< 2 Tantara 18 >

1 Nanañ’asy naho vara tsi-efa t’Iehosafate; f’ie nifampilongo amy Aka­be am-panambaliañe.
Tsono Yehosafati anali ndi chuma chambiri ndi ulemu, ndipo iye anachita mgwirizano wa ukwati ndi Ahabu.
2 Ie taoñe maromaro añe, le nizotso mb’amy Akabe e So­merone mb’eo. Nandenta añondry naho añombe ho aze naho ho amo mpiama’eo t’i Akabe vaho sinigì’e hindre-lia ama’e mb’e Ramote-gilade mb’eo.
Patapita zaka zina, iye anapita kukacheza kwa Ahabu mu Samariya. Ahabu anaphera iye pamodzi ndi anthu amene anali naye, nkhosa zambiri ndi ngʼombe ndipo anamuwumiriza kuti akathire nawo nkhondo Ramoti Giliyadi
3 Fa hoe t’i Aka­be mpanjaka’ Isra­ele am’ Iehosafate mpanjaka’ Iehoda: Hindre-lia amako hao irehe mb’e Ramote-Gilade mb’eo? Le hoe ty natoi’e: Manahak’ azo iraho, naho ondatikoo hoe ondati’oo, vaho ho mpiama’o añ’aly zahay.
Ahabu mfumu ya Israeli anafunsa Yehosafati mfumu ya Yuda kuti, “Kodi mudzapita nane kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha kuti, “Ine ndili ngati inu nomwe, ndi anthu anga ngati anthu anu. Ife tikhala nanu limodzi pa nkhondoyi.”
4 Fe hoe t’Iehosafate amy mpanjaka’ Israeley: Ehe, añontaneo heike ty tsara’ Iehovà.
Koma Yehosafati anatinso kwa mfumu ya Israeli, “Choyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
5 Natonto’ i Akabe amy zao o mpitokio, ondaty efa-jato, le nanoa’e ty hoe; Hionjomb’e Ramote-gilade hihotakotake hao tika, he hifonen-draho? Le hoe iereo: Mionjona, amy t’ie hatolon’ Añahare am-pità’ i mpanjakay.
Tsono mfumu ya Israeli inasonkhanitsa aneneri 400 ndipo inawafunsa kuti, “Kodi tipite kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Mulungu adzawupereka mʼdzanja la mfumu.”
6 Fe hoe t’Iehosafate: Tsy amam-pitoki’ Iehovà hao ty atoy, hañontanean-tika?
Koma Yehosafati anafunsanso kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wina wa Yehova amene ife tingafunsireko?”
7 Le hoe ty mpanjaka’ Israele am’ Iehosafate: Mbe eo t’indaty mete hampañontanean-tika am’ Iehovà, f’ie hejeko; fa le lia’e tsy itokia’e ty hasoa, toe nainai’e raty; i Mikaià ana’ Imlà ‘nio. Le hoe t’Iehosafate; Ehe tsy hanao izay ty mpanjaka.
Mfumu ya Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife kudzera mwa iye titha kufunsira kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa sandilosera zabwino koma zoyipa nthawi zonse. Iyeyu ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu isanene motero.”
8 Aa le tinoka’ i mpanjaka’ Israeley ty mpifehe ami’ty hoe: Hitrifo masika t’i Mikaià ana’ Imlà.
Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa akuluakulu ake ndipo inati, “Kamutengeni Mikaya mwana wa Imula, abwere msanga.”
9 Songa ni­ambesatse amy fiambesa’ey ty mpanjaka’ Israele naho Iehosafate, nisikiñe saro-mireparepa, le niambesatse an-toem-pifofohañe an-dalambei’ i Somerone eo vaho sindre nitoky añatrefa’ iereo eo o mpitokio.
Mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda, atavala mikanjo yawo yaufumu anali atakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopunthira tirigu pa khomo la chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
10 Le niranjie’ i Tsidkià ana’ i Kenaanà ty tsifam-biñe vaho nanao ty hoe: Hoe t’Iehovà: Iretoañe ty hitrofaha’o o nte-Arameo ampara t’ie mongotse.
Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana anapanga nyanga zachitsulo ndipo analengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi udzagunda Aaramu mpaka atawonongedwa!’”
11 Le sambe nitoky o mpitokio nanao ty hoe: Mionjona mb’e Ramote-Gilade, le mihenefa; fa hatolo’ Iehovà am-pità’ i mpanjakay.
