< लूका 1 >
1 बऊत जणेया सेयो गल्ला, जो आसा बीचे ओईया, इतियास लिखणे रे आसा री मताद कित्ती,
Ambiri anayesa kufotokoza nkhani ya zimene zinakwaniritsidwa pakati pathu,
2 जेड़ा कि पईले ई तिने जो इना गल्ला खे देखणे वाल़े और वचनो खे मानणे वाल़े सेवक थे, आसा गे पऊँछाईया।
monga mmene zinaperekedwera kwa ife ndi iwo amene anaona poyambirira ndi atumiki a mawu.
3 तेबेई तो, ओ श्रीमान् थियुफिलुस! माखे बी ये ठीक लगेया कि तिना सबी गल्ला रा सारा आल शुरूओ तेई ठीक-ठीक पता लगाई की तिना ताखे एक-एक करी की लिखूँ।
Popeza inenso ndafufuza mosamalitsa chilichonse kuyambira pachiyambi, zandikomera kukulemberani mwatsatanetsatane inu wolemekezeka Tiofilo,
4 ताकि तूँ ये जाणी लो कि यो गल्ला, जिना री तैं शिक्षा पाई राखी, केड़िया अटल ए।
kuti mudziwe bwinobwino zoona za zinthu zimene mwaphunzitsidwa.
5 यहूदिया प्रदेशो रे राजा हेरोदेसो रे बखते अबिय्याहो रे दलो रे जकरयाह नाओं रा एक पुरोईत था और तेसरी लाड़िया रा नाओं इलीशिबा था। ये दोनो लाड़ा-लाड़ी हारूणो रे कुलो रे थे।
Mʼmasiku a Herode, mfumu ya Yudeya, kunali wansembe dzina lake Zakariya wa gulu la ansembe la Abiya; mkazi wake Elizabeti analinso wa fuko la Aaroni.
6 सेयो दोनो परमेशरो सामणे तर्मी थे और परमेशरो री सारी आज्ञा और बिधिया पाँदे निर्दोष चलो थे।
Onse awiri anali olungama pamaso pa Mulungu, ndipo amasunga malamulo ndi malangizo onse a Ambuye osalakwa konse.
7 तिना रे कोई ल्वाद नि थी, कऊँकि इलीशिबा बांझ थी और सेयो दोनो स्याणे ऊईगे थे।
Koma analibe ana chifukwa Elizabeti anali wosabereka; ndipo onse anali okalamba.
8 एक दिन जेबे जकरयाह आपणे दलो री बारिया पाँदे परमेशरो सामणे पुरोईतो रा काम करो था।
Nthawi yogwira ntchito yotumikira ansembe a gulu la Zekariya, Zekariya ankatumikira ngati wansembe pamaso pa Mulungu,
9 तेबे पुरोईता री रवाजा रे मुताबिक, तेसरे नाओं री चिट्ठी निकल़ी, कि परमेशरो रे मन्दरो रे जाई की तूप बाल़।
Zakariyayo anasankhidwa mwa maere, monga mwa mwambo wa unsembe, kupita mʼNyumba ya Ambuye kukafukiza lubani.
10 और तूप बाल़ने रे बखते, लोका री सारी मण्डल़ी बारे मन्दरो रे आँगणो रे प्रार्थना करने लगी री थी।
Ndipo nthawi yofukiza lubani itafika, gulu lonse lopembedza linkapemphera kunja.
11 तेबे जकरयाहो खे प्रभुए रा स्वर्गदूत तूपो री वेदिया रे दाँणे कनारे खड़ेया रा दिशेया।
Kenaka mngelo wa Ambuye anaonekera kwa iye, atayimirira ku dzanja lamanja la guwa lofukizira.
12 जकरयाह तेसखे देखी की कबराईगा और बऊत डरीगा।
Zakariya ataona mngeloyo, anadzidzimuka ndipo anagwidwa ndi mantha.
13 पर स्वर्गदूते तेसखे बोलेया, “ओ जकरयाह! डर नि, कऊँकि परमेशरे तेरी प्रार्थना सुणी ली री और जो तेरी लाड़ी इलीशिबा ए, तेसा रे ताखे एक पाऊ जमणा और तैं तेसरा नाओं यूहन्ना राखणा।
Koma mngeloyo anati kwa iye: “Usachite mantha, Zakariya; pemphero lako lamveka. Mkazi wako Elizabeti adzakuberekera iwe mwana wamwamuna ndipo udzamutche dzina loti Yohane.
