< Ezekiela 35 >
1 Mboe niheo amako ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 O ana’ ondatio, atrefo ty vohi-tSeire vaho itokio,
“Iwe mwana wa munthu, yangʼana phiri la Seiri; yankhula moliyimba mlandu ndipo
3 ami’ty hoe: Hoe ty tsara’ Iehovà Talè: Ry Vohi-tSeire, atreatrèko irehe, vaho hatorakitsiko ama’o ty tañako hampangoakoahako azo ho tane bangý.
awawuze anthu a kumeneko kuti zimene ndikuyankhula Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu anthu a ku mapiri a Seiri ndikudana nanu. Ndidzatambasula dzanja langa kulimbana nanu, ndipo ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu.
4 Fonga ho rotsaheko o rova’oo le ho vahiny irehe vaho ho fohi’o te izaho Iehovà;
Mizinda yanu ndidzayisandutsa mabwinja, ndipo dziko lanu lidzasanduka chipululu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
5 amy t’ie nitan-keloke nainai’e naho nanolotse o ana’ Israeleo ami’ty haozaram-pibara amy andron-kekoheko’ iareoy, amy sam-pigadoñan-kaloloañey;
“Munali adani a Israeli nthawi zonse, ndipo munkalola kuti Aisraeli aphedwe pa nkhondo pa nthawi ya mavuto awo, pa nthawi imene chilango chawo chinafika pachimake.
6 kanao velon-dRaho hoe t’Iehovà Talè, le hañentseñako lio, hañoridañe azo ty lio; toe niheje’o ty lio’o, vaho lio ro hañotioty azo.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzakukanthani. Imfa idzakulondolani. Popeza sunadane nako kukhetsa magazi, imfa idzakulondola.
7 Le hampangoakoaheko naho ho babangoañeko t’i Seire, vaho haitoako ama’e ty miranga naho ty mimpoly.
Phiri la Seiri ndidzalisandutsa chipululu ndipo ndidzapha onse amene amapita nabwerera kumeneko.
8 Hatsefeko zamañe o vohi’eo, an-kaboa’o ey naho am-bavatane’o ao; vaho an-tsaka’o iaby ao ty hikorovoha’ o zinevom-pibarao.
Ndidzaza mapiri ake ndi mitembo. Ophedwa pa nkhondo adzagwera pa zitunda zanu, zigwa zanu ndi mʼmitsinje yanu yonse.
9 Hampangoakoaheko nainai’e naho tsy hatroatse ka o rova’oo; vaho ho fohi’o te Izaho Iehovà.
Ndidzasandutsa dziko lanu kukhala chipululu mpaka muyaya, ndipo mʼmizinda yanu simudzakhalanso anthu. Zikadzachitika izi mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
10 Amy te ihe nanao ty hoe, Ho ahiko i fifelehañe roe rey naho i tane roe rey, ho tavane’ay; fe tao t’Iehovà.
“Inu munanena kuti, ‘Mitundu iwiri iyi ya anthu, Yuda ndi Israeli, pamodzi ndi mayiko awo omwe idzakhala yathu.’ Munanena chomwechi ngakhale kuti Ine Yehova ndinali momwemo.
11 Aa kanao velon-dRaho hoe t’Iehovà Talè, le ho toloñeko amy haviñerañe naho amy fikirañañe nitoloña’o an-karafelahiañey, vaho ho fohi’ iereo te izaho ty nizaka azo.
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Pali Ine wamoyo, ndithu ndidzachita nanu monga munachita ndi anthu a ku Yuda ndi Israeli poonetsa mkwiyo wanu, nsanje yanu ndi chidani chanu pa iwo. Ndikadzakulangani mudzandidziwadi pakati panupo.
12 Le ho fohi’o te Izaho Iehovà ty nahatsanoñe ty fifosa nanoe’ areo amo vohi’ Israeleo ami’ty hoe: Kanao nengañe bangiñe, le natolotse antika habotseke.
Ndipo mudzadziwa kuti Ine Yehova ndinamva mawu anu onse onyoza amene munanena molimbana ndi mapiri a Israeli. Inu munati, ‘Mapiri a Israeli asanduka bwinja, ndipo aperekedwa kwa ife kuti tiwawononge.’
13 Niebotsebotse amako am-bava irehe, vaho nampitoabore’o rehake; hene tsinanoko.
Mawu anu amene munayankhula monyada kundinyoza Ine ndinawamva.
14 Hoe ty nafè’ Iehovà Talè: Toly ndra hirebeke ty tane-bey toy naho koaheko irehe,
Ine Ambuye Yehova ndikuti: Dziko lonse lapansi lidzasangalala pamene ndidzakusandutsani bwinja.
15 manahake ty nirebeha’o amy lovan-anjomba’ Israeley, t’ie nangoakoake; izay ka ty hanoako azo; ho bangìñe ka irehe, ry Vohi-Seire, naho i Edome iaby, eka ie iabike; vaho ho fohi’ iereo te Izaho Iehovà.
Monga momwe inu munasangalala pamene anthu anga Aisraeli anagwa, Inenso ndidzakuchitani chimodzimodzi. Udzasanduka bwinja, iwe Phiri la Seiri, iwe ndi dziko lonse la Edomu. Zikadzatero anthu onse adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”