< Fitomaniana 2 >
1 Hedèy te nakopo’ i Talè an-drahoñe ao t’i Tsione amy haviñera’ey! Naretsa’e boak’ an-dikerañey pak’ an-tane eo ty hatsomerentsere’ Israele, vaho nandikofa’e ty fatimpaha’e amy androm-pifomboa’ey.
Haa, Ambuye waphimba mwana wamkazi wa Ziyoni ndi mtambo wa mkwiyo wake! Iye wataya pansi ulemerero wa Israeli kuchoka kumwamba. Pa tsiku la mkwiyo wake Iye sanakumbukirenso popondapo mapazi ake.
2 Fa nagedra’ i Talè tsy aman-tsehanga’e o kiboho’ Iakobeo, vaho tsy niferenaiña’e; fa nafetsa’e ambane eo o kijoly fatrats’ i anak’ ampela’ Iehodàio; ie nafotsa’e an-tane; tiniva’e i fifeheañey naho o roandria’eo.
Ambuye anawononga midzi yonse ya Yakobo mopanda chifundo; mu mkwiyo wake anagwetsa malinga a mwana wamkazi wa Yuda. Anagwetsa pansi mochititsa manyazi maufumu ndi akalonga ake.
3 Fa naitoa’e an-kaviñerañe mena ty tsifa’ Israele; nasita’e aolo’ i rafelahiy ty fità’e havana; vaho finorototo’e hoe afo misolebatse t’Iakobe, afo mangotomomoke mb’eo mb’eo.
Atakwiya kwambiri, Ambuye anathyola nyanga iliyonse ya Israeli. Anabweza dzanja lake lamanja pamene mdani anamuyandikira. Ambuye anatentha fuko la Yakobo ngati moto wonyeketsa umene umawononga zinthu zonse zomwe zili pafupi.
4 Nabitso’e hoe rafelahy ty fale’e, najado’e hoe ravetro ty fità’e, vaho zinama’e iaby ze nisoa am-pihaino; an-kivoho’ i anak’ampela’ i Tsioney ty nampidoandoaña’e ty haviñera’e hoe afo.
Wakokera uta wake pa ife ngati ndife adani; wayimiritsa dzanja lake pa ife ngati ndife adani, ndipo anapha onse amene tinkawayangʼana monyadira. Ukali wake ukuyaka ngati moto pa tenti ya mwana wamkazi wa Ziyoni.
5 Fa ninjare rafelahy t’i Talè henanekeo, fa nigenohe’e t’Israele; hene nabea’e o sokemitraha’eo, rinotsa’e o fipalirañe fatratseo; vaho nampitomboe’e amy anak’ampela’ Iehodày ty fangololoihañe naho fandalàñe.
Ambuye ali ngati mdani; wawonongeratu Israeli; wawonongeratu nyumba zake zonse zaufumu ndipo wawononga malinga ake. Iye wachulukitsa kubuma ndi kulira kwa mwana wamkazi wa Yuda.
6 Hinatsakatsa’e i kivoho’ey hoe t’ie nigoloboñe; nampiantoe’e i toem-pivori’e namotoañañey; nampahaliñoe’ Iehovà e Tsione ao o Famantañañeo naho o Sabatao, vaho ninjè’e ami’ty fitorifiha’ i fifomboa’ey i mpanjakay naho o mpisoroñeo.
Wagwetsa malo ake okhalamo ngati khumbi la mʼmunda; wawononga malo ake a msonkhano. Yehova wayiwalitsa Ziyoni maphwando ake oyikika ndi masabata ake. Mokwiya kwambiri, Iye ananyoza mfumu ndi wansembe.
7 Navokovoko’ i Talè i kitreli’ey, nampangorìñe Aze i toe’e niavakey; napo’e am-pitan-drafelahy o rindrin’ anjombao: ie nikorake añ’anjomba’ Iehovà ao, manahake te añ’androm-pivory miavake.
Ambuye wakana guwa lake la nsembe ndipo wasiya malo ake opatulika. Iye wapereka makoma a nyumba zake zaufumu kwa mdani wake; adaniwo anafuwula mʼnyumba ya Yehova ngati kuti ndi pa tsiku la chikondwerero.
