< Hosea 14 >
1 Ry Israele, mimpolia mb’am’ Iehovà Andrianañahare’o; fa nampihotrake azo o hakeo’oo.
Iwe Israeli bwerera kwa Yehova Mulungu wako. Machimo anu ndi amene akugwetsani!
2 Andeso saontsy, le mibaliha mb’am’Iehovà: ano ty hoe: Fonga afaho o hakeoo, rambeso an-kasoa, vaho hengae’ay ty banian-tsoñi’ay.
Bweretsani zopempha zanu ndipo bwererani kwa Yehova. Munene kwa Iye kuti, “Tikhululukireni machimo athu onse ndi kutilandira mokoma mtima, kuti tithe kukuyamikani ndi mawu a pakamwa pathu.
3 Tsy haharombak’ anay t’i Asore; izahay tsy hiningitse an-tsoavala, le tsy hanao ty hoe amo sata-pità’aio: Ry ndrahare’ay. Fa ama’o ty hahaoniña’ ty bode-rae fiferenaiñañe.
Asiriya sangatipulumutse; ife sitidzakwera pa akavalo ankhondo, sitidzanenanso kuti, ‘Milungu yathu’ kwa zimene manja athu omwe anazipanga, pakuti ndinu amene mumachitira chifundo ana amasiye.”
4 Ho jangañeko ty fidisa-voli’ iareo; hikokoako an-tsatrin-tro, fa mitolike ty habosehako.
Ine ndidzachiza kusakhulupirika kwawo ndipo ndidzawakonda mwaufulu pakuti ndaleka kuwakwiyira.
5 Hanahake ty zono am’ Israele iraho; ie hidorenake hoe antake mandriake, vaho hirifondrifoñe hoe Libanone.
Ndidzakhala ngati mame kwa Israeli Ndipo iye adzachita maluwa ngati kakombo. Adzazika mizu yake pansi ngati mkungudza wa ku Lebanoni;
6 Handrevake o ra’eo, naho hanahake ty andramahe ty enge’e, vaho hoe Libanone ty harifondrifo’e.
mphukira zake zidzakula. Kukongola kwake kudzakhala ngati mtengo wa olivi, kununkhira kwake ngati mkungudza wa ku Lebanoni.
7 Himpoly iaby o mialok’ ama’eo; ho tolorañ’ aiñe manahake i ampembay, le hiraorao hoe vahe, vaho handrifondrifoñe hoe ty hamañiran-divai’ i Libanone.
Anthu adzakhalanso mu mthunzi wake. Iye adzakula bwino ngati tirigu. Adzachita maluwa ngati mphesa ndipo kutchuka kwake kudzakhala ngati vinyo wochokera ku Lebanoni.
8 Le hanao ty hoe t’i Efraime: Hanoeko inoñe ka o samposampoo? Fa nitsanoñeko naho nijiloveko, Manahake ty kile maindoñe ama’o iraho, amako ty aharendreha’o voa.
Efereimu adzati, “Ndidzachita nawonso chiyani mafano? Ine ndidzamuyankha ndi kumusamalira. Ine ndili ngati mtengo wa payini wobiriwira; zipatso zako zimachokera kwa Ine.”
9 Ee te hahafohiñe o raha zao ty mahihitse, naho haharendreke o mahilalao. Amy te vantañe o lala’ Iehovào, ie orihe’ o vañoñeo, fe itsikapia’ o miolao.
Ndani ali ndi nzeru? Adzazindikire zinthu izi. Ndani amene amamvetsa zinthu? Adzamvetse izi. Njira za Yehova ndi zolungama; anthu olungama amayenda mʼmenemo, koma anthu owukira amapunthwamo.