14 ताखे आनन्द और खुशी ऊणी और बऊत सारे लोक तेसरे जमणे ते खुश ऊणे।
Ndipo adzakhala chimwemwe ndi chisangalalo kwa iwe, ndipo ambiri adzasangalala chifukwa cha kubadwa kwake,
15 कऊँकि से परमेशरो सामणे महान् ऊणा, तेस अँगूरा रा रस और शराब कदी नि पीणा और से आपणी माया रे गर्भो तेई पवित्र आत्मा ते परेया रा ऊणा।
chifukwa adzakhala wamkulu pamaso pa Ambuye. Iye sadzamwa vinyo kapena chakumwa choledzeretsa, ndipo adzazadzidwa ndi Mzimu Woyera kuyambira pa kubadwa.
16 तेस इस्राएलो बीचा ते कई जणे, तिना रे प्रभु परमेशरो री तरफा खे फेरने।
Iye adzabweretsanso Aisraeli ambiri kwa Ambuye Mulungu wawo.
17 से एलिय्याह री आत्मा और सामर्था रे ऊई की तेसरे आगे-आगे चलणा ताकि पितरा रा मन बाल-बच्चेया री तरफा खे फेरो। आज्ञा नि मानणे वाल़ेया खे तर्मिया री समजा रे ल्याओ और प्रभुए खे एक लायक प्रजा त्यार करो।”
Ndipo iye adzabwera Ambuye asanabwere mu mzimu ndi mphamvu ya Eliya. Adzatembenuzira mitima ya abambo kwa ana awo ndi osamvera ku nzeru ya olungama, kuthandiza anthu kuti akonzekere kubwera kwa Ambuye.”
18 जकरयाहे स्वर्गदूतो ते पूछेया, “ये आऊँ किंयाँ जाणूं कि एड़ा ई मां साथे ऊणा? कऊँकि आऊँ और मेरी लाड़ी तो स्याणे ऊईगे रे।”
Zakariya anamufunsa mngeloyo kuti, “Kodi ndingatsimikize bwanji zimenezi? Ine ndine wokalamba ndipo mkazi wanga ali ndi zaka zambiri.”
19 स्वर्गदूते तेसखे बोलेया, “आऊँ जिब्राईल ए, जो परमेशरो सामणे खड़ा रओआ। आऊँ तां साथे गल्ला करने और ये सुसमाचार सुनाणे रिया तंईं पेजी राखेया
Mngeloyo anayankha kuti, “Ine ndine Gabrieli. Ndimayima pamaso pa Mulungu, ndipo ndatumidwa kwa iwe kudzakuwuza uthenga wabwinowu.
20 और देख जदुओ तक यो गल्ला पूरिया नि ऊई जाओगिया, तदुओ तक तूँ चुप रणा और बोली नि सकदा। कऊँकि तैं मेरिया गल्ला पाँदे कि सेयो आपणे बखते पूरिया ऊणिया, विश्वास नि कित्तेया।”
Ndipo kuyambira tsopano sudzatha kuyankhula kufikira izi zitachitika chifukwa sunakhulupirire mawu awa, amene adzakwaniritsidwe pa nthawi yake yoyenera.”
21 लोक जकरयाहो खे न्याल़दे रए और हैरान ऊईगे कि तेसखे मन्दरो रे इतणी देर किंयाँ ऊईगी?
Pa nthawiyi, anthu ankadikira Zakariya ndipo anadabwa chifukwa anatenga nthawi yayitali ali mʼNyumba ya Mulungu.
22 जेबे से बारे आया, तेबे से तिना साथे गलाई नि सकेया, तेबे तिना खे पता लगी गा कि तिने मन्दरो रे कोई दर्शन पाई राखेया, से तिना साथे साअरे रे गल्ला करदा रया और गूँगा ऊईगा।
Atatuluka sanathe kuyankhulana nawo. Anazindikira kuti anaona masomphenya mʼNyumbamo, chifukwa ankasonyeza zizindikiro kwa iwo koma sankatha kuyankhula.
23 जेबे मन्दरो रे तेसरे पुरोईतो रे कामो री सेवा करने रे दिन पूरे ऊईगे, तेबे से यरूशलेमो नगरो खे छाडी की आपणे कअरो खे चली गा।
Nthawi yake yotumikira itatha, anabwerera kwawo.
