< Ezekiela 2 >
1 nanao amako ty hoe, O ana’ ondatio, miongaha am-pandia, le hivolañako.
Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, imirira kuti ndiyankhule nawe.”
2 Aa ie nisaontsia’e le nimoak’ amako ty Tioke nampitroatse ahy an-tomboke naho tsinanoko i nitsara amakoy.
Pamene ankayankhula nane, Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa, ndipo ndinamva Iye akundiyankhula.
3 Le hoe re tamako, O ana’ondatio, hiraheko mb’ amo ana’ Israeleo irehe, mb’amo fifokoa mpiola niola amakoo; songa niola amako iereo naho o roae’eo, pake henanekeo.
Iye anati, “Iwe mwana wa munthu, Ine ndikukutuma kwa Aisraeli, mtundu wa anthu owukira umene wandiwukira Ine; Iwo ndi makolo awo akhala akundiwukira Ine mpaka lero lino.
4 Aa le hiraheko irehe mb’amo ana-dahy gan-tarehe naho fatra-poo, le hoe ty ho asa’o ama’e, Hoe ty nafe’ Iehovà Talè;
Ndikukutuma kwa anthu okanika ndiponso nkhutukumve. Ndikukutuma kuti akawawuze zimene Ine Ambuye Yehova ndikunena.
5 aa ke hijanjiñe iereo, he tsy hañaoñe, amy t’ie anjomba mpiola; fe ho oni’iareo te tañivo’iareo ao ty mpitoky.
Kaya akamva kaya sakamvera, pakuti iwo ndi anthu opanduka, komabe adzadziwa kuti mneneri ali pakati pawo.
6 Aa ihe ana’ ondatio, ko ihembaña’o, ko irevendreveña’o o saontsi’eo fa mpiola iereo, aa ndra te mpiama’o ty fatike naho hisatse, naho kalengo ty imoneña’o, ko hembaña’o o saontsi’eo, vaho ko miriatsandry aolo’e eo, fa akiba miola iereo.
Tsono iwe mwana wa munthu, usachite nawo mantha kapena kuopa zimene azikanena. Usachite mantha, ngakhale minga ndi mkandankhuku zikuzinge ndipo ukukhala pakati pa zinkhanira. Usachite mantha ndi zimene akunena kapena kuopsedwa ndi nkhope zawo, popeza anthuwa ndi awupandu.
7 Le ho taroñe’o am’ iereo o volakoo, ke hijanjiñe he tsy hañaoñe, amy t’ie mpiola.
Ukawawuze ndithu mawu anga, kaya akamva kaya sakamva. Paja anthuwa ndi awupandu.
8 Aa ihe ka, ana’ ondatio, tsendreño ty ho volañeko; ko miola irehe manahake ty fiolà’ i anjomba mpiolay; sokafo ty falie’o, vaho kamao o azotsokoo.
Koma iwe mwana wa munthu, mvetsera zimene ndikukuwuza. Usakhale wowukira ngati iwowo. Tsono yasama pakamwa pako kuti udye chimene ndikukupatsa.”
9 Aa le nenteako te ingo ty fitañe nahitrik’ amako, naho tama’e ao ty boke peleke;
Nditayangʼana ndinangoona dzanja litaloza ine, litagwira mpukutu wolembedwa.
10 navela’e amako, ie sinokitse añ’ate’e naho alafe’e, naho nisokireñ’ ama’e ao ty fandalañe naho ty fihontohañe, vaho ty hankàñe.
Anawufunyulura pamaso panga. Mpukutu wonse unali wolembedwa kuseri nʼkuseri. Ndipo mawu amene analembedwa mʼmenemo anali a madandawulo, maliro ndi matemberero.