< Ezekiela 36 >

1 O ana’ondatio, Itokio ami’ty hoe o vohi’ Israeleo: O ry vohi’ Israeleo, janjiño ty tsara’ Iehovà.
“Iwe mwana wa munthu, yankhula kwa mapiri a Israeli ndipo unene kuti, ‘Inu mapiri a Israeli, imvani mawu a Yehova.’
2 Hoe ty nafè’ Iehovà Talè: Kanao nanao ty hoe ty ama’o i rafelahiy: Hede! fa amantika o haboañe haehaeo;
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mdani wanu ankanena kuti, ‘Aa! Dziko lamapiri lakalekale lija lasanduka lathu.’
3 Le itokio ami’ty hoe: Hoe ty nafè’ Iehovà Talè: Amy t’ie nampangoakoahe’ iereo naho nagedra’ iereo añ’ ila’o iaby soa te ho fanaña’ o kilakila’ ndatio, naho fa rinambem-pivimbim-pitolom-bolañe vaho nifosae’ ondatio;
Choncho nenera ndipo uwawuze kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anakusakazani ndi kukuponderezani ku mbali zonse motero kuti munakhala mʼmanja mwa anthu a mitundu ina yonse ndipo anthu ankakunenani ndi kukunyozani,
4 ie amy zao, ry vohi’ Israele, janjiño ty tsara’ Iehovà Talè: Hoe t’Iehovà Talè amo vohitseo naho amo haboañeo, amo sakao, amo vavataneo, amo mangoakoakeo naho amo tane babangoañeo vaho amo rova naforintseñeo, ie fitsindroha’ o sehangan-kilakila’ ondaty mañohok’ azeo,
choncho, inu mapiri a Israeli, imvani zimene Ine Ambuye Yehova ndikuwuza mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa, mabwinja ndi mizinda yosiyidwa imene yakhala ikufunkhidwa komanso kunyozedwa ndi anthu a mitundu ina okuzungulirani.
5 aa le inao ty nafè’ Iehovà Talè: Toe nivolañeko ami’ty afom-piforoforoam-pamarahiako o kilakila’ondaty ila’eo naho i Edome iaby, o nitavañe i taney ho aze an-kafalean-troke iabio, ami’ty firengevoham-pañiria’e, hanifike aze añe ho tsindrokeo.
Tsono Ine Ambuye Yehova ndikuti: Mu mkwiyo wanga woopsa ndinayankhula kuyimba mlandu mitundu ina yonse ya anthu makamaka a ku Edomu. Iwowa mwa chimwemwe chodzaza tsaya ndi mwa nkhwidzi analanda dziko langa ndi kulisandutsa lawo ndi kutengeratu dziko la msipu kukhala lawo.’
6 Aa le mitokia mb’an-tane’ Israele naho misaontsia amo vohitseo naho amo haboañeo naho amo sakao vaho amo vavataneo, ty hoe: Inao ty nafè’ Iehovà Talè: Ingo te nivolañe am-parahy naho foroforo iraho ty amy hasalarañe nifeaha’o vave,
Nʼchifukwa chake, lengeza ku dziko la Israeli, ndipo uwuze mapiri ndi magomo, zigwembe ndi zigwa kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndikuyankhula ndi mtima wokwiya kwambiri chifukwa inu munalandira chitonzo cha anthu a mitundu ina.’
7 aa le hoe ty nafè’ Iehovà Talè: Fa nañonjon-tsirañe Raho, toe hivave ty hasalara’e o kilakila’ndaty mañohok’ anahareoo.
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndikulumbira nditakweza dzanja langa kuti mitundu ya anthu idzatozedwanso.
8 Inahareo ka, ry vohi’ Israeleo, habarabijo’ areo o tsampa’o naho o voka’eo le mamokara ho am’ondatiko Israeleo, ie antitotse te hitotsak’eo.
“Koma Inu mapiri a Israeli mudzaphukanso nthambi ndipo mudzawabalira zipatso anthu anga a Israeli, pakuti ali pafupi kubwerera kwawo.
