< 1 Mpanjaka 16 >

1 Aa le niheo am’Ieho ana’ i Kananý ty tsara’ Iehovà amy Baasa, nanao ty hoe:
Ndipo Yehova anayankhula kudzera mwa Yehu mwana wa Hanani, mawu odzudzula Baasa kuti,
2 Kanao naonjoko amy debokey irehe naho nanoeko mpifehe Israele, ondatikoo, naho nañaveloa’o an-tsata’ Iarovame nampanan-tahiñe ondatiko Israeleo hanigik’ ahy hibosehako amo hakeo’eo,
“Ine ndinakukuza kuchokera pa fumbi ndipo ndinakupanga kuti ukhale mtsogoleri wa anthu anga Aisraeli, koma iwe wakhala ukuyenda mʼnjira za Yeroboamu ndi kuchimwitsa anthu anga Aisraeli naputa mkwiyo wanga chifukwa cha machimo awo.
3 inao! ho faopaoheko añe t’i Baasa naho i anjomba’ey vaho hanoeko hambañe amy anjomba’ Iarovame ana’ i Nebatey;
Taonani, Ine ndatsala pangʼono kuwononga Baasa pamodzi ndi nyumba yake, ndipo ndidzachitira nyumba yake zimene ndinachita pa nyumba ya Yeroboamu mwana wa Nebati.
4 ze amy Baasa mibanitse an-drova ao le ho hanen’ amboa vaho habotse’ o voron-tiokeo o aze miantantiritse an-teteke eio.
Agalu adzadya aliyense wa banja la Baasa amene adzafere mu mzinda, ndipo mbalame za mu mlengalenga zidzadya iwo amene adzafere kuthengo.”
5 Ty ila’ o fitoloña’ i Baasao naho o tolon-draha’eo vaho o haozara’eo; tsy fa sinokitse amy bokem-pamoliliañe o mpanjaka’ Israeleoy hao?
Tsono ntchito zina za Baasa ndi zamphamvu zake zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
6 Nitrao-piròtse aman-droae’e t’i Baasa naho nalenteke e Tirtsà ao vaho nandimbe aze ho mpifehe t’i Elà ana-dahi’e.
Baasa anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Tiriza. Ndipo Ela mwana wake anakhala mfumu mʼmalo mwake.
7 Mbore niatreatre i Baasa naho i anjomba’ey, am-pità’ Iehò, mpitoky, ana’ i Kananý ty tsara’ Iehovà, ty amo haloloañe iaby nanoe’e am-pivazohoa’ Iehovào, hanigìk’ aze hiforoforo amo fitoloñam-pità’eo, ie nanahake i anjomba’ Iarovame nañohofa’e lozay.
Komatu Yehova anayankhula kwa Baasa pamodzi ndi banja lake lonse kudzera mwa mneneri Yehu mwana wa Hanani, chifukwa cha zoyipa zonse zimene iye anachita pamaso pa Yehova, kukwiyitsa Yehovayo nakhala ngati nyumba ya Yeroboamu ndiponso chifukwa anawonongeratu banja la Yeroboamu.
8 Amy taom-paha-roapolo-eneñ’ ambi’ i Asa mpanjaka’ Iehoday, ty namotora’ i Elà ana’ i Baasa nifehe Israele e Tirtsà ao vaho nifehe roe taoñe.
Mʼchaka cha 26 cha ufumu wa Asa mfumu ya Yuda, Ela mwana wa Baasa anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira ku Tiriza zaka ziwiri.
9 Nikinià’ i Zimrý mpitoro’e, mpifeleke ty an-tsasa’ o sarete’eo, ie e Tirtsà añe nigenoke ho mamo añ’ akiba’ i Artsà, mpamandro’ i anjomba’e e Tirtsày,
Zimuri, mmodzi mwa akuluakulu ake, amene ankalamulira theka la magaleta ake, anamuchitira chiwembu. Nthawi imeneyi Ela anali ku Tiriza, akumwa koledzera nako mʼnyumba ya Ariza, munthu amene ankayangʼanira nyumba yaufumu ku Tiriza.
10 le nizilik’ ao ty Zimrý nanjevoñe naho namono aze an-taom-paha-roapolo-fito’ ambi’ i Asa, mpanjaka’ Iehoda vaho nandimbe aze nifeleke.
Zimuri anadzalowa, namukantha ndi kumupha mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda. Ndipo Zimuriyo anakhala mfumu mʼmalo mwake.
11 Ie niorotse nifehe naho vata’e niambesatse amy fiambesa’ey, le fonga zinama’e ty anjomba’ i Baasa; tsy nenga’e raike amo longo’eo, ndra amo rañe’eo ty namany an-kijoly.
Zimuri atangoyamba kulamulira, anapha banja lonse la Baasa. Sanasiyepo munthu wamwamuna ndi mmodzi yemwe, wachibale kapena bwenzi lake.
