< Jeremia 37 >

1 Nifehe ho mpanjaka t’i Tsidkia nandimbe i Konia ana’ Iehoiakime ana’ Iosia nanoe’ i Nebokadnetsare, mpanjaka’ i Bavele, mpanjaka an-tane Iehodày.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni, inakhazika pa mpando waufumu Zedekiya mwana wa Yosiya kukhala mfumu ya Yuda. Iye analowa mʼmalo mwa Yehoyakini mwana wa Yehoyakimu.
2 F’ie ndra o mpitoro’eo ndra ondati’ i taneio tsy nañaoñe ty tsara’ Iehovà nisaontsie’e añam’ Iirmeà mpitoky.
Koma Zedekiya kapena atumiki ake ngakhalenso anthu a mʼdzikomo sanasamalire mawu a Yehova amene anayankhula kudzera mwa mneneri Yeremiya.
3 Nirahe’ i Tsidkia mpankaja t’Iehokale ana’ i Selemia naho i Tsefania mpisoroñe ana’ i Maasaia am’ Iirmeà mpitoky nanao ty hoe: Ehe, halalio ho anay t’Iehovà Andrianañaharentika.
Tsono Zedekiya anatuma Yehukali mwana wa Selemiya ndi wansembe Zefaniya mwana wa Maseya kwa mneneri Yeremiya ndi uthenga uwu: “Chonde tipempherereni kwa Yehova Mulungu wathu.”
4 Ie amy zay nifampitamboemboeñe am’ondatio t’Iirmeà; ie mboe tsy nagodoñe am-balabey ao,
Nthawi imeneyinso nʼkuti Yeremiya ali ndi ufulu woyenda pakati pa anthu chifukwa anali asanaponyedwe mʼndende.
5 le niakatse an-tane Mitsraime o lahindefo’ i Paroo; aa ie jinanji’ o nte-Kasdy nañarikatoke Ierosalaimeo i talily ty am’ iereoy le nisitak’ am’ Ierosalaime.
Nthawi imeneyinso nʼkuti gulu lankhondo la Farao litatuluka mʼdziko la Igupto. Ndipo Ababuloni amene anali atazinga Yerusalemu atamva zimenezi, anachoka ku Yerusalemuko.
6 Le niheo am’Iirmeà ty tsara’ Iehovà:
Tsono Yehova anawuza mneneri Yeremiya kuti,
7 Hoe t’Iehovà Andrianañahare’ Israele: Zao ty ho saontsie’ areo amy mpanjaka’ Iehodày nañirak’ anahareo amako hañontane: Himpoly mb’an-tane’e e Mitsraime añe o lian-dahindefo’ i Parò nionjoñe hañolotse anahareoo;
“Uyiwuze mfumu ya Yuda imene inakutuma kuti udzapemphe nzeru kwa ine kuti Ine Yehova, Mulungu wa Israeli ndikuti, gulu lankhondo la Farao limene linatuluka kuti lidzakuthandize lidzabwerera kwawo ku Igupto.
8 le hibalike mb’etoa o nte Kasdio hialy ami’ty rova toy hitavañe vaho hamorototo aze amañ’afo.
Ndipo Ababuloni adzabwerera kudzathira nkhondo mzinda uno. Iwo adzawugonjetsa ndi kuwutentha.
9 Hoe t’Iehovà, Ko mamañahy vatañe ami’ty hoe: Tsy mahay tsy hienga antika o nte-Kasdio. Fa tsy hienga!
“Yehova akuti: Musadzinyenge, nʼkumaganiza kuti, ‘Ndithu Ababuloni adzatisiya.’ Ndithudi sadzakusiyani!
10 Ndra te fonga zinama’areo o lahindefon-te-Kasdy mialy ama’areoo, vaho tsy aman-tsehanga’e naho tsy ty fere an-kiboho’e ao, le ie ty ho nitroatse hamorototo ty rova toy amañ’afo.
Ngakhale mutagonjetsa gulu lonse lankhondo la Ababuloni limene likukuthirani nkhondo ndipo mʼmatenti mwawo ndikutsala anthu ovulala okhaokha, amenewo adzabwera ndi kudzatentha mzinda uno.”
11 Aa ie nisitake Ierosalaime o nte-Kasdio ty amy lian-dahin-defo’ i Paròy,
Gulu lankhondo la Ababuloni litaleka kuthira nkhondo mzinda wa Yerusalemu chifukwa choopa gulu lankhondo la Farao,
12 le niakatse Ierosalaime t’Iirmeà hionjoñe mb’an-tane’ i Beniamine añe handrambe ty anjaran-tane’e añivo’ ondaty ao.
