< Ezekiela 18 >
1 Niheo amako indraike ty tsara’ Iehovà nanao ty hoe;
Yehova anandiyankhula nati:
2 Ino ty tea’ areo ho saontsieñe, ie manoñoñe o razan-drehake zao ty amy tane’ Israeley, manao ty hoe; Nikama valoboke makira o roae’eo vaho mangitsy ty nife’ o amori’eo?
“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
3 Aa kanao velon-dRaho, hoe t’Iehovà Talè, le tsy hanam-pototse ka nahareo hanoñoñe i razan-drehakey e Israele ao.
“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
4 Oniño te kila ahy ze arofo; fonga ahy ty fiain-drae naho ty fiain’anake; ze ondaty manao hakeo ro hihomake.
Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
5 Fa naho vantañe t’indaty, manao ty hahiti’e naho ty havañonañe,
“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
6 tsy mikama an-kaboañe ey, naho tsy miandra fihaino amo samposampon’ anjomba’ Israeleo naho tsy mandeotse ty valin-drañe’e, vaho tsy mitotoke rakemba miambolañe,
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
7 tsy mamorekeke ondaty, fe mañavak’ amy mpampisongoy ty nampitsaloha’e, tsy mampikametse, fe mamahañe ty kerè ami’ty mahakama’e vaho manaroñe ty mihalo an-tsikiñe;
Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
8 tsy mampisongo hangala’e ana’e naho tsy mandrambe tombo’e, manintake ty fità’e ami’ty hatsivokarañe, le manao zaka to añivo’ t’indaty naho t’indaty,
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
9 vaho mañavelo amo fañèkoo naho mitàna o fepèkoo hanao ty hiti’e. Vañon-dre tsi-mete tsy ho veloñe, hoe t’Iehovà Talè.
Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
10 Aa ie mahatoly anake ho malaso ndra mpampiori-dio
“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
11 (ndra te tsy manao ndra raik’ amy raha rezay ty rae’e); ie mifanjotse an-kaboañe ey, mamahotse ty valin-drañe’e,
Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 mamorekeke ty rarake naho ty poi’e, mikizo, tsy mañavake songo, miandra amy ze samposampo, mbore manao hativàñe,
Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
13 mitake ana’e naho mampisongo naho mangala tombo’e, aa vaho ho velon-dre? Toe tsy ho veloñe; hativàñe iaby i nanoe’e rezay; tsy mahay tsy havetrake, vaho ho ama’e ty lio’e.
Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
14 Aa ie misamak’ anake maharendreke o hene hakeo nanoen-droae’eo, le ndra te oni’e tsy orihe’e,
“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
15 tsy mikama am-bohitsey, tsy miandra amo samposampo’ Israeleo, tsy mandeotse ty valin-drañe’e,
“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 naho tsy mamorekeke ondaty, tsy mitana ty tsinoa’e, tsy mampikametse, te mone fahana’e ty saliko, saroña’e sikiñe ty miboridañe
Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 naho sintone’e ty fità’e tsy hanindry ty rarake, tsy mandrambe ana’e, tsy mampitombo, ie manao ze nandiliako iaby vaho mañavelo amo fañèkoo, le tsy hihomake an-tahin-drae’e, fa toe ho veloñe.
Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
18 Ty rae’e ka, ie namorekeke am-pampisoañañe, naho nitavañe an-drahalahi’e, vaho nanao ty tsy havokarañe am’ ondati’eo; oniño t’ie tsy mete tsy hikenkañe ty amo hakeo’eo.
Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
19 Aa naho manao ty hoe nahareo, Aa vaho akore te tsy vavè’ i ana’ey ty tahin-drae’e? Amy te niaiña’ i anakey o lilio, naho ty havañonañe, naho nivontitire’e iaby o fañèkoo, vaho nanoe’e, le toe ho veloñe.
“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
20 T’indaty manao hakeo ty hihomake. Tsy hivave ty tahin-drae’e ty ana’e, vaho tsy hivave ty hakeon’ ana’e ty rae; fa ty havañona’ i vantañey ro aze, naho ty haratia’ i lo-tserekey ro aze.
Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
21 Aa naho iambohoa’ i raty tserekey o hakeo nanoe’eo naho mifahatse amo hene fañèkoo vaho mañavelo an-kamarentane naho an-kahiti’e, toe ho velon-dre fa tsy hivetrake.
“‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
22 Tsy ho volilieñe ama’e o fiolàñe iaby nanoe’eo; o havañonañe anoe’eo ro hiveloma’e.
Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
23 Paiako hao ty fihomaha’ o lo-tserekeo? hoe t’Iehovà Talè, Tsy hàmake te apo’e o sata’eo, soa te ho veloñe?
Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
24 Fa naho mienga i havantaña’ey ty vantañe naho manao hakeo, vaho fonga anoe’e ty sata tiva’ o tsivokatseo, ho veloñe hao? Toe tsy ho volilieñe ama’e ze hene havantañañe nanoe’e, fa i fiolàñe nandilara’ey naho o tahiñe nanoe’eo ty hivetraha’e.
“‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
25 Aa naho anoa’ areo ty hoe: Tsy mira ty lala’ i Talè. Mijanjiña arè ry anjomba’ Israele: Ty lalako hao ro tsy mira? kera ty anahareo ro mengoke.
“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
26 Naho apo’ ty vantañe ty havantaña’e vaho manao hakeo, le hihomake re; o tahiñe nanoe’eo ty hivetraha’e.
Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
27 Ie ka, naho aforintse’ i tsivokatsey o tsy havokarañe nanoe’eo, vaho mañavelo ami’ty fahiti’e naho ty havantañañe le hirombak’aiñe.
Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
28 Kanao nioni’e naho fonga nado’e o fiolàñe nanoe’eo, le toe ho veloñe; tsy hihomake.
Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
29 Aa ie henaneo, naho hanao ty hoe ty anjomba’ Israele, tsy vantañe ty lala’ i Talè; Ry Anjomba’ Israele, tsy mahity hao o lalakoo? Toe ty lala’ areo ro tsy vantañe.
Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
30 Aa le ho zakaeko nahareo ry anjomba’ Israele, songa ty amo sata’eo, hoe t’Iehovà Talè. Misolohoa vaho iambohò o fiolà’ areoo, tsy mone hampiantoe’ o tahi’ areoo.
“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
31 Ahifiho tsy ho ama’ areo ze fonga fiolàñe niolà’ areo, naho itseneo troke vao, vaho arofo vao; fa ino ty hivetraha’ areo, ry anjomba’ Israele?
Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
32 Toe tsy mahafale ahy ty fihomaha’ i mikoromakey, hoe t’Iehovà Talè; aa le mimpolia soa te ho veloñe.
Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”