< Ezekiela 37 >

1 Tàmako amy zao ty fità’Iehovà, le nendese’e an-Tio’ Iehovà vaho navotra’e añivo’ ty vavatane lifo-taolañe,
Dzanja la Yehova linali pa ine, ndipo Mzimu wa Yehova unandinyamula nʼkukandikhazika pakati pa chigwa. Chigwacho chinali chodzaza ndi mafupa.
2 le nampañariarie’e mb’eo mb’eo am’ iereo ao, le nizoeko te maro ty ambone’ i taney vaho nivata’e maike.
Yehova anandiyendetsa uku ndi uku pakati pa mafupawo. Mafupawo anali ochuluka kwambiri mʼchigwa monsemo ndipo anali owuma kwambiri.
3 Le hoe re amako, O ana’ondatio, mete ho veloñe hao o taolañe reo? Le hoe ty natoiko: Ihe ry Iehovà Talè ro maharofoanañe.
Tsono Yehova anandifunsa kuti, “Iwe mwana wa munthu, kodi mafupa amenewa angakhalenso ndi moyo?” Ndinayankha kuti, “Inu Ambuye Yehova, Inuyo nokha ndiye mukudziwa.”
4 Le hoe re amako: Mitokia amo taolañeo, ami’ty hoe: O ry taola-maikeo, Inao ty tsara’ ­Iehovà.
Pamenepo anandiwuza kuti, “Lengeza kwa mafupa amenewa ndi kuwawuza kuti amve mawu a Ine Yehova!
5 Hoe ty nafè’ Iehovà Talè amo taolañe retoañe: Inao! t’ie hampizilihañe tioke vaho ho veloñe;
Uwawuze kuti zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena kwa mafupa ndi izi: Ndidzawuzira mpweya mwa inu, ndipo mudzakhalanso ndi moyo.
6 le hapetako ama’ areo ty lahin-ozatse naho handafihako nofotse, naho hasaroko holitse naho hajoko ama’ areo ao ty kofòke, le ho veloñe, vaho ho fohi’ areo te Izaho Iehovà.
Ndidzakupatsani mitsempha ndi mnofu. Ndiponso ndidzakukutani ndi khungu. Pambuyo pake ndidzawuzira mpweya mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
7 Toe nitokiako amy nandiliañe ahiy, aa naho nitoky, inay ty feo, hehe te nikarankaràñe vaho nifamitrañe o taolañeo, taolañe ami’ty taolañe.
Ndipo ndinanenera monga anandilamulira. Ndipo pamene ndinkanenera, ndinamva gobedegobede, ndipo mafupa aja anayamba kulumikizana, fupa ku fupa linzake.
8 Ie nenteako, hehe te aman-dahin-ozatse, naho nipetak’ am’ iereo ty nofotse vaho nisaroña’ ty holitse f’ie mboe tsy aman-kofòke.
Ine ndinayangʼana, ndipo mitsempha ndi mnofu zinabwera pa mafupawo ndipo khungu linaphimba pamwamba pake, koma munalibe mpweya mwa iwo.
9 Le hoe re amako, Mitokia amy tiokey; itokio ry ana’ ondatio, vaho ano ty hoe i tiokey, Hoe ty nafè’ Iehovà Talè: Mb’ etoa boak’ amo tioke efatseo, ry Tioke, le mikofoha amo zinamañe reo, ho veloñe.
Tsono Yehova anandiwuza kuti, “Nenera kwa mpweya, nenera iwe mwana wa munthu ndi kuwuza mpweya mawu a Ine Ambuye Yehova kuti, ‘Bwera kuno iwe mpweya. Bwera kuchokera ku mbali zonse zinayi ndi kudzawuzira anthu ophedwawa kuti akhalenso ndi moyo.’
10 Aa le nitokiako amy namantoha’e ahiy, naho nizilike am’iereo ao ty tioke nahaveloñe vaho nitroatse am-pandia’e ty lian-dahin-defoñe mitozantozañe.
