< 2 Tantara 23 >
1 Aa ie amy taom-pahafitoy, le nihafatratse t’Iehoiada, le rinambe’e o mpifehe-zatoo naho i Azarià ana’ Ierohame naho Ismaele ana’ Iehonane naho i Azarià ana’ i Ovede naho i Maaseià ana’ i Adaià naho i Elisafate ana’ i Zikrý vaho nifañina am’ iereo.
Mʼchaka chachisanu ndi chiwiri Yehoyada anaonetsa mphamvu zake. Iye anachita pangano ndi olamulira magulu a anthu 100: Azariya mwana wa Yerohamu, Ismaeli mwana wa Yehohanani, Azariya mwana wa Obedi, Maaseya mwana wa Adaya ndi Elisafati mwana wa Zikiri.
2 Le nanitsike Iehodà iereo nanontoñe o nte-Levio amo hene’ rova’ Iehodao naho o talèn’ anjomban-droae’ Israeleo vaho niheo mb’e Ierosalaime mb’eo.
Iwo anayendayenda mʼdziko la Yuda ndipo anasonkhanitsa Alevi ndi atsogoleri a mabanja a Aisraeli ochokera mʼmizinda yonse. Atabwera ku Yerusalemu,
3 Nifañina amy mpanjakay añ’anjomban’ Añahare ao i fivori-bey iabiy, le hoe t’Iehoiada am’ iereo: Heheke te hifehe ty ana’ i mpanjakay amy tsara’ Iehovà ty amo ana’ i Davideoy.
msonkhano wonse unachita pangano ndi mfumu mu Nyumba ya Mulungu. Yehoyada anawawuza kuti, “Mwana wa mfumu adzalamulira monga ananenera Yehova zokhudza ana a Davide.
4 Zao ty hanoe’ areo: ty faha-telo’ areo mpisoroñe naho nte-Levy mpizilik’ ao amy Sabatay ro hañambeñe o lalambeio;
Tsopano zimene muti muchite ndi izi: Limodzi mwa magawo atatu a ansembe ndi Alevi amene mudzakhale pa ntchito pa Sabata muzikalondera pa khomo,
5 ty faha-telo’e ty ho añ’ anjomba’ i mpanjakay; ty faha-telo’e ty ho an-dalambei’ i manantañey; vaho ho an-kiririsan’ anjomba’ Iehovà eo ondaty iabio.
ndi limodzi la magawo atatu likakhale ku nyumba yaufumu ndipo limodzi la magawo atatu likakhale ku chipata cha Maziko ndipo anthu ena onse akakhale mʼmabwalo a Nyumba ya Yehova.
6 Ko ado’ areo himoak’ añ’ anjomba’ Iehovà ao ndra ia’ia naho tsy o mpisoroñeo naho o nte-Levy mpitoroñeo avao; ie ro hizilik’ ao, amy te miavake; vaho fonga hambena’ ondatio o fanoroa’ Iehovào.
Musalole aliyense kulowa mʼNyumba ya Yehova kupatula ansembe ndi Alevi amene akutumikira. Iwo atha kutero chifukwa apatulidwa koma anthu ena onse ayenera kumvera zimene Yehova walamula.
7 Hañarikatoke i mpanjakay o nte-Levio, songa hitañe ty fialia’e am-pità’e; le ho vonoeñe ze ila’e mimoak’ amy anjombay; vaho inahareo, mindreza amy mpanjakay ndra t’ie mizilike ndra te miakatse.
Alevi akhale mozungulira mfumu, munthu aliyense ali ndi chida chake mʼmanja. Aliyense amene alowe mʼNyumba ya Mulungu ayenera kuphedwa. Mukhale nayo pafupi mfumu kulikonse kumene izipita.”
8 Aa le nanoe’ o nte-Levio naho Iehoda iaby ze linili’ Iehoiada, mpisoroñe, le songa rinambe’e ondati’eo, o hizilik’ amy Sabotseio naho o hiakatse amy Sabotseio; amy te tsy navotso’ Iehoiada o mpirimboñeo.
Alevi ndi anthu onse a ku Yuda anachita monga momwe wansembe Yehoyada anawalamulira. Aliyense anatenga anthu ake amene ankagwira ntchito pa Sabata ndi amene amapita kukapuma, pakuti wansembe Yehoyada sanalole gulu lililonse kuti lipite.
9 Mbore zinara’ Iehoiada, mpisoroñe amo mpifehe-zatoo o lefoñe naho fikalañ’ araña naho fikalan-defo’ i Davide mpanjaka, boak’ añ’ anjomban’ Añahareo.
Ndipo Yehoyada anapereka kwa atsogoleri a magulu a anthu 100 mikondo ndi zishango zazikulu ndi zazingʼono zimene zinali za Davide ndipo zinali mʼNyumba ya Mulungu.
10 Le nalaha’e ondaty iabio, songa reke-pialiañe am-pità’e, boak’ ankavana’ i anjombay pak’ ankavia’ i anjombay, am-piozañe amy kitreliy naho amy anjombay, añarisehoañe i mpanjakay.
Iye anayika anthu onse, aliyense ali ndi chida mʼdzanja lake mozungulira mfumu pafupi ndi guwa ndi Nyumba ya Mulungu, kuyambira mbali ya kummwera mpaka kumpoto kwa Nyumba ya Mulungu.
11 Nampiavote’ iereo amy zao i ana-mpanjakay naho naombe ama’e i sabakay naho natolotse aze i fañinay vaho nanoeñe mpanjaka, noriza’ Iehoiada naho o ana’eo vaho nanao ty hoe: Mahavelo ry mpanjaka.
