< Omubuulizi 7 >
1 Obwatiikirivu bw’erinnya eddungi businga eby’akawoowo ebirungi; n’olunaku olw’okufa lusinga olwo olw’okuzaalirwako.
Mbiri yabwino ndi yopambana mafuta onunkhira bwino, ndipo tsiku lomwalira ndi lopambana tsiku lobadwa.
2 Kirungi okulaga mu nnyumba ey’abakungubaga okusinga okulaga mu nnyumba ey’ebyassava. Kubanga buli omu wa kufa, ekyo kiteekwa okuba ku mutima gwa buli muntu.
Kuli bwino kupita ku nyumba yamaliro kusiyana ndi kupita ku nyumba yamadyerero: Pakuti imfa ndiye mathero a munthu aliyense; anthu amoyo azichisunga chimenechi mʼmitima mwawo.
3 Okunakuwala kusinga okuseka, kubanga amaaso amanakuwavu gazzaamu omutima amaanyi.
Chisoni nʼchabwino kusiyana ndi kuseka, pakuti nkhope yakugwa ndi yabwino chifukwa imakonza mtima.
4 Omutima gw’omugezi guba wamu n’abo abali mu nnaku; naye ogw’omusirusiru guba mu kusanyuka.
Mtima wa munthu wanzeru nthawi zonse umalingalira za imfa, koma mitima ya zitsiru imalingalira za chisangalalo.
5 Kirungi okussaayo omwoyo ku kunenya kw’omuntu ow’amagezi okusinga okuwuliriza ennyimba z’abasirusiru.
Kuli bwino kumva kudzudzula kwa munthu wanzeru kusiyana ndi kumvera mayamiko a zitsiru.
6 Okuseka kw’abasirusiru kuli ng’okutulikatulika kw’amaggwa agali mu muliro gw’entamu; na kino nakyo butaliimu.
Kuseka kwa zitsiru kuli ngati kuthetheka kwa moto kunsi kwa mʼphika, izinso ndi zopandapake.
7 Kya mazima, okunyigirizibwa kufuula ow’amagezi okuba omusirusiru, n’enguzi efaafaaganya okutegeera.
Kuzunza ena kumasandutsa munthu wanzeru kukhala chitsiru, ndipo chiphuphu chimawononga mtima.
8 Enkomerero y’ekintu esinga entandikwa yaakyo, n’omugumiikiriza asinga ow’amalala.
Mathero ake a chinthu ndi abwino kupambana chiyambi chake, ndipo kufatsa nʼkwabwino kupambana kudzikuza.
9 Tosunguwalanga mangu nga waliwo akusokaasoka, kubanga obusungu bubeera munda y’abasirusiru.
Usamafulumire kukwiya mu mtima mwako, pakuti mkwiyo ndi bwenzi la zitsiru.
10 Teweebuuzanga nti, “Lwaki ennaku ziri ez’edda zisinga zino?” Kubanga si kya magezi okwebuuza ekibuuzo ng’ekyo.
Usamafunse kuti, “Nʼchifukwa chiyani masiku amakedzana anali abwino kupambana masiku ano?” pakuti si chinthu chanzeru kufunsa mafunso oterewa.
11 Amagezi kintu kirungi, okufaanana ng’eky’obugagga ky’obusika, era kigasa abo abakyalaba enjuba.
Nzeru ngati cholowa, ndi chinthu chabwino ndipo imapindulitsa wamoyo aliyense pansi pano.
12 Amagezi kiwummulo, ng’ensimbi bwe ziri ekiwummulo, naye enkizo y’okumanya y’eno: amagezi gakuuma obulamu bw’oyo agalina.
Nzeru ndi chitetezo, monganso ndalama zili chitetezo, koma phindu la chidziwitso ndi ili: kuti nzeru zimasunga moyo wa munthu amene ali nazo nzeruzo.
13 Lowooza ku Katonda ky’akoze: ani ayinza okugolola ekyo ekyakyama Katonda kye yakola?
Taganizirani zimene Mulungu wazichita: ndani angathe kuwongola chinthu chimene Iye anachipanga chokhota?
14 Ebiseera bwe biba ebirungi, sanyuka; naye bwe biba ebibi, kirowoozeeko; Katonda eyakola ekimu era ye yakola ne kinnaakyo. Noolwekyo omuntu tayinza kuzuula kirimubaako mu nnaku ze ez’omu maaso.
Pamene zinthu zili bwino, sangalala; koma pamene zinthu sizili bwino, ganizira bwino: Mulungu ndiye anapanga nthawi yabwinoyo, ndiponso nthawi imene si yabwinoyo. Choncho munthu sangathe kuzindikira chilichonse cha mʼtsogolo mwake.
15 Mu bulamu bwange buno obutaliimu ndabye bino byombi: omutuukirivu azikiririra mu butuukirivu bwe, n’omukozi w’ebibi n’awangaalira mu bibi bye.