Yeremiya ananyamuka kuchoka ku Yerusalemu ndi kumapita ku dziko la Benjamini kuti akalandire gawo lake la minda ya makolo ake.
13 Ie pok’ an-dalambei’ i Beniamine eo le tsinepa’ ty mpijilo atao Iiria ana’ i Selemia ana’ i Kanania t’Iirmeà ami’ty hoe, Mitotse mb’ amo nte-Kasdio ni-heo.
Koma atafika pa Chipata cha Benjamini, mkulu wa alonda amene dzina lake linali Iriya mwana wa Selemiya, mwana wa Hananiya, anagwira mneneri Yeremiyayo ndipo anati, “Iwe ukuthawira kwa Ababuloni!”
14 Le hoe t’Iirmeà: Vande izay; izaho tsy misitake mb’ amo nte-Kasdio. Fe tsy nihaoñe’e; aa le sinambo’ Iiria t’Iirmeà vaho nasese’e mb’amo roandriañeo.
Yeremiya anati, “Zimenezo si zoona! Ine sindikuthawira kwa Ababuloni.” Koma Iriya sanamumvere. Mʼmalo mwake anagwira Yeremiya nʼkupita naye kwa akuluakulu.
15 Niviñera’ o roandriañeo t’Iirmeà, le finofo’ iareo vaho najo’ iareo an-drohy añ’anjomba’ Ionatane silikitera ao, fa nanoeñe valabey ty ao.
Akuluakuluwo anamupsera mtima Yeremiya ndipo anamukwapula ndi kumuyika mʼnyumba ya mlembi Yonatani, imene anayisandutsa ndende.
16 Aa ie fa najoroboñe añ’efets’ efe’ i valabeiy t’Iirmeà naho nitambatse ao andro maro t’Iirmeà,
Yeremiya anayikidwa mʼndende ya pansi pa nthaka, kumene anakhalako nthawi yayitali.
17 le nampihitrife’ i Tsidkia amy zao re le nampihovañ’ aze naho natola’e añ’anjomba’e ao vaho nañontane aze, ty hoe: Hera ao ty tsara boak’ am’ Iehovà? Toe ao! hoe t’Iirmeà, fa hoe re: Hasese am-pitàm-panjaka’ i Bavele irehe.
Kenaka Mfumu Zedekiya inatuma anthu kuti akayitane Yeremiya ndipo anabwera naye ku nyumba ya mfumu. Atafika mfumu inamufunsa mwamseri kuti, “Kodi pali mawu ena amene Yehova wakuwuza?” Yeremiya anayankha kuti, “Inde. Inu mfumu mudzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni.”
18 Tinovo’ Iirmeà amy Tsidkia mpanjaka’ Iehodà ty hoe, Ino ty tahiko ama’o ndra amo mpitoro’oo ndra am’ ondati’oo te nagodo’o am-po porozò ao?
Pamenepo Yeremiya anafunsa Mfumu Zedekiya kuti, “Kodi ndakulakwirani chiyani inuyo kapena akuluakulu anu kapenanso anthu awa, kuti mundiyike mʼndende?
19 Aia ka o mpitoki’o nitoky ama’o ty hoe: Tsy ho avy haname azo naho ty tane toy ty mpanjaka’ i Baveleo?
Kodi ali kuti aneneri anu amene anakuloserani kuti, ‘Mfumu ya ku Babuloni sidzakuthirani nkhondo pamodzi ndi dziko lino’?
20 Aa le ijanjiño abey, ry taleko mpanjaka: Ehe, tsendreño o halalikoo, le ko ampipolieñ’ ahy mb’añ’anjomba’ Ionatane silikitera mb’eo, tsy mone hivetrake ao.
Koma tsopano, mbuye wanga mfumu, chonde tamverani. Loleni ndinene pempho langa pamaso panu: Musandibwezere ku nyumba ya mlembi Yonatani, kuopa kuti ndingakafere kumeneko.”
21 Aa le nandily t’i Tsidkia, naho najò’ iareo an-kiririsa’ o mpigaritseo t’Iirmeà; vaho nanjotsoañe vonga-mofo boak’ andro hirik’ an-dalam-panoñak’ ao ampara’ te fonga nikapaike ty mofo’ i rovay. Aa le nidoñe an-kiririsam-pigaritse ao t’Iirmeà.
Tsono Mfumu Zedekiya analamula kuti Yeremiya asungidwe mʼbwalo la alonda. Ankamupatsa buledi tsiku ndi tsiku amene ankamugula kwa ophika buledi. Anapitiriza kutero mpaka buledi yense anatha mu mzindamo. Choncho Yeremiya anapitirira kukhala mʼbwalo la alonda.

< Jeremia 37 >