24 तेबे तेसरी लाड़ी इलीशिबा गर्भवती ऊईगी और पाँज मीन्ने तक आपू खे कअरे ये बोली की लकोए रे राखेया,
Zitatha izi, mkazi wake Elizabeti anakhala ndi pakati ndipo anadzibisa kwa miyezi isanu.
25 “मांणूए जो मेरी बेज्जती करी राखी, तिजी खे दूर करने खे, परमेशरे मां पाँदे कृपा करने खे एड़ा करी राखेया।”
Iye anati, “Ambuye wandichitira izi, kuti mʼmasiku ano wandionetsera kukoma mtima kwake ndi kuchotsa manyazi anga pakati pa anthu.”
26 इलीशिबा रे गर्भावस्था रे छटुए मीन्ने परमेशरो री तरफा ते जिब्राईल स्वर्गदूत गलील प्रदेशो रे नासरत नाओं नगरो रे,
Mwezi wachisanu ndi chimodzi, Mulungu anatuma mngelo Gabrieli ku Nazareti, mudzi wa ku Galileya,
27 एक कुआँरिया गे पेजेया। तेसारी मंगणी यूसुफ नाओं रे दाऊदो रे कराने रे एक माठे साथे ऊई थी। तेसा कुआँरिया रा नाओं मरियम था।
kwa namwali wopalidwa ubwenzi ndi Yosefe, wa fuko la Davide. Dzina la namwaliyo linali Mariya.
28 स्वर्गदूते तेसा गे पीतरे आयी की बोलेया, “खुशी और जय तेरी ओ, जेस पाँदे परमेशरो री कृपा ऊई री, प्रभु तां साथे ए।”
Mngeloyo anafika kwa iye nati, “Moni, inu amene Ambuye wakukomerani mtima kwambiri! Ambuye ali ndi inu.”
29 से तेस वचनो ते बऊत कबराई गी और सोचणे लगी कि ये केड़ी गल्ल ए?
Mariya anavutika kwambiri ndi mawu awa ndipo anadabwa ndi kulonjera kotere.
30 स्वर्गदूते तेसा खे बोलेया, “ओ मरियम! डर नि कऊँकि परमेशरो री कृपा तां पाँदे ऊई री।
Koma mngeloyo anati kwa iye, “Usachite mantha Mariya, pakuti wapeza chisomo pamaso Mulungu.
31 देख, तूँ गर्भवती ऊणी, तेरे एक पाऊ जमणा और तैं तेसरा नाओं यीशु राखणा।
Udzakhala woyembekezera ndipo udzabala mwana wamwamuna ndipo udzamupatse dzina loti Yesu.
32 से महान् ऊणा, और परमप्रदानो रा पुत्र ऊणा और प्रभु परमेशरे तेसरे पुरखा दाऊदो रा सिंहासन तेसखे देणा।
Iye adzakhala wamkulu ndipo adzatchedwa Mwana wa Wammwambamwamba. Ambuye Mulungu adzamupatsa Iye mpando waufumu wa abambo ake Davide,
33 और तेस याकूबो रे कराने रे सदा राज्य करना और तेसरे राज्य रा अंत कदी नि ऊणा।” (aiōn )
ndipo adzalamulira pa nyumba ya Yakobo ku nthawi zonse; ufumu wake sudzatha.” (aiōn )
34 मरियमे स्वर्गदूतो खे बोलेया, “ये किंयाँ ऊणा? आऊँ तो मर्दो खे जाणदी ई नि, कऊँकि आऊँ तो एबु कुँवारी ए”
Mariya anafunsa mngeloyo kuti, “Izi zingatheke bwanji popeza ine sindidziwa mwamuna?”
35 स्वर्गदूते तेसा खे जवाब दित्तेया, “पवित्र आत्मा तां पाँदे उतरना और परमप्रदानो री सामर्थ तां पाँदे छांयाँ करनी, तेबेई तो से, जो जमणे वाल़ा ए, तेसखे पवित्र और परमेशरो रा पुत्र बोलेया जाणा।
Mngelo anayankha kuti, “Mzimu Woyera adzabwera pa iwe ndipo mphamvu ya Wammwambamwamba idzakuphimba, ndipo Woyerayo amene adzabadwe adzatchedwa Mwana wa Mulungu.