8 Sinafiri’ Iehovà ty handrotsake ty kijoli’ i anak’ ampela’ i Tsioney; fa kinazazà’e ty taly, tsy nampoli’e ty fità’e tsy handrotsake; nampirovete’e iaby ty fahañe naho ty rindriñe; mitrao-pinìke iereo.
Yehova anatsimikiza kugwetsa makoma a mwana wamkazi wa Ziyoni. Anawayesa ndi chingwe ndipo sanafune kuleka kuwagwetsa. Analiritsa malinga ndi makoma; onse anawonongeka pamodzi.
9 Nalentek’ an-tane ao o lalam-bei’eo; fa rinotsa’e vaho pinoza’e o sikada’eo; songa an-tane tsy mitan-Kàke i mpanjaka’ey naho o roandria’eo; eka tsy manjo aroñaroñe boak’ am’ Iehovà o mpitoki’eo.
Zipata za Yerusalemu zalowa pansi; wathyola ndi kuwononga mipiringidzo yake. Mfumu ndi akalonga ake agwidwa ukapolo pakati pa mitundu ya anthu, palibenso lamulo, ndipo aneneri ake sakupeza masomphenya kuchokera kwa Yehova.
10 Mitozòke an-tane eo ty androanavi’ i Tsione, mijomohoñe, nampibobò deboke añ’ambone’eo; midian-gony am-baniañe; miondre-doha’ mb’an-tane o somondrara mieha’ i Tsioneo.
Akuluakulu a mwana wamkazi wa Ziyoni akhala chete pansi; awaza fumbi pa mitu yawo ndipo avala ziguduli. Anamwali a Yerusalemu aweramitsa mitu yawo pansi.
11 Milesa o masokoo ty amo ranomasoo, mioremeñe ty troko; fa nadoañe an-tane ty ateko, ty amy fandrotsahañe i anak’ampela’ ondatikoy, ty amo anak’ajajao naho o mpinono mitoirañe an-dalan-drovao;
Maso anga atopa ndi kulira, ndazunzika mʼmoyo mwanga, mtima wanga wadzaza ndi chisoni chifukwa anthu anga akuwonongeka, chifukwa ana ndi makanda akukomoka mʼmisewu ya mu mzinda.
12 Hoe iereo aman-drene, aia ty tsako naho ty divay? ie tsipike hoe mate an-dala’ i rovay ey ie midoañe añ’arañan-drene’e ao ty fiai’ iareo.
Anawo akufunsa amayi awo kuti, “Kodi tirigu ndi vinyo zili kuti?” pamene akukomoka ngati anthu olasidwa mʼmisewu ya mʼmizinda, pamene miyoyo yawo ikufowoka mʼmanja mwa amayi awo.
13 Akore ty havereko azo? Añoharako ami’ty inon-drehe ry anak’ ampela’ Ierosalaime? Ino ty hañirinkiriñako ama’o hañohòako azo, ry anak’ampela’ i Tsione? Fa mienene manahake i riakey ty fere’o, ia ty hahamelañe azo?
Ndinganene chiyani za iwe? Ndingakufanizire ndi chiyani, iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu? Kodi ndingakufanizire ndi yani kuti ndikutonthoze, iwe namwali wa Ziyoni? Chilonda chako ndi chozama ngati nyanja, kodi ndani angakuchiritse?
14 Nahaisak’ aroñarom-bande naho hagegeañe ho azo o mpitoki’oo; vaho tsy nabora’ iareo o tahi’oo, hampipoliañe azo boak’an-drohy ao, fa fetsen-dremborake ty niisa’ iareo, toe talim-pandroahañe.
Masomphenya a aneneri ako anali abodza ndi achabechabe. Iwo sanakupulumutse kuti usapite ku ukapolo poyika poyera mphulupulu zako. Mauthenga amene anakupatsa anali achabechabe ndi osocheretsa.
15 Songa miteha-pitañe ama’o ze miary eo; sindre mikosake naho mikofikofi-doha amy anak’ampela’ Ierosalaimey manao ty hoe: Itoy hao i rova nitokaveñe ty hoe: Fahafoniran-Kasoa Vintañe, ty firebeha’ ty tane-bey toiy?
