< Isaia 37 >

1 Aa ie nahajanjiñe izay t’Iekiz­kia, le rinia’e o siki’eo naho nisaron-gony vaho nimoak’ añ’an­jomba’ Iehovà ao.
Mfumu Hezekiya atamva zimenezi, anangʼamba zovala zake navala chiguduli ndipo analowa mʼNyumba ya Yehova.
2 Nirahe’e mb’am’ Iesaià mpitoky ana’ i Amotse amy zao t’i Eliakime mpifeleke i anjombay, naho i Sebnà mpanokitse naho o zokem-pisoroñeo songa nisaron-gony.
Iye anatuma Eliyakimu woyangʼanira nyumba ya mfumu, Sebina mlembi wa bwalo, ndi ansembe akuluakulu, onse atavala ziguduli, kwa mneneri Yesaya mwana wa Amozi.
3 Le hoe ty enta’ iareo ama’e: Hoe t’Iekizkia: Androm-poheke naho trevoke vaho teratera ty andro toy; fa antitotse ho samake o ajajao fe tsy eo ty haozarañe hahatoly.
Iwo anamuwuza kuti, “Hezekiya akunena kuti, ‘Lero ndi tsiku lamavuto, lachilango ndi lamanyazi. Ife lero tili ngati mayi woyembekezera amene pofika nthawi yoti achire akupezeka kuti alibe mphamvu zoberekera.’
4 He ho janjiñe’ Iehovà Andrianañahare’o o saontsi’ i Rabsakè nañiraham-panjaka’ i Asore tale’eo hanigike an’ Andrianañahare veloñe, vaho hendaha’ Iehovà Andrianañahare’o i saontsy jinanji’ey; ehe mihalalia ho amy ze sehanga’e mbe eo.
Mwina Yehova Mulungu wanu adzamva mawu onse a kazembe amene mbuye wake, mfumu ya ku Asiriya anamutuma kudzanyoza Mulungu wamoyo, ndipo Mulunguyo adzamulanga chifukwa cha mawu amene Yehova Mulungu wanu wamva. Choncho pemphererani anthu otsala amene akanali ndi moyo.”
5 Aa le nivo­trak’ am’ Iesaià eo o mpitoro’ Iekizkiao.
Akuluakulu a mfumu Hezekiya atafika kwa Yesaya,
6 Le hoe t’Iesaià am’ iareo: Zao ty ho saontsie’ areo amy tale’ areoy: Hoe ty nafè’ Iehovà: ko hembañ’ amo entañe jinanji’oo, amo niteratera’ o mpitoro’ i Mpanjaka’ i Asoreo Ahikoo.
Yesaya anawawuza kuti, “Kawuzeni mbuye wanu kuti ‘Yehova akunena kuti: Usachite mantha ndi zimene wamva, mawu amene nthumwi za mfumu ya ku Asiriya zandinyoza nawo Ine.
7 Inao te hajoko ama’e ty fañahy, le hijanjiñe tolom-boetse naho himpoly an-tane’e añe vaho hampikorovoheko am-pibara an-tane’e ao.
Tamverani! Ine ndidzayika mwa mfumuyo mzimu wina kotero kuti akadzamva mphekesera ya nkhondo, adzabwerera ku dziko lake, ndipo Ine ndidzachititsa kuti aphedwe ndi lupanga kwawo komweko.’”
8 Aa le nibalike mb’eo t’i Rabsakè, vaho zoe’e nifañotake amy Libnà ty mpanjaka’ i Asore, fa tsinano’e t’ie nienga i Lakise.
Kazembe wa ankhondo uja atamva kuti mfumu ya ku Asiriya yachoka ku Lakisi, iye anabwerera mʼmbuyo ndipo anakapeza mfumu ikuchita nkhondo ndi mzinda wa Libina.
9 Le hoe ty jinanji’e ty amy Tirhakà, mpanjaka’ i Kose, Miavotse mb’etoa re hialy ama’o. Ie jinanji’e izay le nañitrike am’ Iekizkia ty hoe:
Nthawi imeneyi Senakeribu analandira uthenga wakuti Tirihaka, mfumu ya ku Kusi akubwera kudzachita naye nkhondo. Atamva zimenezi, anatumiza amithenga kwa Hezekiya ndi mawu awa:
10 Ty hoe ty ho saontsie’ areo am’ Iekizkia mpanjaka’ Iehodà: Asoao tsy henga’o hanigìke azo t’i Andrianañahare iatoa’o, hanao ty hoe: Tsy hatolo­tse am-pitàm-panjaka’ i Asore t’Ierosalaime.
