< Joela 3 >

1 Inao, hampoliko amy andro rezay, naho amy sa zay, ty fandrohiza’ Iehodà naho Ierosalaime,
“Masiku amenewo ndiponso nthawi imeneyo, nditadzabwezeretsanso Yerusalemu ndi Yuda mʼchimake,
2 naho hatontoko boak’ amy ze hene fifeheañe, naho hampizotsoeko mb’am-bavatane’ Iehosafate mb’eo, vaho eo ty himoahako an-jaka ty am’ ondatikoo naho i lovako Israeley, ie nampiba­ra­tsaheñe amo kilakila’ ondatio añe naho nanjarañe i tanekoy.
ndidzasonkhanitsa anthu a mitundu yonse ndipo ndidzawabweretsa ku Chigwa cha Yehosafati. Kumeneko ndidzawaweruza chifukwa cha cholowa changa, anthu anga Aisraeli, pakuti anabalalitsa anthu anga pakati pa mitundu ya anthu ndikugawa dziko langa.
3 Vinili’ iareo aman-kitsapake ondatikoo, kinalo’ iareo tsimirira ty ajalahy naho navaro’ iareo ty somondrara ho divay hinoma’ iareo.
Anagawana anthu anga pochita maere ndipo anyamata anawasinthanitsa ndi akazi achiwerewere; anagulitsa atsikana chifukwa cha vinyo kuti iwo amwe.
4 Inoñ’amako irehe Tsore naho Tsidone, naho ze hene toe’ i Pilisty? Hañavak’ amako hao? Aa naho Hañavake le hafoteko aniany naho masìka an-doha’ areo i ondro’ areoy,
“Kodi tsopano inu a ku Turo ndi Sidoni ndi madera onse a Filisitiya, muli ndi chiyani chotsutsana nane? Kodi mukundibwezera pa zinthu zimene ndakuchitirani? Ngati inu mukundibwezera, Ine ndidzabwezera zochita zanu mofulumira ndi mwachangu pa mitu yanu.
5 amy te tinava’ areo o volafotiko naho volamenakoo, naho nendese’ areo an-kibohon’drahare’ areo mb’eo o fànako sarotseo,
Pakuti munatenga siliva ndi golide wanga ndi kupita nacho chuma changa chamtengowapatali ku nyumba zanu zopembedzera mafano.
6 naho naleta’ areo amo nte-Ievanio o ana’ Iehodào naho o ana’ Ierosalaimeo haneseañe iareo lavitse ty tane’ iareo añe.
Inu munagulitsa anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kwa Agriki, kuti apite kutali ndi malire a dziko lawo.
7 Inao fa hampionjoneko boak’ an-tane nandetahañe iareo, vaho havàhako an-doha’ areo o sata’ areoo,
“Taonani, Ine ndidzawachotsa kumalo kumene munawagulitsako, ndipo ndidzabwezera zimene mwachita pa mitu yanu.
8 fa haletako am-pità’ o ana’ Iehodào o ana-dahi’ areoo naho o anak’ ampela’ areoo, vaho haleta’ iereo amo nte-Sevào, ondaty tsietoitane añeo, fa izay ty tsinara’ Iehovà.
Ndidzagulitsa ana anu aamuna ndi ana anu aakazi kwa anthu a ku Yuda, ndipo iwo adzawagulitsa kwa Aseba, mtundu wa anthu okhala kutali.” Yehova wayankhula.
9 Tseizo ty hoe amo kilakila’ondatio: Mihentseña hialy; tsekafo o fanalolahio, ampañarineo ze hene lahindefoñe; ampionjono mb’etoa;
Lengezani izi pakati pa anthu a mitundu ina: Konzekerani nkhondo! Dzutsani ankhondo amphamvu! Asilikali onse afike pafupi ndipo ayambe nkhondo.
10 Tefeo ho fibara o lelan-dasarì’ areoo, naho ho lefoñe o fibira’ areoo, ampanò ty hoe o mavozoo: Maozatse iraho;
Sulani makasu anu kuti akhale malupanga ndipo zikwanje zanu zikhale mikondo. Munthu wofowoka anene kuti, “Ndine wamphamvu!”
