< 2 Mpanjaka 1 >
1 Ie nihomake t’i Akabe, le niola am’ Israele t’i Moabe.
Atamwalira Ahabu, Mowabu anawukira Israeli.
2 Nitsirikoake boak’ amy tsingarakara’ i efe’e ambone eo e Someroney t’i Ahkazià le nisiloke vaho nampañitrife’e ty ìrake, ami’ty hoe: Akia. añontaneo amy Baalezebobe, ‘ndrahare’ i Ekrone, ke hiambeñe iraho amo areteko zao.
Ndipo Ahaziya anagwa kuchokera pa khonde la chipinda chake chammwamba ku Samariya, ndipo anavulala kwambiri. Choncho iye anatuma amithenga nawawuza kuti, “Pitani mukafunse kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, ngati ndichire matendawa.”
3 Fe hoe ty tsara’ i anjeli’ Iehovà amy Elià nte-Tisbý: Miongaha, akia mifanalakà amo ìra’ i mpanjaka’ i Someroneio, le ano ty hoe: Aa vaho tsy aman’ Añahare hao t’Israele, t’ie homb’ amy Baalezebobe ‘ndrahare’ i Ekrone hañontane aze?
Koma mngelo wa Yehova anawuza Eliya wa ku Tisibe kuti, “Nyamuka, pita ukakumane ndi amithenga a mfumu ya ku Samariya ndipo ukawafunse kuti, ‘Kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake inu mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni?’
4 Aa le hoe ty nafè’ Iehovà: Tsy hizotso amy fandreañe nijoña’oy irehe, fa toe hivetrake. Le nienga t’i Elià.
Tsono Yehova akuti, ‘Iweyo sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’” Ndipo Eliya ananyamuka.
5 Nimpoly ama’e o ìra’eo, le hoe re ama’e: Ino ty nimpolia’ areo?
Amithenga aja atabwerera kwa mfumu, mfumuyo inawafunsa kuti, “Chifukwa chiyani mwabwerera?”
6 Le nanoa’ iareo ty hoe: Nifanampe ama’ay t’indaty nanao ty hoe: Akia mimpolia mb’ amy mpanjaka nañirak’ anahareoy, vaho isaontsio ty hoe: Hoe ty nafè’ Iehovà: Aa vaho tsy aman’ Añahare hao t’Israele te ihe mañitrike hañontane e Baalezebobe ‘ndrahare’ i Ekrone? Aa le tsy hizotsoa’o i fandreañe nijoña’o, fa toe hihomake.
Iwo anayankha kuti, “Munthu wina anabwera kudzakumana nafe, ndipo anatiwuza kuti, bwererani kwa mfumu imene inakutumani ndipo mukayiwuze kuti, ‘Yehova akuti, kodi popeza kulibe Mulungu ku Israeli, nʼchifukwa chake mukupita kukafunsa nzeru kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni? Tsono sudzadzuka pa bedi wagonapo. Udzafa ndithu!’”
7 Le hoe re am’ iereo: T’indaty manao akore ty nifanalaka ama’ areo, nisaontsy i entañe zay ama’ areo?
Mfumu inafunsa amithengawo kuti, “Kodi munthu amene anabwera kudzakumana nanuyo ndi kukuwuzani zimenezi amaoneka bwanji?”
8 Le hoe ty natoi’ iareo: Ondaty volovoloeñe, midian-kolitse an-toha’e. Le hoe re: I Elià nte-Tisbý izay.
Iwo anayankha kuti, “Munthuyo anavala zovala zaubweya ndi lamba wachikopa mʼchiwuno mwake.” Mfumu inati, “Munthu ameneyo ndi Eliya wa ku Tisibe.”
9 Aa le nañirake ty mpifehe-limampolo rekets’ i limampolo’ey i mpanjakay. Niañambone mb’ama’e mb’eo iereo, le ingo ie niambesatse an-dengom-bohitse ey. Le hoe re ama’e: O ondatin’ Añahareo, hoe ty enta’ i mpanjakay: Mizotsoa.
Pamenepo mfumu inatuma mtsogoleri wa ankhondo ndi anthu ake makumi asanu kwa Eliya. Mtsogoleriyo anapita kwa Eliya, amene anali atakhala pamwamba pa phiri, ndipo anati, “Munthu wa Mulungu, mfumu ikuti, ‘Tsikani!’”
10 Le hoe ty natoi’ i Elià i mpifehe limampoloy: Naho toe ondatin’ Añahare iraho le ee te hizotso boak’ andikerañe ey ty afo hamorototo azo naho o limampolo’oo, Aa le nikodoiñe boak’ andikerañe añe ty afo namorototo aze rekets’ i limampolo rey.
