< Joba 41 >

1 Mahatarike i Leviatàne am-bintañe v-iheo? hatindri’o ambane an-tàly hao i lela’ey?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Lefe’o hao ty mampikiviro i oro’ey, ndra ty hangirike i soma’ey am-pengoke?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Hanao lako halaly ama’o hao re? Ke hivolañe mora ama’o?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Hifañina ama’o hao, handrambesa’o aze ho fetrek’oro’o kitro katroke?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Ho hisà’o hao hoe voroñe? ke ho tantalie’o ho amo anak’ ampela’oo.
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Hifampihehetse ama’e hao o mpanao balikeo? Ho zarae’ iareo am’ o mpanao takinakeo hao re?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Ho tsitsihem-pirango hao i holi’ey? Ndra i loha’ey an-defom-piañe?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Apaoho ama’e ty fità’o vaho tiahio i ho ali’oy te tsy hindroe’o.
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Hete! Toe tsy vente’e t’ie salalaeñe, tsy ho tafahohoke hao te isahañe?
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 I Tsy eo ty lahitsi’ay mahavany hitsobore aze; ia arè ty mahafiatreatre amako?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Ia ty nanolotse ahy, te havahako? ahiko ze hene ambanen-dikerañe ao.
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 Tsy hitsiñeko o kitso’eo, ty haozara’e ra’elahiy, vaho i sandri’e tsaratseakey,
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Ia ty hañolitse o sisin-koli’eo? Ia ty hahafizilik’ añivom-balañorà’e roe ao?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 Ia ty mahafisokake o lalam-bein-tarehe’eo? mampangetraketrake ty fañarikatoha’ o nife’eo.
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 Fisengea’e o sisì’e fatratseo, ie mikititse hoe linite;
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 Akore ty fifampikiteha’e kanao tsy mahafitsifitse ao ty tioke.
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Nifampireketeñe iereo, mifampipiteke, tsy lefe akatrake.
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 Mitsopela-kazavàñe o fihatsìhe’eo, manahake ty holi-maso’ i maraindraiñey o maso’eo.
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Failo milebaleba ty miakatse am-bava’e, afo mipelatse ty mipitsike mb’eo.
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 Mañatoeñe o loa-koro’eo, hoe valàñe mamorotse ambone vinda mirehetse.
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 Mamiañe foroha ty kofò’e, afo misodotse ty miboak’ am-bava’e ao.
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 Mimoneñe an-kàto’e ty haozarañe, vaho mitsinjak’ aolo’e eo ty miroreke.
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 Mifampirekets’ ama’e i holi’e mifanosokeo, gañe ama’e Izay tsy mete asitse.
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 Gañe hoe vato ty fo’e; manahake ty hamafem-bato-lisañe ambane.
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 Ie mivoalatse, miholi-tsandry o fanalolahio; ie vereñe mamoe’ay.
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 Tsy lefe t’ie liherem-pibara, ndra lefoñe, ndra ana-defo, ndra baramino masioñe.
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 Atao’e ho boka maike ty viñe, naho hatae voroke ty torisìke.
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 Tsy mahafandrifitse aze o ana-paleo; atao’e forompotse o vato-piletseo.
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 Tonton-drongoñe ama’e o kobaiñeo, tohafa’e o lefoñe mikaratsakaratsakeo.
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 Silam-balañe-tane masioñe ty ambane’e, hoe mamofopofoke ampemba t’ie miranga fotake.
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 Ampitroatroahe’e hoe valàñe i lalekey; ampanahafe’e ami’ty fampitranahañe rano mañitse i riakey.
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 Anoe’e lala-miloeloe ty am-boho’e ao anoe’e hoe a maròy foty i lalekey.
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 Tsy ambone-tane atoy ty mañirinkiriñe aze, ie nitsenèñe tsy ho aman-tahotse.
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Jilojilove’e iaby ze atao abo; ie ty lohà’ ze hene anam-pirengevohañe.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”

< Joba 41 >