< Daniela 9 >
1 Amy taom-baloham-pifehea’ i Dariavese ana’ i Akrasehòse tarira’ o nte-Medaio, ie nanoeñe mpanjaka an-tane’ o nte-Kasdio;
Mʼchaka choyamba cha Dariyo mwana wa Ahasiwero (wochokera kwa Amedi), amene anakhala mfumu ya ku Babuloni,
2 amy taom-baloham-pifehea’ey, le nañotsohotso amo bokeo iraho, Daniele, ty ami’ty ia’ o taoñe tsinara’ Iehovà am’ Iiremeà mpitokio, ty haha-heneke ty fangoakoahañe Ierosalaime, le fito-polo taoñe.
ine Danieli ndinazindikira powerenga mawu a Yehova opatsidwa kwa mneneri Yeremiya, kuti Yerusalemu adzakhala bwinja kwa zaka 70.
3 Aa le natoliko aman’ Añahare Talè ty tareheko, hipaiako an-tsoloho naho halaly, an-dilitse naho gony vaho lavenoke.
Choncho ndinatembenukira kwa Ambuye Mulungu ndipo ndinamudandaulira ndi kupempha posala kudya, ndi kuvala chiguduli ndi kudzola phulusa.
4 Aa le nihalaly am’ Iehovà Andrianañahareko, nisoloho ami’ty hoe: Ie henane zao ry Talè Andrianañahare jabahinake mañeva fañeveñañe, mpitàm-pañìna naho miferenaiñe amo mikoko Azo naho miambeñe o lili’oo;
Ndinapemphera kwa Yehova Mulungu wanga ndi kuvomereza kuti tinachimwa: Ndinati, “Inu Ambuye, Mulungu wamkulu ndi woopsa, amene mumasunga pangano lanu la chikondi kwa onse amene amakukondani ndi kumvera malamulo anu,
5 nandilatse zahay, nanao hakeo naho tahiñe, fa niola vaho nihànkañe amo fandilia’oo naho o fepè’oo.
tachimwa ndipo tachita zolakwa ndi zoyipa. Takuwukirani posiya malangizo ndi malamulo anu.
6 Tsy nihaoñe’ay o mpitoky mpitoro’oo, ie ami’ty tahina’o iereo te nisaontsy amo mpanjaka’aio naho amo mpifehe’aio naho amo roae’aio vaho amo hene’ ondaty i taneio.
Sitinamvere aneneri atumiki anu, amene anayankhula mʼdzina lanu kwa mafumu athu, kwa akalonga athu, makolo athu, ndi kwa anthu onse a mʼdziko.
7 Ry Talè, Azo ty havantañañe, anay ty fisalaran-daharañe, manahake henanekeo; le am’ ondati’ Iehodào naho o mpimone’ Ierosalaimeo vaho am’ Israele iaby, o marineo naho o tsietoitane añeo amo fonga tane nandroaha’o iareo ty amy lilatse nandilara’ iareoo.
“Ambuye ndinu olungama, koma lero tili ndi manyazi, ife anthu a ku Yuda, a ku Yerusalemu ndi Israeli yense, apafupi ndi akutali omwe, ku mayiko onse kumene munatipirikitsira chifukwa cha kusakhulupirika kwathu.
8 Ry Talè toe ama’ay ty fisalaran-daharañe, amo mpanjaka’aio naho amo mpifehe’aio, vaho amo roae’aio, ty amo ota-faly nanoe’ay ama’oo.
Inu Yehova, ife ndi mafumu athu, akalonga athu ndi makolo athu tili ndi manyazi chifukwa takuchimwirani.
9 Amy Talè Andrianañahare’ay ty fiferenaiñañe naho ty fampipohan-kakeo, fa niola zahay,
Ambuye Mulungu wathu ndi wachifundo ndi wokhululuka, ngakhale kuti tamuwukira:
10 naho tsy nihaoñe’ay ty fiarañanaña’ Iehovà Andrianañahare’ay hañaveloa’ay amo Tsara’e najado’e añatrefa’ay am-pitoky mpitoro’eo.
Ife sitinamvere Yehova Mulungu wathu kapena kusunga malamulo ake amene anatipatsa kudzera mwa aneneri atumiki ake.
11 Fonga nandilatse amy fetse’oy t’Israele, niamboho tsy nahajanjiñe ty fiarañanaña’o; izay ty nifetsaha’ i fatsey ama’ay naho i fanta sinokitse amy Tsara’ i Mosè, mpitoron’ Añaharey, ty amo haota-faly nanoe’ay ama’eo.
Aisraeli onse anachimwira lamulo lanu motero anapatuka, nakana kukumverani. “Choncho matemberero ndi olumbira amene alembedwa mʼmalamulo a Mose, mtumiki wa Mulungu, atigwera chifukwa takuchimwirani.
