< 2 Samoela 8 >

1 Ie añe, linafa’ i Davide o nte-Pilistio le navoho’e ambane vaho tinava’ i Davide am-pità’ o nte Pilistio ty renen-drova’ iareo.
Patapita nthawi, Davide anagonjetsa Afilisti ndi kuwapambana ndipo analanda Metegi Ama kuchoka mʼmanja mwa Afilistiwo.
2 Linafa’e ka o nte-Moabeo le zinehe’e an-taly, ie nampibaboheñe an-tane eo; nanjehe taly roe ho zamañe, le nitana’e ho veloñe ty taly raike. Aa le nitoroñe i Davide o nte-Moabeo, nañenga ama’e.
Davide anagonjetsanso Amowabu. Iye anawalamula kuti agone pansi mʼmizere itatu pa gulu lililonse ndipo anawayeza ndi chingwe. Pa gulu lililonse ankapha anthu amene anali pa mizere iwiri yoyamba, kusiyapo mzere wachitatu. Kotero Amowabu anakhala pansi pa ulamuliro wa Davide ndipo ankapereka msonkho.
3 Linafa’ i Davide ka t’i Kadadetsere ana’ i Rekobe, mpanjaka’ i Tsobà, amy nionjona’e mb’ an-tsaka Eofrata mb’eo hampijadoñe ty fifehea’e.
Komanso Davide anagonjetsa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba, pamene anapita kukakhazikitsa ulamuliro wake mʼmbali mwa mtsinje wa Yufurate.
4 Tinava’ i Davide ama’e ty mpi­ningi-tsoavala arivo-tsi-fiton-jato, naho lahindefoñe ro’ ale; le nanoe’ i Davide fira-sintake iaby o soavalan-tsareteo naho tsy ty zato nahaja’e ho an-tsarete zato.
Davide analanda magaleta 1,000, anthu 7,000 okwera magaleta pamodzi ndi asilikali oyenda pansi 20,000. Iye anadula mitsempha ya akavalo onse okoka magaleta, koma anasiyapo akavalo 100 okha.
5 Aa ie pok’eo o nte-Arame boake Damasek’ añeo hañolotse i Kadade­tsere mpanjaka’ i Tsobà, le zinevo’ i Davide ty ro-ale-tsi-ro-arivo lahindefo’ o nte-Arameo.
Aramu wa ku Damasiko atabwera kudzathandiza Hadadezeri mfumu ya Zoba, Davide anakantha asilikali 22,000.
6 Nampipoha’ i Davide e Ara­me’ i Damasek’ ao ty mpirai-lian-dahindefoñe naho nanoeñe mpitoro’ i Davide o nte-Arameo, vaho nañenga ama’e. Tinolo’ Iehovà fandreketañe amy ze nomba’e iaby t’i Davide.
Iye anakhazikitsa maboma mu ufumu wa Aramu wa ku Damasiko, ndipo Aaramu anakhala pansi pa ulamuliro wake ndipo ankapereka msonkho. Yehova ankamupatsa chipambano Davide kulikonse kumene ankapita.
7 Rinambe’ i Davide ze fikalan-defo volamena amo mpitoro’ i Kadadetsereo vaho nasese’e e Ierosalaime añe.
Davide anatenga zishango zagolide za akuluakulu ankhondo a Hadadezeri ndi kubwera nazo ku Yerusalemu.
8 Le nangalà’ i Davide torisike tsifotofoto ty Betà naho i Berotae, rova’ i Kadadetsere.
Mfumu Davide inatenga mkuwa wambiri kuchokera ku Beta ndi Berotai, mizinda ya Hadadezeri.
9 Aa ie jinanji’ i Toy, mpanjaka’ i Kamate te fonga zinevo’ i Davide ty valobohò’ i Kadadetsere,
Tou, mfumu ya Hamati atamva kuti Davide wagonjetsa gulu lonse lankhondo la Hadadezeri,
10 le nampihitrife’ i Toy amy Davide mpanjaka ty ana’e Iorame, hañontane aze naho hitata aze ty amy nialia’e i Kadadetsere naho nahagioke; fa nimpialy amy Toy t’i Kadadetsere, le nandesa’ Iorame fanake volafoty naho fanake volamena vaho fanake torisike.
anatumiza mwana wake Yoramu kwa mfumu Davide kukamulonjera ndi kukamuyamikira chifukwa cha kupambana kwake pa nkhondo yake ndi Hadadezeriyo, amene analinso pa nkhondo ndi Tou. Yoramu anabweretsa ziwiya zasiliva, zagolide ndi zamkuwa.
11 Nengae’ i Davide mpanjaka am’ Iehovà izay, mindre amo volafoty naho volamena navi’e boak’ amo hene fifeheañe nam­pi­ambanea’eoo:
Mfumu Davide inapereka zinthu zimenezi kwa Yehova, monga anachitira ndi siliva ndi golide zochokera ku mayiko onse amene anawagonjetsa:
12 boak’ Arame naho i Moabe naho amo ana’ i Amoneo naho amo nte-Pilistio naho amy Amaleke vaho amo nikopaheñe amy Kadadetse­re, ana’ i Rekobe, mpanjaka’ i Tsobàio.
Edomu ndi Mowabu, Aamoni ndi Afilisti, ndi Aamaleki. Iye anaperekanso zolanda ku nkhondo zochokera kwa Hadadezeri mwana wa Rehobu, mfumu ya Zoba.
13 Nahazo asiñe t’i Davide te nimpoly amy nandafañe o nte-Ara­meo am-bavatanen-tsira ao, ondaty rai-ale-tsi-valo-arivo.
Ndipo Davide anatchuka atabwera kokakantha Aedomu 18,000 mu Chigwa cha Mchere.
14 Nampipoha’e mpirai’ lia t’i Edome, toe nitsitsihe’e mpirai-lia ty Edome vaho hene natao mpitoro’ i Davide o nte-Edomeo. Natolo’ Iehovà amy Davide ty fandre­ketañe ndra aia’aia ty nomba’e.
Iye anayika maboma mʼdera lonse la Edomu, ndipo Aedomu onse anakhala pansi pa Davide. Yehova ankapambanitsa Davide kulikonse kumene ankapita.
15 Nifelehe’ i Davide t’Israele iaby naho nizaka ze hene ondati’e an-kavantañañe naho an-kavañonañe.
Davide analamulira dziko lonse la Israeli ndipo ankachita zonse mwachilungamo ndi molondola pamaso pa anthu ake onse.
16 Ioabe ana’ i Tseroia ty nifehe i valobohòkey; naho mpamolily t’Iehosafate, ana’i Akilode;
Yowabu mwana wa Zeruya anali mkulu wa ankhondo; Yehosafati mwana wa Ahiludi anali mlembi wa zochitika.
17 mpisoroñe t’i Tsadoke ana’ i Akitobe naho i Akimelek’ ana’ i Abiatare; naho mpitan-tsokitse t’i Sereià;
Zadoki mwana wa Ahitubi ndi Ahimeleki mwana wa Abiatara anali ansembe; Seraya anali mlembi;
18 naho mpifehe’ o nte-Keretìo naho o nte-Peletìo t’i Benaià, ana’ Iehodaià; vaho talèm-pifehe o ana’ i Davideo.
Benaya mwana wa Yehoyada anali mtsogoleri wa Akereti ndi Apeleti; ndipo ana a Davide anali ansembe.

< 2 Samoela 8 >