12 Fonga narotsa’ i Zimrý ty anjomba’ i Baasa, ty amy tsara’ Iehovà nafe’e amy Baasa añamy Iehò, mpi­toky,
Choncho Zimuri anawononga banja lonse la Baasa, molingana ndi mawu amene Yehova anayankhula motsutsa Baasa kudzera mwa mneneri Yehu,
13 ty amo hakeo’ i Baasao naho o tahi’ i Elà ana’eo, amo ha­keo’eo naho ie nampanan-tahiñe Is­raele vaho nanigike ty haviñera’ Iehovà Andrianañahare’ Israele amo hakoaha’ iareoo.
chifukwa cha machimo onse amene Baasa ndi mwana wake Ela anachita nachimwitsa Israeli, anakwiyitsa Yehova, Mulungu wa Israeli ndi mafano awo osapindulitsa.
14 Aa naho o fitoloña’ i Elà ila’eo, o fonga raha nanoe’eo; tsy fa sinokitse amy bokem-pamolili­añe o mpanjaka’ Israeleoy hao?
Tsono ntchito zina za Ela ndi zina zonse zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
15 Ie an-taom-paha-roapolo-fito’ ambi’ i Asa mpanjaka’ Iehoda, le nifehe fito andro e Tirtsà ao t’i Zimrý. Nitobe hañatreatre’ i Gebetonen-te-Pelistio, ondatio henane zay.
Mʼchaka cha 27 cha Asa mfumu ya Yuda, Zimuri analamulira ku Tiriza masiku asanu ndi awiri. Gulu la ankhondo linali litamanga misasa pafupi ndi Gibetoni, mzinda wa Afilisti.
16 Aa ie jinanji’ ondaty an-tobe ao, ty hoe: Nikilily t’i Zimrý namono i mpanjakay, le nanoe’ Israele iaby mpanjaka’ Israele t’i Omrý, mpifehe’ i valobohòkey an-tobe ao amy andro zay.
Ankhondo amene anali ku misasa atamva kuti Zimuri wachita chiwembu ndi kupha mfumu, tsiku lomwelo ku misasako anasankha Omuri, mkulu wa ankhondo kukhala mfumu ya Israeli.
17 Niavotse boak’e Gibetone t’i Omrý rekets’ Israele iaby nañarikatoke i Tirtsà.
Tsono Omuri ndi Aisraeli onse amene anali naye anachoka ku Gibetoni ndi kukazinga Mzinda wa Tiriza.
18 Naho nioni’ i Zimrý t’ie nandrambe i rovay, le nimoak’ amy fitilik’ abo’ i anjom­bam-panjakaiy, le finoro­toto’e ama’e i anjombam-panjakay vaho nihomake,
Zimuri ataona kuti mzinda walandidwa, anathawira ku nsanja ya nyumba ya mfumu ndipo anatentha nyumbayo iye ali momwemo. Kotero iyeyo anafa,
19 ty amo hakeo nanoe’e an-karatiañe am-pivazohoa’ Iehovào amy naña­veloa’e an-tsata’ Iarovamey vaho amo tahiñe nanoe’e hampandilatse Israeleo.
chifukwa cha machimo amene iye anachita, kuchita zoyipa pamaso pa Yehova ndi kuyenda mʼnjira za Yeroboamu, nachimwitsa nazo Aisraeli.
20 Aa naho o fitoloña’ i Zimrý ila’eo; i fikitrohan-draty nanoe’ey; tsy fa sinokitse amy bokem-pamolili­añe o mpanjaka’ Israeleoy hao?
Tsono ntchito zina za Zimuri ndi chiwembu chake chimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
21 Nizara roe amy zao o nte-Israeleo; nañorike i Tibný ana’ i Ginate ty vaki’ ondatio hanoe’ iereo mpanjaka, le nañorike i Omrý ka ty vaki’e.
Pambuyo pake Aisraeli anagawikana pakati: theka linatsatira Tibini mwana wa Ginati kuti limulonge ufumu, ndipo theka lina linatsatira Omuri.
22 Fe naha­rotsake o mpaño­rike i Tibný ana’ i Ginateo o naño­rike i Omrio; aa le nikoromake t’i Tibný vaho nifehe t’i Omrý.
Koma anthu otsatira Omuri anali amphamvu kupambana amene ankatsatira Tibini mwana wa Ginati. Choncho Tibini anafa ndipo Omuri anakhala mfumu.
23 Amy taom-paha-telopolo-raik’ ambi’ i Asa mpanjaka’ Iehoday ty niorota’ i Omrý nifehe’ Israele, le nifeleke folo-tao-ro’amby, nifehe enen-taoñe e Tirtsà.
Mʼchaka cha 31 cha Asa mfumu ya Yuda, Omuri anakhala mfumu ya Israeli, ndipo analamulira zaka 12 ndi miyezi isanu ndi umodzi ku Tiriza.
