< Ezekiela 8 >

1 Ie tamy andro faha-lime’ i volam-pahaene’ i taom-pahaeneñey, izaho nitobok’ an-kibohoko ao, naho niambesatse aoloko eo o roandria’ Iehodào, te niheo amako ty fità’ Iehovà Talè.
Tsiku lachisanu la mwezi wachisanu ndi chimodzi, mʼchaka chachisanu ndi chimodzi, ndinakhala mʼnyumba mwanga pamodzi ndi akuluakulu a ku Yuda. Tsono mphamvu za Ambuye Yehova zinandifikira.
2 Aa le naheoko ty manahake vinta’ ondaty, naho hoe afo ty ambane’ o toha’eo, vaho hoe fireandrean-torisìke vinañe ty ambone’ o toha’eo.
Nditayangʼana ndinangoona chinthu chooneka ngati munthu. Kuchokera pamene pamaoneka ngati chiwuno chake kumatsika mʼmunsi anali ngati moto, ndipo kuchokera mʼchiwuno kukwera mmwamba amaoneka mowala ngati mkuwa wonyezimira.
3 Nahiti’e amako ty nanahake fitàñe naho rinambe’e iraho ami’ty orim-bòloko; naho naonjo’ i Tiokey añivo’ ty tane toy naho i likerañey vaho nendese’e añ’ aroñaron’ Añahare mb’e Ierosa­laime mb’amy fimoahañe an-kiririsa añate’e miatrek’ avaratsey mb’eo, amy fitoboha’ i sarem-pamarahiañe manigìke farahieñeiy,
Iye anatambasula chinthu chooneka ngati dzanja ndipo anagwira tsitsi la pamutu panga. Nthawi yomweyo Mzimu unandikweza mlengalenga. Tsono ndikumachita ngati ndikuona Mulungu kutulo, Mzimu uja unapita nane ku Yerusalemu nundiyika pa khomo la chipata chamʼkati choyangʼana kumpoto. Kumeneko kunali fano limene limaputa mkwiyo wa Mulungu.
4 le ingo te tao ty engen’ Añahare’ Israele, manahake i aroñaroñe nitreako a montoñe añey.
Kumeneko ndinaona ulemerero wa Mulungu wa Israeli ngati momwe ndinaonera mʼmasomphenya mʼchigwa muja.
5 Le hoe re tamako, O ana’ ondatio, ampiandrao mañavaratse o fihaino’oo. Aa le niandra nañavaratse iraho, le inge, avara’ i fimoaham-ban-kitreliy, an-tsari­rañe eo i sarem-pamarahiañey.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tayangʼana kumpoto.” Choncho ndinayangʼana kumpoto ndipo ndinaona pa khomo la chipata pafupi ndi guwa lansembe ndinaona fano loputa mkwiyo wa Mulungu lija.
6 Le hoe re tamako, O ana’ ondatio, isa’o hao o anoe’ iereoo? o hativañe jabajaba anoe’ i anjomba’ Israele atoa handroahañ’ ahy lavitse i toeko miavakeio? F’ie hahaisake hativañe lombolombo izay.
Ndipo Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuona zimene akuchitazi, zonyansa zazikulu zimene Aisraeli akuchita kuno, zinthu zondichotsa Ine kumalo anga opatulika? Koma iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri.”
7 Aa le nendese’e mb’an-dala’ i kiririsay; ie nenteako, le ingo ty hirike amy rindriñey.
Kenaka Iye anandipititsa ku khomo lolowera ku bwalo la Nyumba ya Mulungu. Nditayangʼanitsitsa ndinangoona dzenje pa khomapo.
8 Le hoe re amako, O ana’ ondatio, halio o rindriñeo; aa ie nihalieko i rindriñey, hehe ty lalañe.
Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano bowola pa khomapo.” Ndinabowoladi pa khomapo ndipo ndinapezapo khomo.
9 Le hoe re amako, Miheova, hahaisake ty haleoran-kativañe anoe’ iareo am-po’e ao.
Ndipo Yehova anandiwuza kuti, “Lowa, ndipo ona zinthu zonyansa zimene akuchita pamenepa.”
10 Aa le nimoahako vaho nahatrea, te ingo nanitsike i rindriñey ty sare-sokitse ze karazan-draha milaly naho biby mampangorìñe naho ze fonga samposampo’ i anjomba’ Israeley,
Motero Ine ndinalowa ndi kuyangʼana, ndipo ndinaona pa makoma onse zithunzi za zinthu zosiyanasiyana zokwawa pansi, za nyama zonyansa ndiponso za mafano onse amene Aisraeli ankapembedza.
