< 2 Tesaloniana 2 >
1 Aa le mihalaly ama’ areo zahay ry longo, ty amy fiavi’ i Talèntika Iesoà Norizañeiy naho i fitontonan-tika ama’ey,
Pa za kubweranso kwa Ambuye athu Yesu Khristu ndiponso za kusonkhana kwathu kuti tikumane naye, abale, tikukupemphani
2 t’ie tsy hitroetroe am-betsevetse, tsy ho tsiborehetohe’ ty fañahy, ndra ty lañonañe, ndra ty taratasy atao nihirik’ ama’ay manao te nitondroke ty andro’ i Talè.
kuti musagwedezeke msanga mʼmaganizo kapena kuopsezedwa ndi uneneri, mbiri kapena kalata yokhala ngati yachokera kwa ife, yonena kuti tsiku lija la Ambuye linafika kale.
3 Mitaoa tsy ho fañahie’ ndra iaia amy zay, fa tsy ie naho tsy avy hey i fihànkañey vaho abentatse indaty tsy aman-Kakey, i anam-pandrotsahañey,
Musalole kuti wina aliyense akunamizeni mwa njira ina iliyonse. Pakuti tsikulo lisanafike, kudzakhala mpatuko waukulu kwambiri, ndipo kudzaoneka munthu woyipitsitsa uja, munthu woyenera kuwonongedwayo.
4 ie hanjehatse naho hiebotse ambone’ ze atao ‘ndrañahare ndra fitalahoañe, hitoboke añ’ anjomban’ Añahare ao hieva ho Andrianañahare.
Iyeyo adzatsutsa ndi kudziyika pamwamba pa chilichonse chimene anthu amachitcha mulungu kapena amachipembedza. Iyeyo adzadzikhazika mʼNyumba ya Mulungu ndi kudzitcha Mulungu.
5 Tsy tiahi’ areo hao te nitaliliako te mbe tama’ areo?
Kodi simukukumbukira kuti pamene ndinali nanu pamodzi ndinkakuwuzani zimenezi?
6 le fohi’ areo o misebañe aze henaneo, hampiboake aze an-tsa’e.
Ndipo tsopano mukudziwa chimene chikumuletsa kuonekera, koma adzawululika pa nthawi yake yoyenera.
7 Fa mifanehake añetake ao henaneo i fisitahañe amy Hàkey; fe mbe mitoloñe avao i mpanebañey ampara’ t’ie nasintake añe.
Pakuti mphamvu yobisika yoyipitsitsa ikugwira ntchito ngakhale tsopano; koma amene akutchinga mphamvuyo adzapitiriza kutero mpaka pamene wotchingayo adzachotsedwe.
8 Haboak’ amy zay i tsi-an-Kakey naho ho rebahe’ i Talè ami’ty fikofoham-palie’e vaho harotsa’e ami’ty fireandrea’ i fitotsaha’ey.
Ndipo kenaka woyipitsitsayo adzaonekera, amene Ambuye Yesu adzamugonjetsa ndi mpweya otuluka mʼkamwa mwake ndi kumuwononga ndi ulemerero wa kubwera kwake.
9 Eka, ie pok’ eo i tsy mañambeñe Hàkey, le hatolo’ i mpañìnjey aze ty haozarañe hitoloñe raha tsi-tantane maro reke-biloñe naho sahàtse,
Woyipitsitsayo adzabwera ndi mphamvu za Satana. Adzaonetsa mphamvu zake pochita zizindikiro ndi zodabwitsa zachinyengo.
10 naho ze hene famañahia’ ty hatsivokarañe amo hirotsakeo, ie tsy nandrambe ty fikokoañe ty hatò hahazoa’ iareo rombake.
Iye adzagwiritsa ntchito mtundu uliwonse wachinyengo kupusitsa amene akuwonongeka. Iwo akuwonongeka chifukwa akukana kukonda choonadi ndi kuti apulumutsidwe.
11 Izay ty amañahian’ Añahare iereo, hiantoke ty vande,
Chifukwa cha chimenechi, Mulungu akuwatumizira chinyengo chachikulu kuti akhulupirire bodza.
12 le fonga ho zakaeñe o tsy miantoke ty hato te mone mifale an-katsivokarañeo.
Choncho adzalangidwa onse amene sanakhulupirire choonadi, koma anakondwera mu zoyipa.
13 F’ie tsy mete tsy mañandriañe an’ Andrianañahare ty ama’ areo nainai’e, ry longo isohe’ i Talè, amy t’ie nijoboñen’ Añahare tam-pifotora’e añe ho rombaheñe ami’ty fampiavaha’ i Arofoy vaho ty fatokisañe ty hatò.
Koma tiyenera kuyamika Mulungu chifukwa cha inu abale okondedwa mwa Ambuye, pakuti Mulungu anakusankhani pachiyambi pomwe kuti mupulumuke chifukwa cha ntchito yoyeretsa ya Mzimu ndi chikhulupiriro chanu mʼchoonadi.
14 Izay ty nikanjia’e anahareo amy talili-soa’ay, handrambe ty enge’ i Talèn-tika Iesoà Norizañey.
Iye anakuyitanirani zimenezi kudzera mwa uthenga wathu wabwino, kuti mulandire nawo ulemerero wa Ambuye athu Yesu Khristu.
15 Aa le mijohaña ry longo, mifahara amo fañòhañe nañoha’aio, ke an-tsara he an-taratasy.
Kotero tsono, abale, imani mwamphamvu ndi kugwiritsa ziphunzitso zimene tinakupatsani kudzera mʼmawu apakamwa kapena kudzera mʼkalata.
16 Le i Talèntika Iesoà Norizañey naho i Andrianañahare Raen-tika mpikoko antika naho nanolotse antika fañohoañe tsy modo naho fitamàn-tsoa amy fañisoha’ey abey (aiōnios )
Ambuye athu Yesu Khristu mwini ndi Mulungu Atate wathu, amene anatikonda ife ndipo mwachisomo chake anatipatsa kulimba mtima kwamuyaya ndi chiyembekezo chabwino, (aiōnios )
17 ro hañosike ty arofo’ areo vaho hampijadoñe anahareo amy ze hene tsara naho fitoloñan-tsoa.
akulimbikitseni ndi kukupatsani mphamvu yogwirira ntchito ndi kuyankhula zabwino zilizonse.