12 Fa nampihenefe’e o tsara nitsarae’e ama’aio, naho amo mpizaka nifelek’ anaio, amo hankàñe nafetsa’e ama’aio; o le lia’ey tsy nanoeñe ambanen-dikerañe iabio le fa nanoeñe am’ Ierosalaime.
Inu mwakwaniritsa mawu amene munayankhula otitsutsa ife ndi otsutsa otilamulira potibweretsera tsoka lalikulu. Pa dziko lapansi sipanachitikenso zinthu ngati zimene zaonekera Yerusalemu.
13 Ie sinokitse amy Tsara’ i Mosèy ao, le nidaiñe ama’ay o hekoheko rezao, fa tsy pinai’ay ty lahara’ Iehovà Andrianañahare’ay hiambohoa’ay o hakeo’aio, haharendreke ty hatò.
Monga kunalembedwa mʼMalamulo a Mose, tsoka lililonse latifikira chikhalirecho sitinapemphe Yehova Mulungu wathu kuti atikomere mtima. Sitinasiye machimo athu, ndipo sitinasamale choonadi chanu.
14 Aa le nampihitrife’ Iehovà i fandilovañey vaho nafetsa’e ama’ay; amy te vantañe amo fitoloñañe anoe’e iabio t’Iehovà Andrianañahare’ay, zahay nañatola amy fiarañanaña’ey.
Choncho Yehova anakonza kuti atigwetsere tsoka limeneli, ndipo wachitadi popeza Yehova Mulungu wathu ndi wolungama mu chilichonse amachita; chikhalirecho ife sitinamumvere.
15 Ie amy zao, ry Talè Andrianañahare’ay, Ihe nañakatse ondati’oo an-tane Mitsraime am-pitañe maozatse naho nahazoa’o tahinañe midodea, manahake henane zao; toe nandilatse zahay vaho nañota faly.
“Inu Ambuye Mulungu wathu, munatulutsa anthu anu ku Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo dzina lanu ndi lotchuka mpaka lero. Ife tachimwa, tachita zolakwa.
16 Ry Talè, ty amo havañona’o iabio, ehe ampitoliho tsy homb’ an-drova’o Ierosalaime, vohi’o miavakey, ty haviñera’o naho ty fiforoforoa’o; amy te sirikae’ ondaty mañohok’ anaio t’Ierosalaime naho ondati’oo ty amo hakeo’aio naho o tahin-droae’aio.
Inu Ambuye, molingana ndi zochita zanu zolungama, tikukupemphani kuti muchotse mkwiyo ndi ukali wanu pa Yerusalemu mzinda wanu, phiri lanu loyera. Machimo athu ndi mphulupulu za makolo athu zachititsa kuti onse otizungulira atonze Yerusalemu ndi anthu anu.
17 Ie amy zao, ry Andrianañahare’ay, janjiño ty halali’ i mpitoro’oy naho o fisolohoa’eo, vaho ampireandreaño ty lahara’o, ty ama’o, ry Talè, ty amy toe’o miavake nampangoakoaheñey.
“Tsopano Mulungu wathu, imvani mapemphero ndi zopempha za mtumiki wanu. Kuti anthu onse akudziweni kuti ndinu Ambuye, komerani mtima malo anu opatulika amene asanduka bwinja.
18 Ry Andrianañahareko, atokilaño ty ravembia’o le mijanjiña; sokafo o fihaino’oo vaho vazohò ty fangoakoaha’ay naho i rova tokaveñe ami’ty tahina’oy; toe tsy ty havañona’ay ty itaroña’ay halaly añatrefa’o, fa o fiferenaiña’o tsi-fotofotoo.
Tcherani khutu, Inu Mulungu, ndipo imvani; tsekulani maso anu ndipo onani mabwinja athu ndi mzinda umene umadziwika ndi dzina lanu. Sitikupempha chifukwa chakuti ndife olungama, koma chifukwa cha kukula kwa chifundo chanu.
19 Mijanjiña, ry Talè; mañahà hakeo, Rañandria; haoño vaho mitoloña ry Talè; ko mihànkañe, ry Andrianañahareko, ty amy tahina’oy, amy te kanjieñe ami’ty tahina’o i rova’oy naho ondati’oo.
Inu Ambuye imvani mawu athu! Ambuye khululukani! Ambuye timvereni, ndipo muchitepo kanthu! Kuti anthu adziwe kuti Inu ndinu Mulungu wanga musachedwe chifukwa mzinda wanu ndi anthu anu amadziwika ndi dzina lanu.”