9 Ingo fa Mpiama’ areo iraho, naho hitolihako le ho trabaheñe vaho tongiseñe,
Taonani, Ine ndili mbali yanu ndipo ndidzakukomerani mtima. Mudzalimidwa ndi kudzalidwa.
10 le hampitomboeko ama’ areo t’ondaty, i hene anjomba’ Israeley, eka ie iaby; vaho songa himoneñañe o rovao, le hamboareñe o haran-koakeo.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha anthu anu, nyumba yonse ya Israeli. Mʼmizinda mudzakhalanso anthu ndipo mabwinja adzamangidwanso.
11 Hampitomboeko ama’areo ty ondaty naho hare, hiraorao naho hangetseketseke; naho hampimoneñako manahake i tama’areo haehaey, naho hanoeko soa te am-pifotora’ areo, vaho ho fohi’ areo te Izaho Iehovà.
Ndidzachulukitsa chiwerengero cha amuna pamodzi ndi ziweto zomwe, ndipo adzachuluka kwambiri ndi kubereka ana ambiri. Ndidzakhazika anthu mʼdzikomo monga analili kale, ndi kukulemeretsani kuposa kale. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
12 Hampañaveloeko ama’ areo t’indaty, toe ondatiko Israeleo, le ho fanaña’ iareo, ho lova’ iareo vaho tsy hampirovete’o anake ka henane zay.
Ndidzachititsa anthu kuyenda pa inu, ndiye kuti inu anthu anga Aisraeli. Iwowo adzakhazikika pa inu, ndipo inu mudzakhala cholowa chawo. Simudzalandanso ana awo.
13 Inao ty nafè’ Iehovà Talè: Amy t’ie manao ty hoe; Mampibotseke ondaty irehe vaho nampihontofe’o o fifehea’oo,
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Popeza anthu amanena kuti, ndiwe dziko limene limadya anthu ake ‘kulanda ana a mtundu wake,’
14 aa le tsy hampibotseke ondaty ka irehe, vaho tsy hampandalà’o ana-dahy ka o fifehea’oo, hoe t’Iehovà Talè.
nʼchifukwa chake, simudzadyanso anthu kapena kulanda ana a mtundu wako. Ine Ambuye Yehova ndikutero.
15 Mbore tsy hampijineko azo ka ty hasalara’ o kilakila’ ndatio naho tsy ho vavè’o ty inje’ ondatio vaho tsy hampitsikapie’o ka o fifehea’oo, hoe t’Iehovà Talè.
Sindidzakulolaninso kumva mnyozo wa anthu a mitundu ina, kapena kupirira kunyogodola kwawo kapenanso kupunthwitsanso anthu a mʼdziko lako. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.”
16 Niheo amako indraike ty tsara’ Iehovà manao ty hoe,
Yehova anandiyankhulanso kuti:
17 O ana’ ondatio, Fa nileore’ o sata’eo naho ty fitoloña’ iareo i anjomba’ Israele mimoneñe an-tane’ iareoy; niatrek’ ahy hoe fandeoran’ ampela am-piambolañe ty sata’ iareo.
“Iwe mwana wa munthu, pamene anthu a Israeli ankakhala mʼdziko lawolawo, analiyipitsa ndi makhalidwe awo ndiponso zochita zawo. Machitidwe awo pamaso panga anali onyansa pa zachipembedzo ngati msambo wa mkazi amene ali pa nthawi yake.
18 Aa le nadoako am’ iereo ty fifomboko ty amo lio nampiorihe’ iereo an-taneo, naho o samposampo nanivà’ iareo azeo;
Tsono ndinawalanga chifukwa cha magazi amene anakhetsa mʼdzikomo, ndiponso chifukwa anayipitsa dziko ndi mafano awo.
19 le nabaratsako amo kilakila’ ondatio vaho niparaitak’ amo fifeheañeo; o sata’iareoo naho o fitoloña’iareoo ty nizakako iareo.
Ndinawamwaza pakati pa anthu a mitundu ina ndipo anabalalikira mʼmayiko onse. Ndinawalanga molingana ndi makhalidwe awo ndi zochita zawo.