“Kawuzeni Hezekiya mfumu ya ku Yuda kuti: Usalole kuti Mulungu amene ukumudalira akupusitse ponena kuti, ‘Yerusalemu sadzaperekedwa mʼmanja mwa mfumu ya ku Asiriya.’
11 Inao, tsy jinanji’o hao ty nanoa’ o mpanjaka’ i Asoreo amo hene taneo? ie nampangotomomohe’e; aa havo­tsotse hao nahareo?
Ndithudi iwe unamva zimene mafumu a ku Asiriya akhala akuchitira mayiko onse. Iwo anawawononga kotheratu. Tsono iwe ndiye ndi kupulumuka?
12 Fa rinomban-drahare’e hao o rinotsan-droaekoo: i Gozane naho i Harane, naho i Retsefe vaho o ana’ i Edene e Telasareo?
Makolo anga anawononga mizinda ya Gozani, Harani, Rezefi ndi anthu a ku Edeni amene ankakhala ku Telasara. Kodi milungu inayi ija anawapulumutsa anthu a mizindayi?
13 Aia ty mpanjaka’ i Kamàte naho ty mpanjaka’ i Arpade naho ty mpanjakan-drova’ i Sefarvaime, ty a i Henà vaho Ivà?
Kodi mafumu a ku Hamati, Aripadi, Safaravaimu, Hena ndi Iva ali kuti?”
14 Aa ie rinambe’ Iekizkià i taratasy am-pità’ o nampihitrifeñeoy naho vinaki’e; le nionjomb’ añ’ anjomba’ Iehovà mb’eo t’Iekizkia, vaho vinela’e añatrefa’ Iehovà.
Hezekiya analandira kalata kwa amithenga nayiwerenga pomwepo. Hezekiya anapita ku Nyumba ya Yehova ndipo anayika kalatayo pamaso pa Yehova.
15 Nihalaly am’ Iehovà t’Iekizkia ami’ty hoe:
Ndipo Hezekiya anapemphera kwa Yehova:
16 Ry Iehovà’ i Màroy, Andrianañahare’ Israele, mpiambesatse ambone’ o kerobeo; Ihe ro Andrianañahare, Ihe avao, amy ze kila fifeleha’ ty tane toy; ry Andrianamboats’ i likerañey naho ty tane toy.
“Inu Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli, amene mumakhala pa mpando wanu waufumu pakati pa akerubi, Inu nokha ndiye Mulungu wolamulira maufumu onse a dziko lapansi. Munalenga kumwamba ndi dziko lapansi.
17 Atokilaño ty ravembia’o ry Iehovà naho janjiño; abolanaho o fihaino’oo ry Iehovà vaho vazohò; inao ze hene enta’ i Senkeribe, nahitri’e hañinje an’ Andrianañahare veloñe.
Inu Yehova tcherani khutu ndipo mumve. Inu Yehova, tsekulani maso anu ndipo muone. Imvani mawu onse amene Senakeribu watumiza, kunyoza Mulungu wamoyo.
18 O ry Iehovà, Toe fonga nampangoakoahe’ o mpanjaka’ i Asoreo o fifeheañeo naho o tane’ iareoo,
“Yehova, nʼzoonadi kuti mafumu a Asiriya anawononga mitundu yonse ya anthu ndi mayiko awo.
19 vaho naretsa’ iareo añ’afo ao o ndrahare’ iareoo amy t’ie tsy Andrianañahare, fa sata-pità’ ondaty, hatae naho vato; aa le finongo’e.
Iwo anaponyera pa moto milungu yawo ndi kuyiwononga pakuti sinali milungu koma mafano a mitengo ndi miyala, yopangidwa ndi manja a anthu.
20 Ie henaneo ry Iehovà Andria­nañahare’ay, rombaho am-pità’e zahay, soa te ho fohi’ ze kila fifeleha’ ty tane toy te Ihe ro Iehovà, Ihe avao.
Tsono Inu Yehova Mulungu wathu, tipulumutseni mʼdzanja lake kuti maufumu onse a dziko lapansi adziwe kuti Inu nokha, Inu Yehova, ndiye Mulungu.”