24 Vinili’e talen­ta volafoty roe amy Semere ty tamboho atao So­merone, le nandranjy amy haboañey vaho nitokave’e Somerone i rova nam­boare’ey ty amy tahina’ i Semere tompo’ i tambohoiy.
Iye anagula phiri la Samariya kwa Semeri pa mtengo wa ndalama 6,000 za siliva ndipo pa phiripo anamangapo mzinda, nawutcha Samariya, potsata dzina la Semeri, dzina la mwini wakale wa phirilo.
25 Ni­to­lon-karatiañe am-pihaino’ Iehovà t’i Omrý, lombolombo’ o niaolo aze iabio o haloloañe nanoe’eo;
Koma Omuri anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo anachimwa kuposa mafumu ena onse amene analipo iye asanakhale mfumu.
26 amy te fonga nañaveloa’e o sata’ Iarovame ana’ i Nebateo naho i tahiñe nampanaña’e hakeo Israeley, ie nanigìke Iehovà Andrianañahare’ Israele hiviñera’e amo hakoaha’ iareoo.
Pakuti iye anayenda mʼnjira zonse za Yeroboamu mwana wa Nebati, ndipo tchimo lake anachimwitsa nalo Aisraeli, nakwiyitsa Yehova Mulungu wa Israeli ndi mafano awo opandapake.
27 Le o fitoloña’ i Omrý ila’eo naho ty haozarañe naboa’e, tsy fa sinokitse amy bokem-pamoliliañe o mpanjaka’ Israeleoy hao?
Tsono ntchito zina za Omuri ndi zamphamvu zimene anachita, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
28 Nitrao-piròtse aman-droae’e t’i Omrý naho nalenteke e Somerone ao vaho nandimbe aze nifehe t’i Akabe, ana’e.
Choncho Omuri anamwalira nayikidwa mʼmanda amene anayikidwa makolo ake ku Samariya. Ndipo Ahabu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
29 An-taom-paha-telopolo-valo’ ambi’ i Asa mpanjaka’ Iehoda ty niorota’ i Akabe ana’ i Omrý nifehe Israele le nifeleke Israele e Somerone ao roapolo taoñe ro’amby;
Mʼchaka cha 38 cha ufumu wa Asa, mfumu ya Yuda, Ahabu mwana wa Omuri anakhala mfumu ya Israeli nalamulira Israeli ku Samariya zaka 22.
30 nanao haloloañe am-pivazohoa’ Iehovà t’i Akabe ana’ i Omrý, mandikoatse o niaolo aze iabio.
Ahabu mwana wa Omuri anachita zoyipa zambiri pamaso pa Yehova kupambana mafumu onse akale.
31 Ie amy zao, hoe nimaivañ’ ama’e ty manjotik’ amo hakeo’ Iarovame ana’ i Nebateo t’ie mbore nañenga Iizebele ho vali’e, ie ana’ i Etebaale mpanjaka’ o nte-Tsidoneo naho nimb’eo nitoro­ñe i Baale vaho nitalahoa’e.
Iye sanachiyese ngati chinthu chochepa chabe kuchita machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, koma anakwatiranso Yezebeli, mwana wa Etibaala mfumu ya Asidoni, nayamba kutumikira Baala ndi kumupembedza.
32 Nampitroara’e kitrely ty Baale amy anjomba’ i Baale niran­jie’e e Someroney.
Iye anapangira Baala guwa lansembe mʼnyumba ya Baala imene anamanga ku Samariya.
33 Nam­boare’ i Akabe ka ty ala-vondro; nilombolombo’ o mpanjaka’ Israele niaolo aze iabio t’i Akabe ami’ty fani­giha’e ty haviñera’ Iehovà Andrianañahare’ Israele.
Ahabu anapanganso fano la Asera ndi kukwiyitsa kwambiri Yehova Mulungu wa Israeli, kupambana mafumu onse a Israeli amene analipo iye asanakhale mfumu.
34 Tañ’ andro’e ty namboare’ i Kiale ty Ierikò. I Abirame tañolo­ño­loña’e ty nampipoha’e o mananta’eo le i Segobe tsitso’e ty nampitroara’e o lalambeio ty amy tsara’ Iehovà nitsa­rae’e añam’ Iehosoa ana’ i Noney.
Pa nthawi ya Ahabu, Hiyeli wa ku Beteli anamanganso mzinda wa Yeriko. Pa nthawi yomanga maziko ake, mwana wake woyamba wa mwamuna, Abiramu anamwalira, ndipo pa nthawi yomanga zipata zake, mwana wa mngʼono wa mwamuna Segubu, anamwaliranso. Izi zinachitika monga momwe Yehova ananenera kudzera mwa Yoswa mwana wa Nuni.

< 1 Mpanjaka 16 >