Choncho ndinanenera monga anandilamulira ndipo mpweya unalowa mwa iwo; apo anthu akufawo anakhala ndi moyo, nayimirira ndipo linali gulu lalikulu lankhondo.”
11 Le hoe re amako, O ana’ondatio, Toe o anjomba’ Israele iabio o taolañeo; Heheke, hoe iereo, fa mikàntañe o taola’aio, naho motso ty fitamà’ay, vaho vata’e naitoañe.
Kenaka Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, mafupa awa ndi nyumba yonse ya Israeli. Iwo amanena kuti, ‘Mafupa athu awuma ndipo chiyembekezo chathu chatayika, ife tawonongeka!’
12 Aa le itokio ami’ty hoe; Hoe ty nafè’ Iehovà Talè, Heheke ondatikoo, manokake o kibori’ areoo iraho vaho hakareko an-kibori’ areo ao, mb’an-tane’ Israele mb’eo,
Nʼchifukwa chake nenera ndi kuwawuza kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Inu anthu anga, ndidzafukula manda anu, ndipo ndidzakutulutsanimo ndi kukubwezerani ku dziko la Israeli.
13 le ho fohi’ areo te Izaho Iehovà, ie sokafeko o lona’ areoo, ry ondatikoo, naho aka­reko boak’an-kibori’ areo ao,
Ndipo inu, anthu anga, mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, pamene ndidzafukula manda anu ndikukutulutsanimo.
14 naho hakofoko ama’ areo ao ty Tioko, vaho ho veloñe, le hampitofàko an-tane’ areo eo; ie amy zay ro hahafohiñe te Izaho Iehovà ty nitsara naho nitoloñe, hoe t’Iehovà.
Ine ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo mudzakhalanso ndi moyo. Pambuyo pake ndidzakulowetsani mʼdziko lanulanu. Choncho mudzadziwa kuti Ambuye Yehova ndayankhula zimenezi, ndipo ndidzazichitadi. Ndikutero Ine Yehova!’”
15 Niheo amako indraike ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe:
Yehova anandiyankhula kuti:
16 Ihe ry ana’ ondatio, mandrambesa kobaiñe vaho isokiro ty hoe: Ho a Iehodà, naho o ana’ Israele rañe’eo; le mandrambesa kobaiñe tovo’e, le isokiro ty hoe: Ho a Iosefe, ty kobai’ i Efraime naho i hene anjomba’ Israele mpiama’ey:
“Iwe mwana wa munthu, tenga ndodo ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Yuda ndi Aisraeli oyanjana nawo.’ Utengenso ndodo ina ndipo ulembepo kuti, ‘Ndodo ya Efereimu, ndiye kuti fuko la Yosefe ndi Aisraeli onse oyanjana nawo.’
17 le avitraño, ty raik’ amy raikey soa te ho raike; vaho ho raik’ am-pità’o ao.
Ulumikize ndodo ziwirizi kuti zikhale ndodo imodzi mʼdzanja lako.
18 Aa ie mi­saontsy ama’o o ana’ ondatikoo, hanao ty hoe: Tsy hatoro’o anay hao ty lengo’e?
“Anthu a mtundu wako akadzakufunsa tanthauzo la zimenezi
19 Le ty hoe ty ho asa’o am’ iereo: Inao ty nafè’ Iehovà Talè: Oniño te ho rambeseko ty kobai’ Iosefe boak’ am-pità’ i Efraime rekets’ o fifokoa’ Israele rañe’eo naho hatraoko ama’e naho haharoko amy kobai’ Iehodà ho kobaiñe raike, vaho ho raik’ an-tañako ao.
iwe udzawawuze mawu awa a Ine Ambuye Yehova akuti, ‘Ine ndidzatenga ndodo ya Yosefe imene ili mʼdzanja la Efereimu, ndi ya mafuko a Aisraeli oyanjana naye, ndi kuyilumikiza ku ndodo ya Yuda, kuti zikhale ndodo imodzi, ndipo zidzakhaladi ndodo imodzi mʼdzanja langa!’