21 Aa le nahitri’ Iesaià ana’ i Amotse am’ Iekizkia ty hoe: Hoe ty nafè’ Iehovà, Andrianañahare’ Israele: Amy te ihe ro nihalaly amako ty amy Senkeribe mpanjaka’ i Asore,
Tsono Yesaya mwana wa Amozi anatumiza uthenga wochokera kwa Yehova kwa Hezekiya poyankha pemphero lake lokhudza Senakeribu mfumu ya ku Asiriya.
22 le hoe ty tsara nafè’ Iehovà ama’e: Fa nanirika azo i anak’ ampela’ i Tsioney, nitohafa’e an-drabioñe; vaho nikofikofi-doha amboho’o ao i anak’ ampela’ Ierosalaimey.
Mawu amene Yehova wayankhula motsutsana naye ndi awa: “Mwana wamkazi wa Ziyoni akukunyoza ndi kukuseka. Mwana wamkazi wa Yerusalemu, akupukusa mutu wake pamene iwe ukuthawa.
23 Ia ty sinigì’o naho tineratera’o? Ia ty nañonjona’o feo? Toe nampiandrae’o mañambone ey o maso’oo, hiatreatrea’o t’i Masi’ Israele!
Kodi iwe wanyoza ndi kulalatira ndani? Kodi iwe wafuwulira ndi kumuyangʼana monyada ndani? Watsutsana ndi Woyerayo wa Israeli!
24 O mpitoro’oo ty nañamavoa’o i Talè, ami’ty hoe: Amo hatsifotofoton-tsaretekoo ty nitroarako ankaboa’ o vohitseo, an-tsifitsifi’ i Lebanone ao; fonga finirako ze mendoraveñe abo; naho ze akao soa; nizilihako i haboañe lavitse ama’ey, ty ala-vondro an-goloboñe kobokara.
Kudzera mwa amithenga ako iwe wanyoza Ambuye. Ndipo wanena kuti, ‘Ndi magaleta anga ochuluka ndafika pamwamba pa mapiri, pamwamba penipeni pa mapiri a Lebanoni. Ndagwetsa mitengo yamkungudza yayitali kwambiri, ndi mitengo yabwino kwambiri ya payini. Ndafika pa msonga pake penipeni, nkhalango yake yowirira kwambiri.
25 Nihaly iraho vaho ninon-drano, le ami’ty lelam-pandiako ty nañamaihako ze hene saka’ i Mitsraime.
Ndakumba zitsime ku mayiko achilendo ndi kumva madzi akumeneko ndi mapazi anga ndawumitsa mitsinje yonse ya ku Igupto.’
26 Mboe tsy jinanji’o hao? Tsietoimoneñe izay ty nisafiriako taolo añe t’ie naereñereko; ie o tafetetse henaneo; te hafotetse ho kivotrevotre mangoakoake o rova nifatrareñeo.
“Kodi sunamvepo kuti zimenezi ndinazikonzeratu kalekale? Ndinazikonzeratu masiku amakedzana; tsopano ndazichitadi, kuti iwe kwako nʼkusandutsa mizinda yotetezedwa kukhala milu ya miyala.
27 Aa le ni-kede ozatse o mpimone’eo, niampoheke vaho nisalatse, nanahake ty ahetse an-kivoke ey, hoe rongoñe antsetra, hoe ahetse ambone anjomba, mae t’ie mbe tsy matoe.
Anthu amene ankakhala kumeneko analibenso mphamvu, ankada nkhawa ndi kuchititsidwa manyazi. Anali ngati mbewu za mʼmunda, ngati udzu wanthete, ali ngati udzu omera pa denga, umene mphepo imawumitsa usanakule nʼkomwe.
28 Fe apotako o fiambesa’oo, naho o fiavota’oo, o fimoaha’oo vaho o famantsiña’o amakoo.
“Koma Ine ndimadziwa zonse za iwe; ndimadziwa pamene ukuyima ndi pamene ukukhala; ndimadziwa pamene ukutuluka ndi pamene ukulowa, ndiponso momwe umandikwiyira Ine.
29 Aa kanao nitazataza’o, naho nañambone mb’amo sofiko toañe ty korà’o, le hanoeko am-piantsoña’o ao ty porengoko, naho am-pivimbi’o ty laboridiko, vaho hampolieko mb’amy lalañe nomba’o mb’etoañey.
