< Genesisy 23 >

1 Zato tsi-roapolo fito’amby taoñe ty haantera’ i Sarà, ty taon-kavelo’ i Sarà,
Sara anakhala ndi moyo zaka 127.
2 ie nivilasy e Kiriàte-arbà (toe i Kebròne) an-tane’ Kanàne ao; le nimbeo t’i Avrahame handala i Sarà vaho hirovetse aze.
Anamwalirira ku Kiriyati-Araba, kumeneku ndi ku Hebroni, mʼdziko la Kanaani, ndipo Abrahamu anapita kukakhuza maliro a Sara, namulirira.
3 Niongak’ amy vilasi’ey t’i Avrahame vaho nisaontsy amo nte-Kheteo, ami’ty hoe,
Kenaka Abrahamu ananyamuka pamene panali mtembo wa mkazi wakepo kupita kukayankhula ndi anthu a ku Hiti. Ndipo anati,
4 Renetane naho mpañialo ama’ areo iraho; anoloro hanañañe ama’ areo handentehako i vilasikoy tsy ho aolom-pihaino.
“Ine ndine mlendo wongoyendayenda kwanu kuno. Bwanji mundigulitse malo woti akhale manda kuti ndiyikepo thupi la mkazi wanga.”
5 Le hoe ty natoi’ o nte-Kheteo amy Avrahame,
Anthu a ku Hiti aja anamuyankha Abrahamu kuti,
6 Ijanjiño roandriako; Mpifeleke ama’ay irehe. Alenteho an-kibory lengo’e ama’ay i vilasi’oy, tsy ia ama’ay ty hitañe azo amy lona’ey tsy handeveña’o i vilasi’oy.
“Tatimverani mbuye wathu, inu ndinu mwana wa mfumu wamkulu pakati pathu. Chonde ikani thupi la mkazi wanu mʼmanda aliwonse amene mungafune. Palibe mmodzi wa ife amene adzakukanizani manda ake kuti musayike mkazi wanu.”
7 Niongake t’i Avrahame vaho nibokok’ am’ ondati’ i taneio, amo ana’ i Kheteo,
Tsono Abrahamu anayimirira naweramira anthu a dziko la Hiti aja
8 le nisaon­tsia’e ty hoe, Naho no’areo ty handentehako tsy ho aolom-pihainoko i vilasikoy, le janjiño, vaho halalio t’i Efrone ana’ i Tsokare
nati, “Ngati mwaloladi kuti ndiyike mkazi wanga kuno, ndiye ndimvereni. Mundipemphere kwa Efroni mwana wa Zohari
9 ty hanolora’e ahiko i lakato’ i Makpelà ama’ey; i añ’ ila’ i tete’eiy. Ami’ty vola-foty do’e ty hanolora’e ahy ho fanañako añivo’ areo ao ho fandentehako.
kuti andigulitse phanga la Makipela, limene lili kumapeto kwa munda wake. Mumupemphe kuti andigulitse pamtengo wake ndithu inu mukuona kuti akhale manda.”
10 Niam­besatse añivo’ o nte-Kheteo t’i Efrone; vaho hoe ty natoi’ i Efrone nte-Khete amy Avrahame am-pijanjiña’ ze hene nte-Khete mpiheo mb’an-dalam-bei’ i rovaio:
Pamenepo nʼkuti Efroni Mhiti ali pomwepo pakati pa anthuwo amene anabwera ku chipata cha mzindawo. Ndipo onse akumva anamuyankha Abrahamu
11 Aiy! ry Androanavio: Janjiño iraho, fa omeiko azo i tonday, naho atoloko azo i lakato ama’ey. Añatrefa’ o ana’ ondatiko etoañe ty anolorako azo; aleveño i vilasi’o.
nati, “Ayi mbuye wanga tandimverani, ine ndikukupatsani mundawo ndiponso phanga limene lili mʼmenemo. Ndikukupatsani malowa pamaso pa anthu a mtundu wanga. Chonde ikani mtembo wamkazi wanu.”
12 Aa le nibokok’ añatrefa’ ondati’ i taneio t’i Avrahame,
Apo Abrahamu anaweramanso mwaulemu pamaso pa anthu a mʼdzikolo
13 vaho nanao ty hoe amy Efrone am-pijanjiña’ ondati’ i taneio, Aa naho mete le janjiño o ahikoo! Hitolo­rako drala amy tetekey; andrambeso amako le haleveko ao i vilasikoy.
ndipo anthu onse akumva Abrahamu anati kwa Efroni, “Ngati kungatheke, chonde ndimvereni. Ine ndichita kugula mundawu. Landirani ndalama za mundawu kuti ine ndiyike mkazi wanga mʼmenemo.”
14 Nanoiñe i Avrahame t’i Efrone ami’ty hoe,
Koma Efroni anamuyankha Abrahamu nati,
15 O talèko, Inao; mañeva 400 sekelem-bolafoty i taney, fa inon-jay añivon-tika? Aleveño i vilasi’oy.
“Mundimvere mbuye wanga; mundawo mtengo wake ndi masekeli asiliva okwana 400. Koma zimenezo nʼchiyani pakati pa ine ndi inu? Ikani mtembo wa mkazi wanu.”
16 Niantofa’ i Avrahame t’i Efrone le linanja’e amy Efrone i volafoty tsinara’e am-pijanjiña’ o nte-Kheteoy, i sekele volafoty 400 an-danjam-pandetake rey.
Abrahamu anavomera mtengo umene ananena Efroni Ahiti onse akumva ndipo anamuwerengera masekeli asiliva okwana 400 monga mwa mtengo wa ndalama umene amalonda a nthawi imeneyo ankagwiritsa ntchito.
17 Aa le tsitsike voalily ty tonda’ i Efrone e Makpelà ao atiñana’ i Mamrè añe, i tetekey reketse ty lakato’e ao, naho ze hatae amy tetekey naho ze mifahetse amy taney,
Choncho munda wa Efroni wa ku Makipela umene unali kufupi ndi Mamre, kuphatikiza munda, phanga linali mʼmenemo pamodzi ndi mitengo yonse ya mʼmundamo, zinaperekedwa
18 amy Avrahame ho fanaña’e añatrefa’ o ana’ i Kheteo, aolo’ ze mpimoak’ an-dalambei’ i rovay.
kwa Abrahamu ngati chuma chake pamaso pa anthu onse a ku Hiti amene anabwera ku chipata cha mzindawo.
19 Añe izay le naleve’ i Avrahame amy lakato an-tete’ i Makpelày miatreke i Mamrè (toe i Khebrone) an-tane Kanàne ao t’i Sarà.
Zitatha izi, Abrahamu anayika mkazi wake Sara mʼphanga la mʼmunda wa ku Makipela, kufupi ndi ku Mamre (kumene ndi ku Hebroni) mʼdziko la Kanaani.
20 Songa pinate’ o ana’ i Kheteo ho a i Avrahame i tonday rekets’ i lakato ama’e ao ho fandetehañe.
Choncho Ahiti anapereka munda pamodzi ndi phanga la mʼmenemo kwa Abrahamu kuti akhale manda.

< Genesisy 23 >