20 Ie nivolañe naho niloloke vaho nisoloho amo tahikoo naho amo hakeo’ ondatiko Israeleo, vaho nitaron-kalaly añatrefa’ Iehovà Andrianañahareko ty amy vohi-masin’ Añaharekoy;
Ndikuyankhula ndi kupemphera, kuvomereza machimo anga ndi machimo a anthu anga Aisraeli ndi kupempherera phiri lake loyera kwa Yehova Mulungu wanga,
21 aa ie mbe nivolañe am-pilolofañe, va’e amy fisoroñañe harivay, le nihela-pitiliñe amako t’i Gabriele nitendrek’ amako amy aroñaroñe valoha’ey vaho nañedre ahy.
Gabrieli, munthu uja amene ndinamuona mʼmasomphenya poyambirira, anabwera kwa ine mowuluka. Iyi inali nthawi ya nsembe ya madzulo.
22 Nampandrendrehe’e naho nisaontsia’e ty hoe: Ry Daniele, nivotrake etoan-draho hampahafohiñ’ azo i aroñaroñey.
Anandilangiza kuti, “Danieli ndabwera tsopano kuti ndikupatse nzeru kuti uzitha kumvetsa zinthu.
23 Ie vaho nihalaly, le nahitrike i tsaray, le ingo te pok’ etoan-draho hañoke azo; fa vata’e kokoan-drehe; aa le fohino o tsarao naho rendreho o aroñaroñeo.
Utangoyamba kupemphera, Mulungu anayankha. Tsono ine ndabwera kudzakuwuza yankholo, popeza ndiwe wokondedwa kwambiri. Choncho mvetsetsa pamene ndikufotokoza za zinthu zimene unaziona mʼmasomphenya.
24 Fa najadoñe am’ ondati’oo naho amy rova’o miavakey ty hereñandro fitompolo hampijihetse i fiolày, hampigadon-kakeo, hijebañañe o tahiñeo, hampizilike havantañañe tsy ho modo nainai’e, naho hanjitse ty aroñaroñe naho ty fitokiañe, vaho horizañe i Masiñe do’ey.
“Zaka 490 zinayikidwa kuti anthu a mtundu wako ndi mzinda wanu woyera aleke zoyipa, asiye tchimo. Iwo adzapereka dipo kupepesera zolakwa zawo. Zikadzatero anthu adzaonetsa moyo wachilungamo nthawi zonse. Izi zidzatsimikiza zimene unaziona mʼmasomphenya zija ndi zimene ananenera aneneri. Malo opatulika adzakhazikitsidwa.
25 Mahafohina arè naho maharendreha t’ie hifototse ami’ ty fitseizañe i tsara hampipolieñe ondatio hamboatse Ierosalaimey, am-para’ i Mpifehe Tinendrey, le ho hereñandro fito naho hereñandro enempolo-ro’ amby, vaho hamboareñe indraike i damokey naho i kijoliy, an-tsam-poheke.
“Tsono udziwe ndipo uzindikire izi kuti kuyambira pamene lamulo linaperekedwa kuti Yerusalemu akonzedwenso mpaka pamene mfumu Yodzozedwa idzafike padzapita zaka 49. Pa zaka 434 mzinda wa Yerusalemu udzamangidwanso, ndipo mabwalo ndi ngalande zake zidzatetezedwa. Koma nthawiyi idzakhala ya masautso.
26 Aa ie modo i hereñandro enem-polo-ro’amby rey le haitoañe tsy amam-panàñañe i Norizañey; le homb’eo ondati’ i mpifelekeio handrotsake i rovay naho i toetse miavakey; le hoe fisorotombahañe ty ho figadoña’e le fampangoakoahañe ty nalahatse am-para te heneke i aliy.
Patatha zaka 434, Wodzozedwayo adzaphedwa ndipo sadzakhala ndi aliyense. Anthu a wolamulira amene adzabwere adzawononga mzinda ndi Nyumba ya Mulungu. Kutha kwake kudzafika ngati chigumula. Komabe nkhondo idzapitirira mpaka chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu chitachitika.
27 Hanoe’e fañina mijadoñe amy màroy ho ami’ty hereñandro raike; fe añivo’ i hereñandroy re ro hampijihetse i soroñey naho i engay, le añ’elan-draha tiva ty hampangoakoahe’e, ampara’ te nadoañe amy mpampangoakey i famongorañe nafetsey.
Adzachita pangano lolimba ndi anthu ambiri kwa zaka zisanu ndi ziwiri. Koma pakatinʼpakati pa sabata limodzilo iye adzaletsa kupereka nsembe ndi chopereka. Chonyansa chosakaza chija adzachiyika mʼNyumba ya Mulungu, ndipo chidzakhalapobe mpaka wochita zimenezi atalangidwa ndi chiwonongeko chimene Mulungu ananeneratu.”