36 देख, तेरे टब्बरो री इलीशिबा रे बी स्याणदे बखते पाऊ ऊणे वाल़ा ए। ये तेसा रा, जेसा खे बांझ बोलोए, छटा मीन्ना चली रा।
Ngakhale Elizabeti mʼbale wako adzakhala ndi mwana mu ukalamba wake ndipo iye amene amati ndi wosabereka, uno mwezi wake wachisanu ndi chimodzi.
37 कऊँकि परमेशर सब कुछ करी सकोआ।”
Pakuti palibe chinthu chosatheka ndi Mulungu.”
38 मरियमे बोलेया, “देख, आऊँ परमेशरो री दासी ए, मां साथे तेरे वचनो रे मुताबिक ओ।” तेबे स्वर्गदूत तेसा गे ते चली गा।
Mariya anayankha kuti, “Ine ndine mtumiki wa Ambuye. Zikhale kwa ine monga mwanenera.”
39 तिना दिना रे मरियम उठी की फटाफट पाह्ड़ी इलाके रे यहूदा प्रदेशो रे एक नगरो खे गई
Nthawi imeneyo anakonzeka ndipo anapita mofulumira ku mudzi wa ku mapiri a dziko la Yudeya,
40 और तेसे जकरयाहो रे कअरे जाई की इलीशिबा खे नमस्ते कित्ती।
kumene anakalowa mʼnyumba ya Zakariya nalonjera Elizabeti.
41 जिंयाँ ई इलीशिबे मरियमा री नमस्ते सुणी, तिंयाँ ई बच्चा तेसा रे पेटो रे उटकेया और ईलीशिबा पवित्र आत्मा ते फरी गी।
Elizabeti atamva moni wa Mariya, mwana anatakataka mʼmimba mwake, ndipo Elizabeti anadzazidwa ndi Mzimu Woyera.
42 तेबे तेसे मरियमा खे जोरे की बोलेया, “तूँ सबी जवाणसा बीचे धन्य ए और जेस बच्चे खे तां जन्म देणा से बी धन्य ए।
Anafuwula ndi mawu akulu kuti, “Ndiwe wodala pakati pa akazi, ndipo ndi wodala mwana amene udzabereke!
43 ये कृपा मां पाँदे केथा ऊई कि मेरे प्रभुए री आम्मा मांगे आयी?
Koma nʼchifukwa chiyani andikomera mtima kuti amayi a Ambuye anga abwere kwa ine?
44 जिंयाँ ई मैं तेरी नमस्ते सुणी, तिंयाँ ई बच्चा मेरे पेटो रे खुश ऊई की उटकणे लगेया।
Nthawi yomwe ndinamva mawu akulonjera kwanu, mwana anatakataka mʼmimba mwanga chifukwa cha chimwemwe.
45 धन्य ए से, जिने विश्वास कित्तेया कि जो गल्ला प्रभुए री तरफा ते तेसा गे बोलिया, सेयो पुरिया ऊणिया।”
Wodala iye amene wakhulupirira kuti chimene Ambuye wanena kwa iye chidzakwaniritsidwa!”
46 तेबे मरियमे बोलेया, “मेरा प्राण प्रभुए री बढ़ाई करोआ।
Ndipo Mariya anati: “Moyo wanga ulemekeza Ambuye.
47 और मेरी आत्मा मेरा उद्धार करने वाल़े परमेशरो ते खुश ए।
Ndipo mzimu wanga ukondwera mwa Mulungu Mpulumutsi wanga,
48 कऊँकि तिने आपणी दासिया कनारो खे देखेया, तेबेई तो, देखो, आजो ते सारे जुगा-जुगा रे लोका माखे धन्य बोलणा।
pakuti wakumbukira kudzichepetsa kwa mtumiki wake. Kuyambira tsopano mibado yonse idzanditcha wodala,
49 कऊँकि तिने शक्तिमाने मेरे बड़े-बड़े काम करी राखे और तेसरा नाओं पवित्र ए।
pakuti Wamkuluyo wandichitira ine zinthu zazikulu, dzina lake ndi loyera.
50 तेस परमेशरो री दया, जो तेसते डरोए, पीढ़िया री पीढ़िया तक बणी री रओई।
Chifundo chake chifikira kwa iwo amene amuopa Iye kufikira mibadomibado.
