< Banzembo 21 >

1 Wuta na buku ya mokambi ya bayembi. Nzembo ya Davidi. Yawe, mokonzi azali kosepela na nguya na Yo; Tala ndenge nini elonga oyo opesi ye epesi ye esengo monene!
Kwa mtsogoleri wa mayimbidwe. Salimo la Davide. Inu Yehova, mfumu ikusangalala mu mphamvu yanu, chimwemwe chake nʼchachikuludi pa kupambana kumene mumapereka!
2 Okokisi posa ya motema na ye mpe opimeli ye te oyo azalaki kosenga Yo.
Inu mwayipatsa zokhumba za mtima wake ndipo simunayimane zopempha za pa milomo yake. (Sela)
3 Oyei epai na ye na mapamboli ya motuya. Na moto na ye, olatisi ye motole ya wolo oyo basangisa na eloko mosusu.
Inu munayilandira ndi madalitso ochuluka ndipo munayiveka chipewa chaufumu chagolide weniweni pa mutu wake.
4 Asengaki Yo bomoi, mpe opesaki ye yango; opesaki ye bomoi molayi mpe ya libela na libela.
Iye anakupemphani moyo, ndipo munamupatsa masiku ochuluka kwamuyaya.
5 Nkembo na ye ezali monene mpo na lobiko oyo opesaki ye; olatisaki ye na kongenga mpe na lokumu.
Kudzera mʼzigonjetso zimene munapereka, ulemerero wake ndi waukulu; Inu mwapereka pa iyo ulemerero ndi ufumu.
6 Solo, okomisi ye etima ya mapamboli ya seko na seko; okomisaki ye moto ya esengo na miso na Yo.
Zoonadi Inu mwayipatsa madalitso amuyaya, Inu mwayipatsa chisangalalo ndi chimwemwe chimene chili pamaso panu.
7 Mokonzi atiaka elikya na Yawe, aninganaka te mpo na bolingo ya Ye-Oyo-Aleki-Likolo.
Pakuti mfumu imadalira Yehova; kudzera mʼchikondi chake chosatha cha Wammwambamwamba, iyo sidzagwedezeka.
8 Loboko na Yo ekokanga banguna na Yo nyonso; loboko na Yo ya mobali ekokanga bayini na Yo.
Dzanja lanu lidzayimitsa adani anu onse; dzanja lanu lamanja lidzagwira adani anu.
9 Tango okomimonisa, okokomisa bango lokola fulu ya moto. Yawe akosilisa koboma bango na kanda na Ye, mpe moto ekozikisa bango.
Pa nthawi ya kuonekera kwanu mudzawasandutsa ngʼanjo yamoto yotentha. Mu ukali wake Yehova adzawameza, ndipo moto wake udzawatha.
10 Okolimwisa mabota na bango na mokili, mpe bakitani na bango, kati na bana ya bato.
Inu mudzawononga ana awo pa dziko lapansi, zidzukulu zawo pakati pa anthu.
11 Atako bakani kosala Yo mabe, atako basali mabongisi ya mabe mpo na kotelemela Yo, bakotikala kolonga ata moke te;
Ngakhale iwo akukonzereni chiwembu mwa kuchenjera kwawo sadzapambana;
12 pamba te okobengana bango tango okobwakela bango bambanzi ya tolotolo na Yo.
pakuti mudzawapirikitsa ndipo adzaonetsa misana yawo pamene mudzawaloza ndi mivi yanu.
13 Yawe, telema na nguya na Yo! Tokoyemba nguya na Yo na nzela ya banzembo.
Mukwezeke Inu Yehova mʼmphamvu yanu, ife tidzayimba nyimbo ndi kutamanda mphamvu yanu.

< Banzembo 21 >