Aneneri ena onse amanenera chimodzimodzi kuti, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo kapambaneni, pakuti Mulungu adzamupereka mʼdzanja la mfumu.”
12 Nanao ty hoe amy Mikaià i mpihitrike nitok’ azey: Inao! songa mitoky hasoa amy mpanjakay o mpitokio, aa ehe te hindray ami’ty raik’ am’iereo ty saontsi’o vaho mitaroña hasoa.
Wauthenga amene anapita kukayitana Mikaya anati kwa iye, “Taonani aneneri ena onse ngati munthu mmodzi akulosera za chipambano cha mfumu. Mawu anunso agwirizane ndi awo ndipo muyankhule zabwino.”
13 Le hoe t’i Mikaià: Kanao veloñe t’Iehovà, ze tsaraen’ Añahareko, izay ty ho volañeko.
Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndidzanena zimene Mulungu wanga andiwuze.”
14 Ie pok’ amy mpanjakay, le hoe i mpanjakay ama’e: O Mikaià, hañavelo mb’e Ramote-gilade mb’eo hao zahay hialy he hifoneñako? le hoe re; Mionjona le mandreketa, fa hatolotse am-pità’o.
Iye atafika mfumu inamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite ku nkhondo kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Kathireni nkhondo ndipo kapambaneni, pakuti mzindawo udzaperekedwa mʼdzanja lanu.”
15 Le hoe i mpanjakay tama’e: Impire ty nandiliako azo ty tsy hivolañe ndra inoñ’ inoñe naho tsy ty hahiti’e amy tahina’ Iehovày?
Mfumu inati kwa iye, “Kodi ndikuwuze kangati kuti ulumbire kuti usandiwuze chilichonse koma zoonadi mʼdzina la Yehova?”
16 Le hoe re: Nitreako te niparaitak’ an-kaboañe ey iaby t’Israele hoe añondry tsy amam-piarake; le hoe t’Iehovà; Tsy amam-piarake iretoañe, apoho songa himpoly mb’an-kiboho’e an-kanintsiñe ondatio.
Ndipo Mikaya anayankha kuti, “Ine ndinaona Aisraeli atabalalika mʼmapiri monga nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mu mtendere!’”
17 Le hoe ty mpanjaka’ Israele am’ Iehosafate; Tsy vinolako hao t’ie tsy hitoky hasoa amako, fa raty?
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti sandinenera zabwino koma zoyipa zokhazokha?”
18 le natovo’e ty hoe, Janjiño arè ty tsara’ Iehovà: Nitreako niambesatse am-piambesa’ey t’Iehovà, le nijohañe ampità’e havana naho havia’e eo iaby i valobohòn-dike­rañey.
Mikaya anapitiriza ndi kunena kuti, “Imvani tsono mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu ndi gulu lonse lakumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi lamanzere.
19 Le hoe t’Iehovà: Ia ty hanigike i Aka­be mpanjaka’ Israele, hampionjone’e mb’ eo hikorovoke e Ramote-gilade añe? Aa le inao ty raike, le inay ka ty ila’e.
Ndipo Yehova anati, ‘Ndani amene adzamunyengerere Ahabu mfumu ya Israeli kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi ndi kukafera komweko?’ “Wina ananena zina, winanso ananena zina.”
20 Loneake amy zao ty fañahy nijohañe añatrefa’ Iehovà, nanao ty hoe: Izaho ty hanjizy aze. Le hoe t’Iehovà ama’e: Akore?
Pomaliza mzimu wina unatuluka ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, “Ine ndikamunyengerera!” Yehova anafunsa kuti, “Ukagwiritsa ntchito njira yanji?”
21 Le hoe re, Hionjomb’eo iraho ho fañahin-dremborake am-palie’ o mpitoki’e iabio. Le hoe re: Toe ho sigihe’o vaho hañeneke; akia, ano.
Mzimuwo unati, “Ine ndidzapita ndi kukhala mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri ake onse!” Yehova anati, “‘Iwe ukamunyengadi iyeyo. Pita kachite zimenezo.’
22 Aa le ingo te nampipoha’ Iehovà am-palie’ o mpitoki’o reo ty fañahy mandañitse; fa toe hankàñe ty nitsara’ Iehovà azo.
“Choncho Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anuwa. Yehova waneneratu kuti inu mukaona tsoka.”
23 Nañarine aze t’i Tsidkià ana’ i Kenaanà, le tinampifi’e ty fiambina’ i Mikaià vaho nanao ty hoe: Nimb’ aia ty fañahi’ Iehovà boak’ amako hivolañe ama’o?