20 Aa ie nimoak’ amo kilakila’ ndatio, le tiniva’ iareo i añarako masiñey; ie nanoa’ ondatio ty hoe, Ondati’ Iehovà iretoañe, ie fa nienga i tane’ey.
Atafika kwa anthu a mitundu ina, kulikonse kumene anapitako, anayipitsa dzina langa loyera. Zinatero popeza anthu ponena za iwo ankanena kuti, ‘Awa ndi anthu a Yehova, komatu anachotsedwa ku dziko lake.’
21 Aa le nitretrezeko i añarako masiñe nitivae’ i anjomba’ Israeley amo kilakila’ndaty nañaveloa’eoy.
Koma Ine ndinkadera nkhawa dzina langa loyera, limene Aisraeli analiyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene anapitako.
22 Aa le saontsio ty hoe i anjomba’ Israeley, Inao ty nafè’ Iehovà Talè: Tsy ty ama’ areo ty anoako zao, ry anjomba’ Israeleo, fa ty amy añarako masiñe tiniva’ areo añivo’ o kilakila’ndaty nañaveloa’ areoo.
“Nʼchifukwa chake awuze Aisraeliwo kuti Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ine ndidzachita zimene ndidzachitezo osati chifukwa cha inuyo Aisraelinu ayi, koma chifukwa cha dzina langa, limene mwaliyipitsa pakati pa anthu a mitundu ina kumene munapitako.
23 Le ho masiñeko i añarako ra’elahiy, i tiniva’ areo añivo’ o kilakila’ ndatioy, i vineta’ areo anteñateña’ iereoy; vaho ho fohi’ o kilakila’ndatio te Izaho Iehovà, hoe t’Iehovà Talè, naho avahe’ areo añatrefam-pihaino’ iareo eo iraho.
Ndidzaonetsa chiyero cha dzina langa lotchuka, limene layipitsidwa pakati pawo. Anthu a mitundu inayo atadzazindikira kuti ndaonetsa kudzera mwa inu kuti dzina langa ndi loyera, iwo adzadziwanso kuti Ine ndine Yehova. Ndikutero Ine Ambuye Yehova.
24 Le ho rambeseko amo kilakila’ndatio nahareo, naho hatontoko boak’ amy ze hene fifelehañe, vaho ho enteko mb’an-tane’ areo mb’eo.
“Pakuti Ine ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina. Ndidzakusonkhanitsani kuchoka ku mayiko onse ndi kukubwezerani ku dziko lanulanu.
25 Le ho fitsezako rano malio, naho halio amo haleora’ areo iabio, vaho ho lioveko amo samposampo’ areoo.
Ndidzakuwazani madzi oyera, ndipo mudzakhala oyera mtima. Zonse zimene zimakuyipitsani zidzachoka. Ndidzakuyeretsani pochotsa mafano anu onse.
26 Ho tolo­rako arofo vao nahareo, naho hampizilihako troke vao; naho hafahako am-pañova’ areo ao i troke mamàtoy, vaho ho tolorako arofo nofotse.
Ndidzakupatsani mtima watsopano ndi kulowetsa mzimu watsopano mwa inu. Ndidzachotsa mwa inu mtima wanu wowuma ngati mwala ndi kukupatsani mtima wofewa ngati mnofu.
27 Aa le hajoko ama’ areo t’i Troko naho hampañoriheko o lilikoo soa te hambena’ areo o fañèkoo, hitoloña’ areo.
Ndipo ndidzayika Mzimu wanga mwa inu ndipo ndidzakuthandizani kutsatira malangizo anga ndi kukusungitsani mosamala kwambiri malamulo anga.
28 Le himoneña’ areo i tane natoloko aman-droae’ areoy naho ho ondatiko nahareo vaho ho Andrianañahare’ areo iraho.
Mudzakhala mʼdziko limene ndinapatsa makolo anu. Mudzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wanu.
29 Ho votsorako amo haleora’ areoo; naho ho tokaveko i ampembay hamokara’e vaho tsy halamako ama’ areo ty hasalikoañe.
Ndidzakupulumutsani ku zonse zokuyipitsani. Ndidzakuchulukitsirani tirigu ndipo sindidzakugwetseraninso njala.