Pa moyo wanga wopanda phinduwu ndaona zinthu ziwiri izi: munthu wolungama akuwonongeka mʼchilungamo chake, ndipo munthu woyipa akukhala moyo wautali mʼzoyipa zake.
16 Teweefuulanga mutuukirivu ayitiridde wadde okwefuula ow’amagezi ow’ekitalo; oleme okwezikiriza.
Usakhale wolungama kwambiri kapena wanzeru kwambiri, udziwonongerenji wekha?
17 Tobanga mwonoonyi kakuzzi wadde okuba omusirusiru; oleme okufa ng’ekiseera kyo tekinnatuuka.
Usakhale woyipa kwambiri, ndipo usakhale chitsiru, uferenji nthawi yako isanakwane?
18 Ekyo kirungi okiyige, na kiri oleme kukibuusa maaso, kubanga oyo atya Katonda abyewala okubiyitiriza.
Nʼkwabwino kuti utsate njira imodzi, ndipo usataye njira inayo. Munthu amene amaopa Mulungu adzapewa zinthu ziwiri zonsezi.
19 Ow’amagezi ne bw’aba omu mu kibuga, aba w’amaanyi okusinga abakulembeze ekkumi ab’omu kibuga ekyo.
Nzeru zimapereka mphamvu zambiri kwa munthu wanzeru kupambana olamulira khumi a mu mzinda.
20 Ddala ku nsi tekuli muntu mutuukirivu, atakola bibi.
Palibe munthu wolungama pa dziko lapansi amene amachita zabwino zokhazokha ndipo sachimwa.
21 Towulirizanga buli kigambo, bantu kye boogera, si kulwa ng’owulira omuweereza wo ng’akukolimira,
Usamamvetsere mawu onse amene anthu amayankhula, mwina udzamva wantchito wako akukutukwana,
22 kubanga naawe okimanyidde ddala mu mutima gwo, ng’emirundi mingi okolimidde abalala.
pakuti iwe ukudziwa mu mtima mwako kuti nthawi zambiri iwenso unatukwanapo ena.
23 Ebyo byonna nabyekenneenya n’amagezi ne ŋŋamba nti, “Mmaliridde okuba omugezi,” wabula kino kyandi wala.
Zonsezi ndinaziyesa ndi nzeru zanga ndipo ndinati, “Ine ndatsimikiza mu mtima mwanga kuti ndikhale wanzeru,” koma nzeruyo inanditalikira.
24 Amagezi ne bwe gaba ga kikula ki, gali wala nnyo era tegalojjeka, kale ani ayinza okugavumbula?
Nzeru zimene zilipo, zili kutali ndipo ndi zozama kwambiri, ndani angathe kuzidziwa?
25 Bwe ntyo ne nkyusa omutima gwange nnoonye okutegeera, nekkanye, era nnoonyereze amagezi ndowooze ne ku bintu nga bwe biri, n’okutegeera obusirusiru bw’okukola ebibi: n’eddalu ery’obusirusiru.
Kotero ndinayikapo mtima wanga kuti ndidziwe, ndifufuze ndi kumafunafuna nzeru ndi mmene zinthu zimakhalira ndipo ndinafunanso kudziwa kuyipa kwa uchitsiru ndiponso kupusa kwake kwa misala.
26 Ekintu kye nalaba eky’obulabe ekisinga okufa, ye mukazi alina omutima ogusendasenda, era ogusikiriza, era emikono gye gisiba ng’enjegere. Oyo ayagala Katonda, y’awona omukazi oyo, kyokka ye omwonoonyi talema kugwa mu mutego gwe.
Ndinapeza kanthu kowawa kupambana imfa, mkazi amene ali ngati khoka, amene mtima wake uli ngati khwekhwe, ndipo manja ake ali ngati maunyolo. Munthu amene amakondweretsa Mulungu adzathawa mkaziyo, koma mkaziyo adzakola munthu wochimwa.
27 Omubuulizi agamba nti, “Laba, kino kyenvumbudde: “Okugatta ekintu ku kinnaakyo, okuzuula enkola y’ebintu,
Mlaliki akunena kuti, “Taonani, chimene ndinachipeza ndi ichi: “Kuwonjezera chinthu china pa china kuti ndidziwe mmene zinthu zimachitikira,
28 bwe nnali nga nkyanoonyereza nabulako kye nzuula, okuggyako okulaba omusajja omwesimbu omu mu basajja lukumi, kyokka mu bakazi bonna ssaalabamu n’omu atuukiridde.
pamene ine ndinali kufufuzabe koma osapeza kanthu, ndinapeza munthu mmodzi wolungama pakati pa anthu 1,000, koma pakati pawo panalibepo mkazi mmodzi wolungama.
29 Wabula kino kyokka kye nalaba: Katonda yatonda omuntu nga mugolokofu, naye abantu ne beenoonyeza ebintu ebirala bingi.”
Chokhacho chimene ndinachipeza ndi ichi: Mulungu analenga munthu, anamupatsa mtima wolungama, koma anthu anatsatira njira zawozawo zambirimbiri.”