Ndipo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi ndi kumenya khofi Mikaya. Zedekiya anafunsa kuti, “Kodi mzimu wochokera kwa Yehova unadzera njira iti pamene unachoka kwa ine kupita kwa iwe?”
24 Le hoe t’i Mikaià: Inao! ho isa’o amy andro himoaha’o an-traño añate’e ao hietaha’oy.
Mikaya anayankha kuti, “Udzadziwa pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
25 Le hoe ty mpanjaka’ Israele, Endeso t’i Mikaià, le ampolio amy Amone mpifehe’ i rovay naho am’ Ioase anam-panjaka ao;
Pamenepo mfumu ya Israeli inalamula kuti, “Tengani Mikaya ndipo mupite naye kwa Amoni, wolamulira mzindawo ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu,
26 le ano ty hoe: Hoe i mpanjakay: Apoho an-drohy ao tia; vaho fahano mofon-kasotriañe naho ranom-pijaleañe, ampara’ te mimpoly an-kanintsin-draho.
ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyike munthu uyu mʼndende ndipo musamupatse kanthu kalikonse koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwera mwamtendere.’”
27 Le hoe t’i Mikaià, Aa kanao himpoly an-kanintsin-drehe, tsy nitsara añamako t’Iehovà. Le hoe re: Janjiño izay ry ondatio, inahareo iaby.
Mikaya anayankhula kuti, “Ngati inu mukabwera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo anawonjeza kuti, “Anthu nonsenu, mumve zimene ndanenazi.”
28 Aa le nionjoñe mb’e Ramote-gilade mb’eo i mpanjaka’ Israeley naho Iehosafate mpanjaka’ Iehoda.
Choncho mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
29 Le hoe ty mpanjaka’ Israele am’ Iehosafate; Hihonohono iraho te hizilik’ an-kotakotak’ ao; f’ihe ka, aombeo o saro’o mireparepao. Aa le nañonohono-vatañe i mpanjaka’ Israeley; vaho nimoak’ an-kotakotak’ ao iereo.
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Ine ndipita ku nkhondo modzibisa koma iwe uvale mikanjo yaufumu.” Kotero mfumu ya Israeli inadzibisa ndipo inapita ku nkhondoko.
30 Fe hoe ty nafanto’ i mpanjaka’ i Aramey amo mpifehen-tsarete’eo; Ko ialia’o ty kedeke ndra ty bey naho tsy i mpanjaka’ Israeley avao.
Tsono mfumu ya Aramu inalamulira olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu koma mfumu ya Israeli yokha.”
31 Ie amy zao naho niisa’ o mpifehen-tsareteo t’Ie­hosafate le hoe iereo: Ingo i mpanjaka’ Israeley. Aa le nitoliha’ iareo hialy; fe nikoike t’Iehosafate le nañolotse aze t’Iehovà vaho niroroten’ Añahare iereo hisitake.
Olamulira magaleta ataona Yehosafati, iwo anaganiza kuti, “Mfumu ya Israeli ndi iyi.” Kotero anatembenuka kukamenyana naye koma Yehosafati anafuwula, ndipo Yehova anamuthandiza. Mulungu anawabweza mʼmbuyo,
32 Aa ie nirendre’ o mpifehe sareteo t’ie tsy i mpanjaka’ Israeley le nivalike tsy nihoridaña’e.
pakuti olamulira magaleta ataona kuti sanali mfumu ya Israeli, anasiya kumuthamangitsa.
33 Fe teo t’indaty nampi­voho-pale tsinahi’e nahatrofake i mpanjaka’ Israeley añivo’ o fikala’e ambane naho i aron’ araña’ey, le hoe re amy mpin­day saretey; Ampivioño o fità’oo, le ampiavoto amy valobohòkey iraho fa loho-fere.
Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndipo analasa mfumu ya Israeli pakati polumikizira malaya achitsulo. Mfumu inawuza oyendetsa galeta kuti, “Bwerera, undichotse pa nkhondo pano. Ndavulazidwa.”
34 Niindra avao i hotakotakey amy andro zay; ie amy zao nahafijohañe an-tsarete ao niatreke o nte-Arameo i mpanjaka’ Israeley am-para’ te hariva; le nihomake te nitsofotse i àndroy.
Nkhondo inakula kwambiri tsiku lonse, ndipo mfumu ya Israeli inakhala tsonga mʼgaleta lake kuyangʼanana ndi Aaramu mpaka madzulo. Ndipo pamene dzuwa linkalowa inamwalira.

< 2 Tantara 18 >