Yehoyada ndi ana ake anatulutsa mwana wa mfumu ndipo anamumveka chipewa chaufumu ndipo anamupatsa Buku la Chipangano namulonga ufumu. Yehoyada ndi ana ake anamudzoza ndipo anafuwula kuti, “Ikhale ndi moyo wautali mfumu!”
12 Ie tsinano’ i Atalià ty fikoraha’ ondaty nilay handrenge i mpanjakaio le nimoak’ añ’ anjomba’ Iehovà ao mb’am’ ondatio mb’eo.
Ataliya atamva phokoso la anthu akuthamanga ndi kukondwerera mfumu, anapita ku Nyumba ya Yehova komwe kunali anthuko.
13 Niisa’e te inge nijohañe marine i faha’ey am-pimoahañe eo i mpanjakay naho nitotok’ amy mpanjakay o roandriañeo naho o mpitan-trompetrao naho nirebeke iaby ondati’ i taneio naho nampipopò trompetra naho nitintim-pititihañe o mpisaboo, nisabo vaho nitarike am-pandrengeañe. Aa le niriate’ i Atalià o saro’eo nanao ty hoe: Fiola! Fiola!
Iye anayangʼana, ndipo anaona mfumu itayima pa chipilala chake chapakhomo. Atsogoleri ndi oyimba malipenga anali pafupi ndi mfumuyo, ndipo anthu onse a mʼderali amakondwerera ndi kuyimba malipenga ndiponso oyimba ndi zida amatsogolera matamando. Pamenepo Ataliya anangʼamba mkanjo wake ndipo anafuwula kuti, “Kuwukira! Kuwukira!”
14 Nampiakare’ Iehoiada amo mpifehe-zato nifeleke i valobohòkeio re, le nanoa’e ty hoe: Akaro añivo’ o firimboñañe añ’anjombao re, le zevò am-pibara ze mañorik’ aze; ami’ty nandilia’ i mpisoroñey ty hoe: Ko vonoeñe añ’ anjomba’ Iehovà ao.
Wansembe Yehoyada anatumiza olamulira magulu a anthu 100 aja, amene amayangʼanira asilikali ndipo anawawuza kuti, “Mutulutseni ameneyu pakati pa mizere yanu ndipo muphe aliyense amene adzamutsata.” Pakuti ansembe anati, “Musamuphere mʼNyumba ya Mulungu wa Yehova,”
15 Aa le tsinepa’ iareo am-pitàñe; le ie pok’ amy fimoahan-tsoavalan’ anjombam-panjakay le zinevo’ iereo.
choncho anamugwira pamene amafika pa chipata cha Kavalo pa bwalo la nyumba yaufumu, ndipo anamuphera pamenepo.
16 Le nifañina añivo’e naho ondaty iabio vaho i mpanjakay t’Iehoida, t’ie ho ondati’ Iehovà.
Tsono Yehoyada anachita pangano, iye mwini ndi anthu onse ndiponso mfumu kuti adzakhala anthu a Yehova.
17 Aa le nomb’an-traño’ i Baale mb’eo ondaty iabio nandrotsak’ aze, nandemok’ o kitreli’eo naho o sare’eo, vaho vinono’ iareo t’i Matane mpisoro’ i Baale aolo’ o kitrelio.
Anthu onse anapita ku kachisi wa Baala ndipo anamugwetsa. Iwo anaphwanya maguwa ndi mafano ndi kupha Matani wansembe wa Baala patsogolo pa maguwawo.
18 Le tinendre’ Iehoiada o mpifehe’ i anjomba’ Iehovào ho ambanem-pità’ o mpisoroñe nte-Levy zinara’ i Davide am-pirimboñañe mifandimbe añ’anjomba’ Iehovà ao hañenga soroñe am’ Iehovào, ty amy nanokirañe amy Tsara’ i Mosèy, am-pirebehañe naho takasy nampanoe’ i Davide.
Kenaka Yehoyada anayika ansembe, omwe anali Alevi kukhala oyangʼanira Nyumba ya Yehova, amene Davide anawapatsa ntchito yoti azipereka nsembe zopsereza kwa Yehova mʼNyumba ya Mulungu, monga zinalembedwa mʼmalamulo a Mose kuti azitero akukondwera ndi kuyimba monga Davide analamulira.
19 Tinendre’e ka o mpiamben-dala’ i anjomba’ Iehovàio, soa tsy aman-dalañe hiziliha’e t’indaty tsy malio.
Ndipo anayika alonda a pa khomo pa zipata za Nyumba ya Yehova kuti aliyense amene ndi odetsedwa asalowe.
20 Le nendese’e o mpifele-jatoo naho o roandriañeo naho o mpifelek’ ondatio naho ze hene ondati’ i taney vaho nampizotsoe’e boak’ añ’ anjomba’ Iehovà ao i mpanjakay; le nizilik’ amy lalambey amboney mb’ añ’ anjomba’ i mpanjakay mb’eo re vaho nampiambesareñe am-piambesam-pifeheañe eo i mpanjakay.
Iye anatenga olamulira magulu a anthu 100, anthu otchuka, olamulira anthu ndi anthu onse a mʼderalo ndipo anabweretsa mfumu kuchokera ku Nyumba ya Mulungu. Iwo anapita ku nyumba yaufumu kudzera ku Chipata Chakumitu ndipo anayikira mfumu mpando wolemekezeka,
21 Le nandia taroba iaby ondati’ i taneio vaho nitofa i rovay amy te vinono am-pibara t’i Atalià.
ndipo anthu onse a mʼderali anakondwera. Tsono mu mzinda munali bata chifukwa Ataliya anaphedwa ndi lupanga.