11 le nijohañe añatrefa’ irezay eo ty androanavy fitompolo’ i anjom­ba’ Israeley, naho añivo’ iereo eo ty nijohaña’ Iaazanià ana’ i Safane, songa fitàñe amam-pañembohañe vaho nionjoñe mañambone ty rahon-katoen-emboke nilodolodo.
Patsogolo pa zimenezi panayima akuluakulu makumi asanu ndi awiri a Aisraeli, ndipo Yaazaniya mwana wa Safani anali atayima pakati pawo. Aliyense wa iwo anali ndi chofukizira lubani mʼdzanja lake ndipo utsi wa fungo lokoma la lubani unkafuka.
12 Le hoe re tamako, O ana’ondatio, isa’o hao o anoe’ o androanavin’ anjomba’ Israeleo añ’ieñeo, songa ondaty an-dakaton-tsare ao? fa hoe iereo, Tsy mahavazoho an-tika t’Iehovà; fa naforintse’ Iehovà ty tane toy.
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waona zimene akuluakulu a Aisraeli akuchita mu mdima, aliyense akupembedza fano lakelake mʼnyumbamo? Iwo akuti, ‘Yehova sakutiona; Yehova walisiya dziko!’
13 Natovo’e ty hoe amako: Mitoliha indraike, hahaoniñe t’ie manao hativañe mandako izay.
Iye anandiwuzanso kuti, ‘Iwe udzawaonanso akuchita zinthu zonyansa kwambiri.’”
14 Nente’e amy zao iraho mb’ amy fimoahañe an-tsariran’ anjomba’ Iehovà mitolik’ avaratsey mb’eo, le hehe ty rakemba maro miambesatse eo mirovetse amy Tamoze.
Kenaka anapita nane pa khomo la ku khomo la chipata cha Nyumba ya Mulungu choyangʼana kumpoto, ndipo kumeneko ndinaona akazi ena atakhala pansi, akulira mulungu wawo wotchedwa Tamuzi.
15 Le hoe re amako, O ana’ ondatio, oni’o hao zao? aa le mitoliha in­draike hahaoniñe mandikoatse izay.
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi ukuziona zimenezi? Iwe udzaona zinthu zimene zili zonyansa kwambiri kuposa izi.”
16 Aa le nendese’e mb’an-kiririsa añate’ i anjomba’ Iehovày, le hehe ty lahilahy roapolo-lim’ amby varañe am-pimoahañe an-kivoho’ Iehovà eo, añivo’ ty lapalapa naho ty kitrely, miamboho amy kivoho’ Iehovà, mitolik’ atiñanañe ty lahara’ iareo, mijoro amy masoàndroy.
Kenaka Iye anapita nane mʼkati mwa bwalo la Nyumba ya Yehova. Kumeneko ku khomo lolowera ku Nyumba ya Yehova pakati pa khonde ndi guwa lansembe, panali amuna 25. Anafulatira Nyumba ya Mulungu wa Yehova ndipo nkhope zawo zinaloza kummawa, ndipo ankapembedza dzuwa choyangʼana kummawa.
17 Le hoe re amako, Mahaoniñe v’iheo, ana’ ondatio? Raha maivañe amy anjomba’ Iehodày hao ty anoe’ iereo o hativañe anoe’ iereo atoañeo? te tsitsife’ iereo fikatramoañe ty tane mbore mibalike hanigìke ty habosehako, ie mitoho-tseva añ’oro’e eo.
Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi waziona zimenezi? Kodi nʼchinthu chopepuka kuti anthu a ku Yuda azichita zonyansa zimene akuchitazi pano? Kodi afike mpaka pomafalitsa za ndewu mʼdziko lonse? Iwotu akuwutsa ukali wanga. Akundipsetsa mtima ndi zochita zawo!
18 Aa le Izaho ka ty hanolotse leveleve; le tsy hiheve ty masoko, vaho tsy hiferenaiñako, le ndra t’ie mipoña-toreo an-tsofiko ao, tsy hanoin-dRaho.
Choncho Ine ndidzawalanga ndili wokwiya. Sindidzawamvera chisoni kapena kuwaleka. Ngakhale atandifuwulira mʼmakutu mwanga sindidzawamvera.”

< Ezekiela 8 >