30 Hampiregoregoeko ka o voan-kataeo, naho ty havokara’ o tetekeo, tsy hinjè’ ty kerè ka nahareo añivo’ o kilakila’ ndatio.
Ndidzachulukitsa zipatso za mʼmitengo yanu ndi zokolola za mʼmunda mwanu, kotero kuti simudzanyozedwanso pakati pa anthu a mitundu ina chifukwa cha njala.
31 Ho tiahi’ areo amy zao o sata-rati’ areoo naho o fitoloñañe tsy vokatseo, vaho ho heje’ areo vintañe am-pahaoniña’ areo eo ty fiai’ areo ty amo hakeo naho haloloa’ areoo.
Pamenepo mudzakumbukira makhalidwe anu oyipa ndi ntchito zanu zoyipa. Machimo anu ndi ntchito zanu zonyansa zidzakuchititsa nokha manyazi.
32 Tsy ty ama’ areo ty anoako izay, hoe t’Iehovà Talè, maharendreha; mimeñara naho misalara amo sata’ areoo, ry anjomba’ Israeleo.
Tsono dziwani kuti Ine sindidzachita zimenezi chifukwa cha inuyo ayi, ndikutero Ine Ambuye Wamphamvuzonse. Ndiyetu chitani manyazi ndipo mugwetse nkhope zanu, inu Aisraeli chifukwa cha makhalidwe anu!
33 Hoe ty nafè’ Iehovà Talè: amy andro nañaliovako anahareo amo fonga tahi’ areooy, fa hampimoneñako o rovao, vaho hamboareñe o tane hoakeo.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pa tsiku limene ndidzayeretse machimo anu onse, ndidzayikamonso anthu mʼmizinda yanu, ndipo ndidzamanganso nyumba pa mabwinja.
34 Ho rokafeñe i tane bangiñey, ie napoke ho ratraratra amo mpiary azeo;
Dziko limene linasanduka chipululu lizidzalimidwanso. Mʼmalo moti aliyense wopitamo alione dzikolo ngati chipululu tsopano adzaliona lolimidwa.
35 ie nanoeñe ty hoe: Nihambañe an-tane Edene ty tane liolio toy taolo; vaho ni-fatratse i rova mangoakoake naho bangiñe reroañe.
Iwo adzati, ‘Dziko ili, limene linali chipululu, lasanduka munda wa Edeni. Mizinda imene inali mabwinja osiyidwa ndi owonongedwa, tsopano ndi yotetezedwa ndi yokhalamo anthu.
36 Le ho fohi’ o kilakila’ ndaty nengañe mañohok’ anahareoo te Izaho Iehovà ty namboatse o niantoo, vaho nambole i niliolioy; Izaho Iehovà ty nitaroñe, Izaho ty hitoloñe.
Ndipo anthu a mitundu ina okhala pafupi nanu amene anatsala adzadziwa kuti Ine Yehova ndine amene ndinamanganso mizinda yowonongeka ndi kudzalanso zinthu zatsopano mʼmalo mʼmene munali chipululu. Ine Yehova ndayankhula ndipo ndidzazichitadi.’
37 Hoe ty nafè’ Iehovà Talè: Izay ty hitsoeha’ i anjomba’ Israeley t’ie hitoloñe, le ho maroeko hoe lia-raike.
“Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzalolanso Aisraeli kuti andipemphe zoti ndiwachitire: Ndidzachulukitsa anthu awo ngati nkhosa.
38 Manahake o añondry miavakeo, o añondry an-tsabadidam-pitalahoa’ Ierosalaimeo, ty hanitsifañe lia-rai’ ondaty o rova hoakeo; vaho ho fohi’ iareo te Izaho Iehovà.
Adzachulukadi ngati nkhosa zomwe ankapereka ngati nsembe ku Yerusalemu pa nthawi za chikondwerero. Choncho mizinda ya mabwinja idzadzaza ndi anthu. Zikadzatero adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”

< Ezekiela 36 >