< Joba 22 >
1 Le hoe ty natoi’ i Elifaze nte-Temane:
Pamenepo Elifazi wa ku Temani anayankha kuti,
2 Mahasoa an’Andrianañahare hao t’indaty? mahafitoloñ’aze hao t’ie bey moko?
“Kodi munthu nʼkukhala waphindu kwa Mulungu? Kodi munthu wanzeru angamupindulire Iye?
3 Mahafale i El-Sadai hao t’ie vantañe? aman-tambe’e hao te fonire’o tsy aman-kila o sata’oo?
Kodi Wamphamvuzonse akanapeza chabwino chotani iweyo ukanakhala wolungama? Kodi iyeyo akanapeza phindu lanji makhalidwe ako akanakhala angwiro?
4 Ty fañeveña’o ama’e hao ty añendaha’e azo hizaka’e?
“Kodi nʼchifukwa choti umamuopa, kuti azikudzudzula, kuti azifuna kukukokera ku mlandu?
5 Tsy mitoabotse hao o tahi’oo? Tsi-vatse o hakeo’oo!
Kodi osati nʼchifukwa chakuti kuyipa kwako nʼkwakukulu? Kodi machimo ako si opanda malire?
6 Nangala’o tsoake ami’ty tsy vente’e i rahalahi’oy, vaho hinoli’o hiboridañe.
Iwe unkawumiriza abale ako kuti akupatse chikole popanda chifukwa; umalanda anthu zovala zawo ndi kuwasiya amaliseche.
7 Tsy nanjotsoa’o rano ty taliñiereñe hinoma’e, vaho nitana’o amy salikoeñey ty mahakama.
Sunawapatse madzi anthu otopa, ndipo unawamana chakudya anthu anjala,
8 Tompo’ ty tane toy ty fanalolahy; vaho mpioneñe ao ty aman-kasy.
ngakhale unali munthu wamphamvu, wokhala ndi malo akeake, munthu waulemu wake, wokhala mʼdzikomo.
9 Nampolie’o hara’e o vantotseo, vaho navitso’o ty taña’ o bode-raeo.
Ndipo akazi amasiye unawachotsa wopanda kanthu, ndipo unapondereza ana amasiye.
10 Toly t’ie arikoboñem-pandrike, naho itsoborean-ka’endrahañe;
Nʼchifukwa chake misampha yakuzungulira, nʼchifukwa chake tsoka ladzidzidzi lakuchititsa mantha,
11 an-kamoromoroñañe tsy hahaisaha’o, vaho mandipots’azo ty rano bey.
nʼchifukwa chake kuli mdima kuti sungathe kuona kanthu, nʼchifukwa chakenso madzi achigumula akumiza.
12 Tsy andindin-dikerañe ao hao t’i Andrianañahare? Isaho ka ty haabo’ o vasiañeo, t’ie an-tiotiots’ eñe.
“Kodi Mulungu sali kutalitali kumwamba? Ndipo ona nyenyezi zili mmwamba kwambirizo, ona kutalika kwake pamene zililipo!
13 Hoe irehe: Ino ty arofoanan’ Añahare? hahafiranga o ieñe milodolodoo hao ty fizakà’e?
Komabe iweyo ukunena kuti, ‘Kodi Mulungu amadziwa chiyani? Kodi Iye amaweruza mu mdima woterewu?
14 Mañibok’ aze o rahoñe mikopokeo tsy hahavazohoa’e, vaho an-kivoho’ i likerañey ty fidraidraita’e.
Mitambo yakuda yamuphimba, kotero kuti Iye sakutiona pamene akuyendayenda pamwamba pa thambopo.’
15 Horihe’o hao i lalañe haehae nilià’ ondaty tsereheñeoy?
Kodi iwe udzayendabe mʼnjira yakale imene anthu oyipa ankayendamo?
16 O sinintoñe aolo’ ty andro’eo; ie sinaon-drano-vohitse o faha’eo,
Iwo anachotsedwa nthawi yawo isanakwane, maziko awo anakokoloka ndi madzi achigumula.
17 ie nanao ty hoe aman’ Añahare: Ihankaño zahay; naho, Ino ty mete hanoa’ i El-Sadai?
Anthuwo anati kwa Mulungu, ‘Tichokereni! Kodi Wamphamvuzonse angatichitire chiyani?’
18 Mbe natsafe’e hasoa avao ty anjomba’e. Fe lavits’ ahy ty famerea’ o tsivokatseo.
Chonsecho ndi Iye amene anadzaza nyumba zawo ndi zinthu zabwino, choncho ine sindigwirizana ndi uphungu wa anthu oyipa.
19 Oni’ o vañoñeo Izay, le fale, iankahafa’ o malioo añ’ inje,
“Anthu olungama amaona kuwonongeka kwawo ndipo amakondwera; anthu osalakwa amangoseka, akamuona woyipa akulangidwa.
20 [ami’ty hoe]: Toe naitoeñe o malaiñe anaio, niforototoe’ ty afo o vara’ iareoo.
Amanena kuti, ‘Ndithudi adani athu awonongeka ndipo moto wawononga chuma chawo!’
21 Aa le mifampilongoa ama’e, hanintsiña’o, hitotsaha’ ty soa.
“Gonjera Mulungu kuti ukhale naye pamtendere; ukatero udzaona zabwino.
22 Ehe, rambeso am-palie’e ty Hake, vaho ahajao añ’arofo’o ao o tsara’eo.
Landira malangizo a pakamwa pake ndipo usunge mawu ake mu mtima mwako.
23 Mimpolia amy El-Sadai le ho vaoen-drehe, ampisitaho lavitse i kiboho’oy ty tsy to.
Ukabwerera kwa Wamphamvuzonse udzabwezeretsedwa; ukachotsa zoyipa zonse zimene zimachitika mʼnyumba mwako,
24 Ahajao an-debok’ ao ty vara, ty volamena’ i Ofire amo vato an-torahañeo.
ndipo chuma chamtengowapatali nuchiona ngati fumbi, golide wa ku Ofiri numutaya ku miyala ya ku zigwa.
25 Le i El-Sadai ty ho vara’o, ie ty volafoty ki’e ama’o,
Pamenepo Wamphamvuzonseyo adzakhala golide wako, siliva wako wamtengowapatali.
26 vaho hifalea’o t’i El-Sadai, le hampiandrae’o aman’ Añahare ty lahara’o.
Pamenepo udzakondwera naye Wamphamvuzonse ndipo udzakweza nkhope yako kwa Mulungu.
27 Hihalaly ama’e irehe, le hijanjiña’e, ie havaha’o o nifantà’oo.
Udzamupempha ndipo adzakumvera, ndipo udzapereka zimene unalonjeza.
28 Hisafiry irehe, le ho tafetetse vaho hireandreañe amo lala’oo ty hazavàñe.
Chimene watsimikiza kuti uchite, chidzachitikadi, kuwala kudzakuwunikira pa njira yako.
29 Naho eo ty areke, le hanoa’o ty hoe: tsiringèvotse! ty mirè-batañe ro haha.
Pamene anthu agwetsedwa pansi, iwe nʼkunena kuti, ‘Akwezeni!’ Pamenepo Iye adzapulumutsa anthu oponderezedwa.
30 Havotso’e hao ty tsy malio tahiñe, hañaha azo ty faliom-pità’o.
Iye adzapulumutsa ngakhale munthu amene ndi wolakwa, ameneyo adzapulumutsidwa kudzera mʼkulungama kwako.”