< Zabbuli 25 >

1 Zabbuli ya Dawudi. Eri ggwe, Ayi Mukama, gye ndeeta okusaba kwange.
Salimo la Davide. Kwa Inu Yehova, ndipereka moyo wanga.
2 Neesiga ggwe, Ayi Mukama, tondeka kuswala mu maaso g’abalabe bange. Tobaganya kumpangula.
Ndimadalira Inu Mulungu wanga. Musalole kuti ndichite manyazi kapena kuti adani anga andipambane.
3 Ddala ddala abakwesiga tebaajulirirenga, naye ab’enkwe baliswazibwa.
Aliyense amene amayembekezera kwa Ambuye sadzachititsidwa manyazi koma achinyengo ndiwo adzachititsidwe manyazi ndipo sadzakhala ndi chodzitetezera.
4 Njigiriza nga bwe nnaakolanga, Ayi Mukama, ondage amakubo go mwe nnaatambuliranga.
Ndidziwitseni njira zanu Inu Yehova, phunzitseni mayendedwe anu;
5 Onjigirizenga okunywerera ku mazima go, era onkulemberenga mu byonna; kubanga ggwe Katonda, ow’obulokozi bwange era essuubi lyange liri mu ggwe olunaku lwonna.
tsogolereni mʼchoonadi chanu ndi kundiphunzitsa, pakuti Inu ndinu Mulungu mpulumutsi wanga, ndipo chiyembekezo changa chili mwa Inu tsiku lonse.
6 Jjukira, Ayi Mukama, okusaasira kwo okunene, n’okwagala kwo okungi, kubanga byava dda.
Kumbukirani Inu Yehova chifundo ndi chikondi chanu chachikulu, pakuti ndi zakalekale.
7 Tojjukira bibi byange n’obujeemu bwange eby’omu buvubuka bwange. Onzijukire, Ayi Mukama, ng’okwagala kwo gye ndi bwe kuli, kubanga oli mulungi.
Musakumbukire machimo a ubwana wanga ndi makhalidwe anga owukira; molingana ndi chikondi chanu ndikumbukireni ine, pakuti Inu Yehova ndinu wabwino.
8 Mukama mulungi, era wa mazima, noolwekyo ayigiriza aboonoonyi ekkubo lye.
Yehova ndi wabwino ndi wolungama; choncho Iye akulangiza ochimwa mʼnjira yake.
9 Abawombeefu abaluŋŋamya mu kkubo ettuufu n’abayigiriza ekkubo lye.
Amatsogolera odzichepetsa kuti achite zolungama ndipo amawaphunzitsa njira zake.
10 Amakubo ga Mukama gonna gajjudde okwagala n’amazima eri abo abagondera endagaano ye n’ebiragiro bye.
Njira zonse za Yehova ndi zachikondi ndi zokhulupirika kwa iwo amene amasunga zofuna za pangano lake.
11 Olw’erinnya lyo, Ayi Mukama, onsonyiwe ebibi byange, kubanga bingi.
Chifukwa cha dzina lanu, Inu Yehova, khululukireni mphulupulu zanga, ngakhale kuti ndi zochuluka.
12 Omuntu wa ngeri ki atya Katonda? Oyo gw’anaayigirizanga okukwata ekkubo lye yamulondera.
Tsono ndani munthu amene amaopa Yehova? Yehova adzamulangiza njira yoti ayitsate.
13 Obulamu bwe bunajjuzibwanga emikisa gya Katonda, era bazzukulu be ensi eriba yaabwe.
Iye adzakhala pa ulemerero masiku ake onse, ndipo zidzukulu zake zidzalandira dziko ngati cholowa chawo.
14 Mikwano gya Mukama be bo abamugondera; anaababikkuliranga ekyama eky’endagaano ye.
Yehova amawulula chinsinsi chake kwa iwo amene amamuopa; amawulula pangano lake kwa iwowo.
15 Ntunuulira Mukama buli kiseera, kubanga yekka y’anzigya mu kabi.
Maso anga ali pa Yehova nthawi zonse, pakuti ndi Iye yekha amene adzawonjola mapazi anga mu msampha.
16 Nkyukira, Ayi Mukama, onkwatirwe ekisa, kubanga nsigadde bw’omu, era ndi munafu.
Tembenukirani kwa ine ndipo mundikomere mtima, pakuti ndili ndekhandekha ndipo ndikuzunzika.
17 Obuyinike bweyongedde mu mutima gwange; mponya okweraliikirira kwange.
Masautso a mu mtima mwanga achulukirachulukira; masuleni ku zowawa zanga.
18 Tunuulira ennaku endiko, weetegereze obulumi bwange; onzigyeko ebibi byange byonna.
Penyani mazunzo anga ndi zovuta zanga ndipo mufafanize machimo anga onse.
19 Laba abalabe bange nga bwe beeyongedde obungi n’okunkyawa kwe bankyawamu!
Onani mmene adani anga achulukira ndi momwe chidani chawo ndi ine chakulira.
20 Labiriranga obulamu bwange, obamponye; tondekanga mu buswavu, kubanga ggwe kiddukiro kyange.
Tetezani moyo wanga ndi kundilanditsa; musalole kuti ndichite manyazi, pakuti ndimathawira kwa Inu.
21 Amazima n’obulongoofu bindabirirenga, essubi lyange liri mu ggwe.
Kukhulupirika ndi kulungama kwanga kunditeteze, chifukwa chiyembekezo changa chili mwa Inu.
22 Nunula Isirayiri, Ayi Katonda, omuwonye emitawaana gye gyonna.
Wombolani Israeli Inu Mulungu, ku mavuto ake onse!

< Zabbuli 25 >