeo, songa mpisabo mitoloñe añ’ anjomban’ Añaharey,
Wamkulu wa Alevi mu Yerusalemu anali Uzi mwana wa Bani, mwana wa Hasabiya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mika. Uzi anali mmodzi wa zidzukulu za Asafu, amene anali oyimba nyimbo pa nthawi zachipembedzo mʼNyumba ya Mulungu.
23 fa am’iereo ty lili’ i mpanjakay, ty fanohanañe o mpisaboo, ze ipaiañe boak’ andro.
Pakuti mfumu inalamula kuti tsiku ndi tsiku pa nthawi zachipembedzo oyimba nyimbowo azikhalapo.
24 Naho i Petakià, ana’ i Mesezabele, ana’ i Zerà, ana’ Iehodà ty tam-pità i mpanjakay ty amy ze nioza am’ ondatio.
Petahiya mwana wa Mesezabeli, mmodzi mwa zidzukulu za Zera mwana wa Yuda ndiye ankayimirira Aisraeli pa bwalo la mfumu ya Perisiya.
25 Le o tanàñe reketse teteke nimoneña’ ty ila’ o ana’ Ieho­daoo, e Kiriate-arba naho o tanà’eo naho e Dibone naho o tanà’eo vaho e Ie­kabe-zeele naho o tanà’eo;
Anthu ena a fuko la Yuda ankakhala ku Kiriyati-Ariba ndi midzi yake, ku Diboni ndi midzi yake, ku Yekabizeeli ndi midzi yake,
26 le e Iehosoa naho e Moladà vaho e Bete-pelete;
ku Yesuwa, Molada, Beti-Peleti,
27 naho e Katsare-saole naho e Beer-sevà rekets’ o tanà’eo
Hazari-Suwali, Beeriseba ndi midzi yawo.
28 naho e Tsiklage naho e Mekonà rekets’ o tanà’eo;
Ku Zikilagi, Mekona ndi midzi yawo,
29 naho e En-drimone naho e Tsorà naho e Iarmote;
ku Eni-Rimoni, Zora, Yarimuti,
30 e Zanoake, e Adolame naho o tanà’eo, e Lakise rekets’ o tete’ iareoo, e Azekà rekets’ o tanà’eo. Aa le nitobe mifototse e Beer-Sevà eo pak’ am-bavatane’ i Hinome eo iereo.
Zanowa, Adulamu ndi midzi yake, ku Lakisi ndi minda yake, ku Beeriseba mpaka ku chigwa cha Hinomu.
31 Le o ana’ i Beniamineo mifototse e Gibà, le e Mikmase naho e Aiià naho e Betele rekets’ o tanà’eo;
Nazonso zidzukulu za Benjamini zinkakhala mʼdera lawo kuyambira ku Geba mpaka ku Mikimasi, Ayiya, Beteli ndi midzi yake,
32 e Anatote, e Nobe, e Ananià;
ku Anatoti, Nobu ndi Ananiya,
33 e Kàtsore, e Ramà, e Gitaime;
ku Hazori, Rama ndi Gitaimu,
34 e Kadide, e Tseboime, e Nebalate;
ku Hadidi, Zeboimu ndi Nebalati,
35 e Lode naho e Ono naho am-bavatane’ o mpandrafitseo.
ku Lodi, Ono ndi ku chigwa cha Amisiri.
36 Le o nte-Levio; nampireketeñe amy Beniamine o firimboña’ Iehoda ila’eo.
Magulu ena a Alevi a ku Yuda ankakhala ku Benjamini.

< Nehemia 11 >