20 Aa le ho am-pità’o ao añatrefam-pihaino’ iareo eo i kobaiñe hisokira’o rey,
Ndodo ziwiri zimene udzalembepozo zikadzakhala mʼmanja mwako pamaso pa anthu onse,
21 le hanoa’o ty hoe, Hoe ty nafè’ Iehovà Talè, Ingo ho rambeseko amo kilakila’ndatio o ana’ Israeleo, amy nomba’ iareo añey, le hatontoko boak’ etia naho eroa vaho hampoliko mb’an-tane’ iareo ao.
udzawawuze kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzawachotsa Aisraeli pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapita ku ukapolo. Ndidzawasonkhanitsa kuchokera ku mbali zonse ndi kubwera nawo ku dziko lawolawo.
22 le hanoeko fifeheañe raike iereo am-bohibohi’ Israeleo ao; naho mpanjaka raike ty ho mpanjaka’ iareo iaby; le lia’e tsy ho fifelehañe roe ka iereo vaho tsy ho zaraeñe ho fifeheañe roe ka.
Ndidzawasandutsa mtundu umodzi mʼdzikomo, pa mapiri a Israeli. Padzakhala mfumu imodzi yowalamulira, ndipo sadzakhalanso mitundu iwiri kapena kugawikana maufumu awiri.
23 Tsy haniva-vatañe amo samposampo’eo naho amo raha veta’ iareoo naho amo fiolà’ iareo iabio ka iereo fa ho rombaheko amo kibohotse iaby nandilara’ iareoo naho ho lioveko ho ondatiko vaho ho Andrianañahare’ iareo iraho.
Sadzadziyipitsanso ndi mafano awo, kapena ndi zinthu zawo zonyansa, kapenanso ndi ntchito zawo zoyipa zilizonse. Ndidzawapulumutsa ku machimo awo onse ndi kuwayeretsa. Choncho adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
24 Ho mpanjaka hifehe iareo t’i Davide mpitoroko, le ho raik’ avao ty mpiara’ iareo; hañaveloa’ iareo o lilikoo naho hañambeñe vaho hitana o fañèkoo.
“‘Mtumiki wanga Davide adzakhala mfumu yawo, motero onsewa adzakhala ndi mʼbusa mmodzi. Iwo adzatsatira malamulo anga ndipo adzasamalira kusunga malangizo anga.
25 Himoneña’ iareo i tane natoloko am’ Iakobe mpitorokoy, i nimoneñan-droae’ areoy; toe himoneñe ao iereo rekets’ o ana’eo naho o anan’ana’eo nainai’e kitro añ’afe’e, le ho mpifehe’ iareo nainai’e t’i Davide mpitoroko.
Iwo adzakhala mʼdziko limene ndinalipereka kwa mtumiki wanga Yakobo, dziko limene makolo anu ankakhalamo. Iwo ndi ana awo pamodzi ndi zidzukulu zawo adzakhala kumeneko ndipo Davide adzakhala mfumu yawo kwa muyaya.
26 Mbore hanoako fañinam-panintsiñañe, ho fañina tsy modo; hajadoko iereo naho hampidobodoeko vaho haoreko ho nainai’e añivo’ iareo ao i toeko miavakey.
Ndidzachita nawo pangano lamtendere; lidzakhala pangano lamuyaya. Ndidzawakhazikitsa ndi kuwachulukitsa, ndipo ndidzayika malo anga opatulika pakati pawo kwamuyaya.
27 Ho am’ iereo ao i kivohokoy, le Izaho ty ho Andrianañahare’ iareo vaho h’ondatiko iereo.
Nyumba yanga yokhalamo idzakhala pakati pawo; Ine ndidzakhala Mulungu wawo, ndipo iwo adzakhala anthu anga.
28 Le ho fohi’ o kilakila’ ndatio te Izaho Iehovà ty mampiavake Israele ie añivo’ iereo ao nainai’e i toeko miavakey.
Pamenepo anthu a mitundu ina adzadziwa kuti Ine Yehova ndiye amene ndimasandutsa Israeli kukhala woyera, pamene malo anga opatulika adzakhala pakati pawo kwamuyaya!’”

< Ezekiela 37 >