51 तिने आपणे आथो रे जरिए सामर्था रे काम दिखाए और जो आपू खे बड़ा समजोए, सेयो रूल़ाई ते।
Iye wachita zamphamvu ndi dzanja lake; Iye anabalalitsa iwo amene ali onyada mʼmaganizo awo.
52 तिने राजेया रा राज खत्म करी ता और शरीफ ऊच्चे कित्ते।
Iye anachotsa olamulira pa mipando yawo yaufumu, koma wakweza odzichepetsa.
53 तिने पूखे अच्छी चीजा ते रजाए और अमीर खाली आथे निकयाल़ी ते।
Iye wakhutitsa a njala ndi zinthu zabwino koma anachotsa olemera wopanda kanthu.
54 तिने आपणा सेवक इस्राएल सम्बाल़ी ता। ताकि आपणी तेसा दया रे वादे खे याद करुँ,
Iye anathandiza mtumiki wake Israeli, pokumbukira chifundo chake.
55 जो अब्राहम और तेसरे कुल़ो पाँदे सदा रणी, जेड़ा तिने म्हारे बाओ-दादेया खे बोलेया था।” (aiōn )
Kwa Abrahamu ndi zidzukulu zake ku nthawi zonse monga ananena kwa makolo athu.” (aiōn )
56 मरियम तकरीबन तीन मीन्ने तक तेती रई और तेबे कअरो खे चली गी।
Mariya anakhala ndi Elizabeti pafupifupi miyezi itatu ndipo kenaka anabwerera kwawo.
57 तेबे इलीशिबा रे बच्चा पैदा करने रा बखत पूरा ऊईगा और तेसा रे एक पाऊ जम्मेया।
Itakwana nthawi yoti Elizabeti abereke, anabereka mwana wamwamuna.
58 तेसा रे पड़ोसी और टब्बरो वाल़ेया जेबे ये सुणेया कि प्रभुए तेसा पाँदे बड़ी पारी दया करी राखी, सेयो तेसा साथे बऊत खुश ऊए।
Anansi ndi abale ake anamva kuti Ambuye anamuchitira chifundo chachikulu ndipo anakondwera naye pamodzi.
59 तेबे एड़ा ऊआ कि सेयो आठुए दिने बाल़को रा खतना करने आए और तेसरा नाओं, तेसरे बाओ रे नाओं पाँदे जकरयाह राखणे लगे।
Pa tsiku lachisanu ndi chitatu anabwera ndi mwana kuti adzachitidwe mdulidwe, ndipo anafuna kumupatsa dzina la abambo ake Zakariya,
60 तेबे बच्चे री आम्मे बोलेया, “ना; एसरा नाओं यूहन्ना राखणा।”
koma amayi ake anayankhula nati, “Ayi, atchulidwe kuti Yohane.”
61 तेबे तिने बोलेया, “तेरे टब्बरो रे एड़ा नाओं केसी रा निए।”
Iwo anati kwa iye, “Palibe mmodzi mwa abale ake amene ali ndi dzina limeneli.”
62 तेबे तिने तेसरे बाओ ते साअरे रे पूछेया, “तूँ एसरा क्या नाओं राखणा चाएया?”
Pamenepo anapanga zizindikiro kwa abambo ake kuti adziwe dzina limene akanakonda kumutcha mwanayo.
63 तेबे तिने लिखणे री पट्टी मुंगाई की लिखी ता, “एसरा नाओं यूहन्ना ए” और सब हैरान ऊईगे।
Iye anapempha poti alembepo, ndipo chodabwitsa kwa aliyense analemba kuti, “Dzina lake ndi Yohane.”
64 तेबे तेसरा मूँ और जीब तेबुई खुली गी। तेबे से बोलणे जोगा ऊईगा और परमेशरो रा धन्यवाद करने लगेया।
Nthawi yomweyo pakamwa pake panatsekuka ndi lilime lake linamasuka ndipo anayamba kuyankhula, nayamika Mulungu.
65 तेसरे ओरे-पोरे रणे वाल़े लोक डरी गे और तिना सबी गल्ला री चर्चा यहूदिया प्रदेशो रे सारे पाह्ड़ी इलाके रे फैली गी।
Anansi onse anachita mantha kwambiri, ndipo ku madera onse a kumapiri a Yudeya, anthu anayankhula zinthu zonsezi.