Eliya anayankha mtsogoleriyo kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu makumi asanu akowo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
11 Nañirake mpifehe limampolo indraike re rekets’ i limampolo’ey. Le nisaontsia’e ty hoe: Ry ‘ndatin’ Añahareo, hoe i mpanjakay: Mizotsoa ami’ty manao zao.
Zitachitika izi, mfumu inatumanso mtsogoleri wina pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleriyo anati kwa Eliya, “Munthu wa Mulungu, zimene mfumu ikunena ndi izi, ‘Tsikani msangamsanga!’”
12 Le hoe ty natoi’ i Elià: Naho toe ‘ndatin’ Añahare iraho, le ee te hizotso boak’ an-dikerañe ey ty afo hamorototo azo naho o limampolo’oo. Le nizotso boak’ aman’ Añahare an-dikerañe añe ty afo namorototo aze rekets’ i limampolo’ey.
Eliya anayankha kuti, “Ngati ndine munthu wa Mulungu, moto utsike kuchokera kumwamba, ukupsereze iwe pamodzi ndi anthu ako makumi asanuwo!” Pomwepo moto unatsikadi kuchokera kumwamba ndipo unapsereza mtsogoleriyo pamodzi ndi anthu akewo.
13 Nañirake indraike re, le ty mpifehe limampolo fahatelo reketse ty limam-polo’e. Nitroatse mb’eo i mpifehe limampoloy, le nitongalek’ añatrefa’ i Elià eo vaho nihalalia’e ami’ty hoe: Ry ondatin’ Añahare, miambane ama’o, ehe te ho vara am-pahaisaha’o ty fiaiko naho ty fiai’ o mpitoro’o limampolo retoañe.
Ndipo mfumu inatumanso mtsogoleri wachitatu pamodzi ndi asilikali ake makumi asanu. Mtsogoleri wachitatuyu anakwera pa phiripo ndi kugwada pamaso pa Eliya. Iye anayankhula mopemba kuti, “Munthu wa Mulungu, chonde musandiwononge ineyo pamodzi ndi atumiki makumi asanu anuwa!
14 Toe nihotrake boak’ andikerañe ey ty afo namorototo i mpifehe limampolo taolo rey rekets’ i limampolo’ iareoy; fe ee te ho sarotse ampahaoniña’o henaneo ty fiaiko.
Taonani, moto unatsika kuchokera kumwamba ndi kupsereza atsogoleri awiri pamodzi ndi anthu awo onse. Koma tsopano musawononge moyo wanga!”
15 Le hoe ty tsara’ i anjeli’ Iehovày amy Elià: Mindreza fizotso ama’e, ko hembañe. Le niongake re nizotso mindre ama’e mb’ amy mpanjakay mb’eo.
Mngelo wa Yehova anati kwa Eliya, “Pita naye, usamuope.” Choncho Eliya ananyamuka natsika naye limodzi kupita kwa mfumu.
16 Le hoe re tama’e: Hoe ty nafè’ Iehovà: Ie nañitrik’ ìrake hañontane i Baalezebobe, ‘ndrahare’ i Ekrone; tsy aman’Añahare hao t’Israele hañontanea’o i tsara’ey? Toly ndra tsy hizotsoa’o o fandreañe nijoña’oo fa toe hivetrake.
Eliya anawuza mfumu kuti, “Yehova akuti, ‘Chifukwa chiyani munatumiza amithenga kwa Baala-zebubu, mulungu wa ku Ekroni, kukafunsa ngati muti muchire? Kodi mu Israeli mulibe Mulungu woti nʼkukuyankhani funso lanu? Choncho, popeza mwachita izi, simudzadzuka pamene mwagonapo; mudzafa ndithu.’”
17 Aa le nihomake re ty amy tsara’ Iehovà nisaontsie’ i Eliày. Le niorotse nandimbe aze nifehe t’Iehorame amy taom-paharoe’ Iehorame ana’ Iehosafate mpanjaka’ Iehoday; amy t’ie tsy nanañ’ ana-dahy.
Motero Ahaziya anafadi, monga mwa mawu a Yehova amene Eliya anayankhula. Tsono popeza Ahaziya analibe mwana, Yoramu analowa ufumu mʼmalo mwake mʼchaka chachiwiri cha Yehoramu mwana wa Yehosafati mfumu ya ku Yuda.
18 Le o fitoloñañe ila’e nanoe’ i Ahkaziào, tsy fa sinokitse amy bokem-pamoliliañe o mpanjaka’ Israeleoy hao?
Ntchito zina zonse zimene Ahaziya anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a ku Israeli?