< Jeremia 1 >

1 Ty enta’ Iirmeà ana’ i Kilkià mpiamo mpisoroñe nte-Anatote an-tane’ Beniamìneo,
Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
2 ie nivotraha’ ty tsara’ Iehovà tañ’andro’ Iosià ana’ i Amone, mpanjaka’ Iehodà, amy taom-paha folo-telo-ambi’ i fifehea’ey.
Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
3 Niheova’e ka tañ’andro’ Iehoiakime ana’ Iosià, mpanjaka’ Iehodà pak’ami’ty fimodoa’ ty taoñe faha folo-raik’ambi’ i Tsidkià ana’ Iosià mpanjaka’ Iehodà, ampara’ ty faneseañe Ierosalaime an-drohy añe amy volam-paha-limey.
Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
4 Aa le niheo amako ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe:
Yehova anayankhula nane kuti,
5 Ihe mbe tsy tsineneko an-trok’ ao le nifàntako; aolo’ ty niboaha’o an-koviñ’ ao le navahako, vaho tinendreko ho mpitoky amo kilakila’ ndatio.
“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
6 Le hoe ty nataoko, Ehe Talè ­Iehovà! Izaho tsy mahafivolañe, fa mbe anak’ ajaja.
Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
7 Aa hoe t’Iehovà amako: ko manao zao, t’ie Anak’ ajaja; fa ze amantohako azo ty handenà’o le ndra inoñ’ inoñe ty hatoroko azo, ty ho taroñe’o.
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
8 Ko ihembaña’o; fa mpiama’o iraho handrombak’ azo, hoe t’Iehovà.
Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
9 Nahiti’ Iehovà amy zao ty fità’e, le nedrè’e ty vavako; vaho nanao ty hoe amako t’Iehovà: Ingo te napoko am-palie’o ao o entakoo;
Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
10 Oniño te androany ty nampijadoñako azo ambone’ o fifelehañeo naho o fifeheañeo. Ty hañombotse naho hampigorobañe, ty hamotsake naho handrotsake; ty handranjy vaho hambole.
Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
11 Mbore nimb’amako ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe: O Iirmeà, mahaisake ino v-iheo? le hoe ty asako: Mahatrea ty tsampa-mahabibo.
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
12 Le hoe t’Iehovà amako, Toe nahaonin-drehe; fa jilojiloveko o volakoo hahatafeterako aze.
Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
13 Niheo amako fañindroe’e ty tsara’ Iehovà, nanao ty hoe: Inoñe o isa’oo? le hoe iraho, Mahatrea valàñe mikokèntrekokèntreñe iraho; le boak’ avaratse ey ty fihilañam-bava’e.
Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
14 Aa le hoe t’Iehovà tamako: Ho boroboñafe’ ty hekoheko boak’ avaratse añe amy ze hene’ndaty an-tane atoy.
Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
15 Ingo ho koiheko iaby ze fifokoa’ o fifeheañe avaratseo, hoe t’Iehovà, homb’ atoy, songa hampipoke ty fiambesam-panjaka’e an-dalam-bey fimoahañe am’ Ierosa­laime, naho amy ze fonga kijoly miarikoboñe aze, vaho amy ze hene rova’ Iehodà.
Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 Aa le ho taroñeko te hizakako ty hatsivokara’ iareo; amy te naforintse’ iareo iraho, naho mañemboke aman’ drahare ila’e, vaho mitalaho amo sata-pità’iareoo avao.
Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
17 Ihe arè, mampidiaña vania vaho miavòta, saontsio ze hene amantohako azo; ko ifimpìña’o, tsy mone hampi­tsolofiñeko añatrefa’iereo.
“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
18 Hehe te nanoeko rova finatratse irehe, bodam-biñe, naho kijoly torisìke, amo tane iabio, amo mpanjaka’ Iehodao, amo roan­dria’eo, amo mpisoro’eo, vaho am’ ondati’ i taneio.
Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
19 Toe hialia’ iereo; fe tsy hahagioke, amy te ama’o iraho, hoe t’Iehovà, hañahako azo.
Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

< Jeremia 1 >