66 सब सुणने वाल़े आपणे-आपणे मनो रे बिचार करने लगे, “ये बाल़क केड़ा ऊणा?” कऊँकि परमेशरो रा आथ तेस साथे ए।
Aliyense amene anamva izi anadabwa nazo nafunsa kuti, “Kodi mwana uyu adzakhala wotani?” Pakuti dzanja la Ambuye lili pa iye.
67 तेबे तेसरा पिता जकरयाह पवित्र आत्मा ते परी गा और भविष्यबाणी करने लगेया,
Abambo ake, Zakariya, anadzazidwa ndi Mzimu Woyera ndipo ananenera kuti,
68 “प्रभु इस्राएलो रा परमेशर धन्य ए, जो तिने आपणे लोका कनारो खे देखेया और तिना खे छुटकारा दित्तेया
“Alemekezeke Ambuye, Mulungu wa Israeli chifukwa wabwera ndi kuwombola anthu ake.
69 और आपणे सेवक दाऊदो रे कराने रे आसा खे उद्धारकर्ता पेजी राखेया।
Iye wakweza nyanga yachipulumutso kwa ife mu nyumba ya mtumiki wake Davide.
70 जेड़ा तिने आपणे पवित्र भविष्यबक्तेया ते बुलवाया था, जो दुनिया रे शुरूओ ते ऊँदे ऊए आयी रे (aiōn )
(Monga mmene ananenera kudzera mwa aneneri oyera), (aiōn )
71 मतलब-आसा रे दुश्मणा ते और बैरिया रे आथो ते म्हारा उद्धार करी राखेया।
chipulumutso kuchoka kwa adani athu ndi kuchoka mʼdzanja la onse otida,
72 ताकि आसा रे बाप-दादेया पाँदे कृपा करी की आपणी पवित्र वाचा याद राखो
kuonetsa chifundo kwa makolo athu ndi kukumbukira pangano lake loyera,
73 और से कसम जो तिने आसा रे पिते अब्राहमो साथे खाई थी
lumbiro limene analumbira kwa kholo lathu Abrahamu:
74 कि तेस आसा खे ये देणा, ताकि आसे आपणे दुश्मणा रे आथो ते बची की
kutilanditsa ife mʼdzanja la adani athu, ndi kutipanga ife timutumikire Iye mopanda mantha,
75 परमेशरो सामणे पवित्रता, और धार्मिकता साथे सारी जिन्दगी नच्चके रई की तेसरी सेवा करदे रईए।
mʼchiyero ndi mʼchilungamo masiku athu onse.
76 ओ बाल़क! ताखे परमप्रदान परमेशरो रा भविष्यबक्ता बोलेया जाणा, कऊँकि तूँ प्रभुए री बाट त्यार करने खे तिना रे आगे-आगे चलणा।
“Ndipo iwe mwana wanga udzatchedwa mneneri wa Wammwambamwamba; pakuti udzapita patsogolo pa Ambuye kukonza njira yake,
77 ताकि तिना रे लोका खे उद्धारो रा ज्ञान देई सके, जो तिना रे पापो री माफिया ते मिलोआ।
kupatsa anthu ake chidziwitso cha chipulumutso kudzera mwa chikhululukiro cha machimo awo,
78 ये आसा रे परमेशरो री तेसा बड़िया दया ते ऊणा; जेसरी बजअ ते, स्वर्गो ते आसा पाँदे प्यागा रा प्रयासा ऊणा।
chifukwa cha chifundo chachikulu cha Mulungu wathu, ndipo kuwala kwa dzuwa kudzafikira ife kuchokera kumwamba,
79 ताकि न्हेरे रे और मरने वाल़ेया खे जिन्दगी देई सको, और आसा रे पैरा खे शान्तिया री बाटा रे सिदे चलाई सको।”
kuwalira iwo okhala mu mdima ndi mu mthunzi wa imfa, kutsogolera mapazi athu mu njira yamtendere.”
80 तेबे से बाल़क यूहन्ना बड़दा और आत्मा रे तागतबर ऊँदा गया और इस्राएलो रे सामणे आऊणे रे दिना तक, जंगल़ो रे रया।
Ndipo mwanayo anakula nakhala wamphamvu mu mzimu; ndipo anakhala ku chipululu mpaka pamene anaonekera poyera mu Israeli.