Onse oyenda mʼnjira yako akukuwombera mʼmanja; akugwedeza mitu yawo ndi kukunyodola iwe mwana wamkazi wa Yerusalemu: “Kodi mzinda uja ndi uwu umene unkatchedwa wokongola kotheratu, chimwemwe cha dziko lonse lapansi?”
16 Nampidañadaña falie ama’o o fonga malaiñe azoo; mikosasàke naho mikodrìtse nife manao ty hoe: Fa nabean-tika; itoy ‘nio i andro nitaman-tikañey, fa tendreke, le isake.
Adani ako onse akutsekulira pakamwa ndi kukunyoza; iwo akunyogodola ndi kukukuta mano awo, ndipo akuti, “Tamumeza. Tsiku ili ndi lomwe timayembekezera; tili ndi moyo kuti tilione.”
17 Fa nanoe’ Iehovà i naereñere’ey; fa nihenefa’e i fetse najado’e añ’andro taoloy; fa naretsa’e ambane eo le tsy niferenaiña’e; vaho nampirebehe’e ama’o o rafelahi’oo; naonjo’e ty tsifa’ o malaiñ’azoo.
Yehova wachita chimene anakonzeratu; wakwaniritsa mawu ake, amene anatsimikiza kale lomwe. Wakuwononga mopanda chifundo, walola mdani kuti akondwere chifukwa cha kugwa kwako, wakweza mphamvu za adani ako.
18 Mitoreo añ’arofo amy Talè iereo: O ry kijoli’ i anak’ampela’ i Tsioney, ampikararaho ranomaso hoe sorotombake handro an-kaleñe; ko ampahazoe’o fiaiñe ty fañova’o; ko ampitofa’o o fihaino’oo.
Mitima ya anthu ikufuwulira Ambuye. Iwe khoma la mwana wamkazi wa Ziyoni, misozi yako itsike ngati mtsinje usana ndi usiku; usadzipatse wekha mpumulo, maso ako asaleke kukhetsa misozi.
19 Miongaha, mikoeaha te haleñe, ami’ty fiorota’ o fijilovañeo; adoaño ty arofo’o hoe rano añatrefan-dahara’ i Talè; añonjono fitañe ama’e ho ami’ty fiai’ o keleia’o mitoirañe ami’ty kerè an-doha o lalañeo iabio.
Dzuka, fuwula usiku, pamene alonda ayamba kulondera; khuthula mtima wako ngati madzi pamaso pa Ambuye. Kweza manja ako kwa Iye chifukwa cha miyoyo ya ana ako, amene akukomoka ndi njala mʼmisewu yonse ya mu mzinda.
20 Hehe ry Iehovà biribirio: ia o nanoa’o o raha zaoo? Habotse’ o rakembao hao o tolin-tsabo’eo? o ajaja otroñe’e am-pitàñeo? Ho zamaneñe an-toe’ i Talè miavak’ ao hao ty mpisoroñe naho ty mpitoky?
Inu Yehova, onani, ndipo ganizirani: kodi ndani amene mwamuchitirapo zinthu ngati izi? Kodi amayi adye ana awo, amene amawasamalira? Kodi ansembe ndi aneneri awaphere mʼmalo opatulika a Ambuye?
21 Ty tora’e naho ty androanavi-bey, songa màndre an-tane an-dalañe eo; o somondrarakoo naho o ajalahikoo, fonga zinevo’ i fibaray; binaibai’o amy andron-kaviñera’oy zinama’o fa tsy niferenaiña’o.
Anyamata ndi okalamba aligone pamodzi pa fumbi la mʼmisewu ya mu mzinda; anyamata anga ndi anamwali anga aphedwa ndi lupanga. Inu Yehova mwawapha pa tsiku la mkwiyo wanu; mwawapha mopanda chifundo.
22 Kinoi’o hoe añ’androm- pivory miavake, o hekoheko miariseho ahikoo; vaho leo raike tsy nahabotatsake, tsy nanisañe amy andron-kaviñera’ Iehovày; o notroñekoo naho nibeizekoo ro fonga nabea’ i rafelahiy.
Ngati momwe mumayitanira pa tsiku la phwando, chimodzimodzinso mwandiyitanira zoopsa mbali zonse. Pa tsiku limene Yehova wakwiya palibe amene angathawe ndi kukhala ndi moyo; mdani wanga wawononga onse amene ndinkawasamala ndi kuwalera.