Chifukwa umandikwiyira Ine ndi kuti mwano wako wamveka mʼmakutu anga, ndidzakola mphuno yako ndi mbedza ndikuyika chitsulo mʼkamwa mwako, ndipo ndidzakubweza pokuyendetsa njira yomwe unadzera pobwera.
30 Le zao ty ho viloñe ama’o: hikama o raha mitiry avao nahareo ami’ty taoñe toy; le ze mijirike ama’e ami’ty taom-paharoe; le mitongisa ami’ty taom-pahatelo naho manataha, amboleo valoboke vaho ikamao ty voka’e.
“Iwe Hezekiya, chizindikiro chako cha zimene zidzachitike ndi ichi: “Chaka chino mudzadya zimene zamera zokha, ndipo chaka chachiwiri zimene zaphukira pa zomera zokha, koma chaka chachitatu mudzafesa ndi kukolola, mudzawoka mitengo yamphesa ndi kudya zipatso zake.
31 Le hamahatse mañambane ty hengaha’ i anjomba’ Iehodày, vaho hamoa mañambone.
Anthu a nyumba ya Yuda amene adzatsalire adzazika mizu yawo pansi ndipo adzabereka zipatso poyera.
32 Fa boake Ierosalaime ao ty hiavota’ ty honka’e vaho hirik’ am-bohi-Tsione o mahafibotàfotseo; ho henefe’ ty fahimbaña’ Iehovà’ i Màroy.
Pakuti ku Yerusalemu kudzachokera anthu otsala, ndi ku phiri la Ziyoni gulu la anthu opulumuka. Changu cha Yehova Wamphamvuzonse chidzachita zimenezi.
33 Aa le hoe t’Iehovà ty amy Mpanjaka’ i Asorey: tsy himoake an-drova atoy re, ndra hitifitse ana-pale, tsy hiatrefa’e am-pikalañe ndra hampitoabora’e votren-tane.
“Choncho Yehova akunena izi za mfumu ya ku Asiriya: “Iye sadzalowa mu mzinda umenewu kapena kuponyamo muvi uliwonse. Sadzafika pafupi ndi mzindawu ndi ankhondo ake a zishango kapena kuwuzinga ndi mitumbira yankhondo.
34 I lalañe nomba’e mb’etoañey, ty himpolia’e mb’eo, tsy himoake ami’ty rova toy re, hoe t’Iehovà
Adzabwerera potsata njira yomwe anadzera pobwera; sadzalowa mu mzinda umenewu,” akutero Yehova.
35 Fa harovako naho ho rombaheko ty amako ty rova toy, vaho ty amy mpitoroko Davidey.
“Ine ndidzawuteteza ndi kuwupulumutsa mzindawu, chifukwa cha Ine mwini ndiponso chifukwa cha pangano ndi mtumiki wanga Davide!”
36 Aa le nionjom-beo ty anjeli’ Iehovà nanjamañe ty Rai-hetse-tsi-valo-ale-tsi-lime arivo an-tobe’ o nte-Asoreo; le ie nivañoñe maraindray t’indaty, hehe te fonga nidondom-pate ty ey.
Tsopano mngelo wa Yehova anapita ku misasa ya nkhondo ya ku Asiriya ndikukapha asilikali 185,000. Podzuka mmawa mwake anthu anangoona mitembo ponseponse!
37 Niavotse amy zao t’i Senkeribe mpanjaka’ i Asore, nimpoly vaho nitoboke e Ninevèy ao.
Choncho Senakeribu mfumu ya ku Asiriya anasasula misasa nʼkuchoka kubwerera kukakhala ku Ninive.
38 Le teo t’ie niloloke añ’ anjomba’ i Nisroke ndrahare’e ao, te namatsik’ aze am-pibara ty Adrameleke naho i Sarezere ana’e vaho nifiotse mb’ an-tane Ararate añe. I Esar-kadone ana’e ty nandimbe aze ho mpifeleke.
Tsiku lina, pamene ankapembedza mʼnyumba ya mulungu wake, Nisiroki, ana ake awiri, Adirameleki ndi Sarezeri anamupha ndi lupanga, ndipo anathawira mʼdziko la Ararati. Ndipo mwana wake Esrahadoni analowa ufumu mʼmalo mwake.

< Isaia 37 >