11 Malisà! mb’etoy ry kilakila’ ondaty mañohokeo; ampizotsò o fanalolahi’oo ry Iehovà.
Bwerani msanga, inu anthu a mitundu yonse kuchokera ku mbali zonse, ndipo musonkhane kumeneko. Tumizani ankhondo anu Yehova!
12 Mitrobotroboa ry kilakila ondatio, mionjona mb’am-bavatane’ Iehosefate eo. fa eo ty hitobohako hizaka o kilakila ondaty miarisehoo.
“Mitundu ya anthu idzuke; ipite ku Chigwa cha Yehosafati, pakuti kumeneko Ine ndidzakhala ndikuweruza anthu a mitundu yonse yozungulira.
13 Sonjono ty fitatahañe, fa matoe i vokatsey, miziliha, mandialià, fa pea i fipiritañey, naho mandopatse o sajoao, fa bey ty haloloa’ iareo.
Tengani chikwakwa chodulira tirigu, pakuti mbewu zakhwima. Bwerani dzapondeni mphesa, pakuti mopsinyira mphesa mwadzaza ndipo mitsuko ikusefukira; kuyipa kwa anthuwa nʼkwakukulu kwambiri!”
14 Rehoreho, fikorakorahañe ty am-bavatanem-panàmpan-kevetse, fa mitotoke ty andro’ Iehovà am-bavatanem-panàmpan-kevetse.
Chigulu cha anthu, chigulu cha anthu, mʼchigwa cha chiweruzo! Pakuti tsiku la Yehova layandikira mʼchigwa cha chiweruzo.
15 Hampaieñeñe i àndroy naho i volañey, vaho hasinta’ o vasiañeo o filoeloea’eo.
Dzuwa ndi mwezi zidzadetsedwa, ndipo nyenyezi sizidzawalanso.
16 Le hitroñe boak’e Tsione ao t’Iehovà, hampipoña-piarañanañañe boak’e Ierosalaime ao; le hihondrahondra o likerañeo naho ty tane toy; fa fitamà’ ondati’eo t’Iehovà naho ty fipalira-maoza’ o ana’ Israeleo.
Yehova adzabangula kuchokera mu Ziyoni ndipo mawu ake adzamveka ngati bingu kuchokera mu Yerusalemu; dziko lapansi ndi thambo zidzagwedezeka. Koma Yehova adzakhala pothawira pa anthu ake, linga la anthu a ku Israeli.
17 Aa le ho fohi’ areo te Izaho Iehovà Andrianañahare’ areo, mpimoneñe e Tsione, vohi-masiko, ao, aa le hiavake t’Ierosalaime, vaho tsy hiranga ama’e ka o ambahinio.
“Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine Yehova Mulungu wanu, ndimakhala mu Ziyoni, phiri langa lopatulika. Yerusalemu adzakhala wopatulika; alendo sadzamuthiranso nkhondo.
18 Ie amy andro zay, hampitsopatsopake divay vao o vohitseo, le horikorihen-dronono o haboañeo, naho hene hikararahan-drano o saka’ Iehodào, le higoangoañe boak’ añ’anjomba’ Iehovà ao ty rano hanondrake ty vavatane’ i Sitime.
“Tsiku limenelo mapiri adzachucha vinyo watsopano, ndipo zitunda zidzayenderera mkaka; mitsinje yonse ya ku Yuda idzadzaza ndi madzi. Kasupe adzatumphuka mʼnyumba ya Yehova ndipo adzathirira Chigwa cha Sitimu.
19 Ho babangoañe t’i Mitsraime, naho ho ratrotratro bangý t’i Edome, ty amy hasiaha’ iareo amo ana’Iehodào, ie nampiorike lio-màliñe an-tane’ iareo eo.
Koma Igupto adzasanduka bwinja, Edomu adzasanduka chipululu, chifukwa cha nkhondo imene anathira anthu a ku Yuda mʼdziko limene anakhetsa magazi a anthu osalakwa.
20 Fa himoneñe nainai’e t’Iehodà; naho tariratse an-tariratse t’Ierosalaime
Koma Yuda adzakhala ndi anthu mpaka muyaya ndi Yerusalemu ku mibadomibado.
21 Le ho lioveko ty lio’iareo mboe tsy nilioveko fa himoneñe e Tsione ao t’Iehovà.
Kukhetsa magazi kwawo kumene Ine sindinakhululuke ndidzakhululuka.”

< Joela 3 >