< 1 Samoela 29 >
1 Natonto’ o nte-Pilistio e Afeke eo ty valobohò’ iareo vaho nitobe marine i rano migoangoa’ Iezreeley o ana’ Israeleo.
Afilisti anasonkhanitsa asilikali awo onse ku Afeki, ndipo Israeli anamanga misasa yawo pa chitsime cha Yezireeli.
2 Aa ie nandahatse o mpirai-lia’e zato naho arivoo o talèm-Pilistio, le nivoly i Akise t’i Davide naho ondati’eo.
Pamene atsogoleri a Afilisti ankatsogolera magulu awo ankhondo a miyandamiyanda, Davide ndi ankhondo ake ankayenda pambuyo pamodzi ndi Akisi.
3 Le hoe o talèm-Pilistio; Manao inoñ’ atoy o nte-Evreo? Le hoe ty natoi’ i Akise amo talèm-Pilistio, Tsy i Davide hao i mpitoro’ i Saoley nimpiamako tamy andro zay, o taoñe rezaoy? Ie mboe tsy nahatreavako hila mifototse amy nivotraha’e amako pake henaneo.
Tsono atsogoleri a Afilisti aja anafunsa kuti, “Kodi Ahebri awa akufuna chiyani?” Akisi anayankha kuti, “Uyu ndi Davide, mtumiki wa Sauli mfumu ya Israeli. Iye wakhala ndi ine kwa masiku ndithu, kapena titi zaka ndipo kuyambira tsiku limene anachoka kwa Sauli mpaka lero, ine sindinapeze cholakwa mwa iye.”
4 F’ie niboseha’ o talèm-Pilistio le hoe ty asa’ o talèm-Pilisitio ama’e: Ampolio hibalike mb’amy toetse natolo’o azey mb’eo tsy hindre aman-tika an-kotakotak’ ao tsy mone hivalike ho rafelahy t’ie mialy, inoñe ty ho fifampilongoañe soa ama’e naho i talè’ey naho tsy o loha’ ondaty retiañeo?
Koma atsogoleri a ankhondo a Afilisti anamukwiyira Akisi kwambiri ndipo anati, “Mubweze munthuyu kuti abwerere ku malo amene unamupatsa. Iye asapite nafe ku nkhondo kuopa kuti angadzasanduke mdani wathu. Kodi iyeyu adzadziyanjanitsa bwanji ndi mbuye wake? Iyeyutu adzadziyanjanitsa ndi mbuye wake pakupha anthu ali panowa?
5 Tsy ie hao i Davide nitakasie’ iereo an-tsinjake ty hoe: Zinama’ i Saole o arivo’eo naho i Davide o aleale’eo?
Paja ameneyu ndi Davide yemwe ankamuvinira namuyimbira kuti, “‘Sauli wapha anthu 1,000 koma Davide wapha miyandamiyanda?’”
6 Kinoi’ i Akise ama’e amy zao t’i Davide le nanao ama’e ty hoe: Kanao veloñe t’Iehovà, vañon-drehe, le soa am-pahatreavako ty fiavota’o naho ty fimpolia’o amy valobohòkey pak’ amy ihe nindre amakoy; le tsy nahatrea hila ama’o iraho sikal’ amy andro nomba’o amako pake henaneo; f’ie tsy no’ o talèo.
Kotero Akisi anayitana Davide ndipo anamuwuza kuti, “Pali Yehova wamoyo, iwe wakhala wodalirika ndipo chikanakhala chinthu chabwino kuti uzimenya nkhondo pamodzi nane popeza chibwerere iwe kuno ine sindinapeze cholakwa chilichonse ndi iwe. Koma atsogoleri enawa ndiwo sakukufuna.
7 Aa le mimpolia, le mañaveloa am-panintsiñañe, tsy hanjehara’o o talèm-Pilistio.
Tsono bwerera. Upite mu mtendere kuopa kuti ungachite kanthu kena koyipira atsogoleri a Afilistiwa.”
8 Aa hoe t’i Davide amy Akise, Ino o nanoekoo? Ino ty nioni’o amy mpitoro’oy amo hene andro nindrezako ama’o pak’ androanio, te tsy hionjonako hialy amo rafelahin-talèko mpanjakao?
Davide anafunsa Akisi kuti, “Kodi ndachita chiyani? Kodi mwapeza cholakwa chotani mwa ine mtumiki wanu chiyambire kukutumikirani mpaka lero? Tsono chifukwa chiyani sindingapite kukamenya nkhondo ndi adani a mbuye wanga mfumu?”
9 Le hoe ty natoi’ i Akise amy Davide: Fantako t’ie soa am-pahatreavako, manahake ty anjelin’ Añahare; fe sinaotsi’ o talèm-Pilistio ty hoe t’ie tsy hitraok’ aman-tika hionjom-ban-kotakotake mb’eo.
Akisi anayankha kuti, “Ine ndikudziwa kuti ndiwe wangwiro ngati mngelo wa Mulungu. Komabe atsogoleri a ankhondo a Afilisti akuti, ‘Davide asapite nafe ku nkhondo.’
10 Aa le mañaleñaleña rekets’ o mpitoro’ i talè nindre ama’oo; le mañampitsoa, ie mazava, le miavota.
Tsono udzuke mmamawa, pamodzi ndi ankhondo ako amene unabwera nawo, ndipo unyamuke kukangocha.”
11 Aa le niampitso t’i Davide, ie naho ondati’eo niavotse amy maraiñey, nimpoly mb’an-tane’ o nte-Pilistio mb’eo; vaho nionjomb’e Iezreele mb’eo o nte-Pilistio.
Choncho Davide ndi anthu ake anadzuka mmamawa kubwerera ku dziko la Afilisti. Koma Afilistiwo anapita ku Yezireeli.