< Banzembo 116 >
1 Nalingaka Yawe, pamba te ayokaka mongongo mpe mabondeli na ngai.
Ndimakonda Yehova pakuti Iyeyo amamva mawu anga; Iye amamva kulira kwanga kopempha chifundo.
2 Ayokaki ngai; boye nakobelela Ye bomoi na ngai mobimba.
Pakuti ananditchera khutu, ndidzayitana Iye masiku onse a moyo wanga.
3 Minyololo ya kufa ezingelaki ngai, somo ya mboka ya bakufi ekangaki ngai; nakomaki moto ya pasi mpe ya mawa. (Sheol )
Zingwe za imfa zinandizinga, zoopsa za ku dziko la anthu akufa zinandigwera; ndinapeza mavuto ndi chisoni. (Sheol )
4 Kasi nabelelaki Kombo ya Yawe: « Yawe, nabondeli Yo, bikisa ngai! »
Pamenepo ndinayitana dzina la Yehova: “Inu Yehova, pulumutseni!”
5 Yawe asalaka ngolu mpe azali sembo, Nzambe na biso ayokelaka bato mawa.
Yehova ndi wokoma mtima ndi wolungama Mulungu wathu ndi wodzaza ndi chifundo.
6 Yawe abatelaka bato oyo bazangi mayele. Nalembaki nzoto, kasi abikisi ngai.
Yehova amateteza munthu wodzichepetsa mtima; pamene ndinali ndi chosowa chachikulu, Iye anandipulumutsa.
7 Molimo na ngai, zongela kimia na yo, pamba te Yawe asaleli yo bolamu.
Pumula iwe moyo wanga, pakuti Yehova wakuchitira zokoma.
8 Solo, okangoli ngai na kufa, okawusi mpinzoli na ngai mpe obateli makolo na ngai ete ekweya te.
Pakuti Inu Yehova mwapulumutsa moyo wanga ku imfa, maso anga ku misozi, mapazi anga kuti angapunthwe,
9 Nakotambola liboso ya Yawe kati na mokili ya bato ya bomoi.
kuti ine ndiyende pamaso pa Yehova mʼdziko la anthu amoyo.
10 Solo, nazalaka na elikya, ezala soki nalobaka: « Nazali moto na pasi makasi. »
Ine ndinakhulupirira; choncho ndinati, “Ndasautsidwa kwambiri.”
11 Kati na mitungisi na ngai, nazalaki komilobela: « Bato nyonso bazali bakosi. »
Ndipo ndili mʼnkhawa yanga ndinati, “Anthu onse ndi abodza.”
12 Nini nakoki kozongisela Yawe mpo na bolamu na Ye nyonso epai na ngai?
Ndingamubwezere chiyani Yehova, chifukwa cha zokoma zake zonse zimene wandichitira?
13 Nakotombola kopo ya elonga mpe nakobelela Kombo ya Yawe.
Ndidzakweza chikho cha chipulumutso ndipo ndidzayitana dzina la Yehova.
14 Nakokokisa bandayi na ngai epai na Yawe na miso ya bato na Ye nyonso.
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse.
15 Kufa ya bayengebene ya Yawe ezali na motuya makasi na miso na Ye.
Imfa ya anthu oyera mtima ndi yamtengowapatali pamaso pa Yehova.
16 Yawe, yoka ngai, nazali mosali na Yo. Nazali mosali na Yo, mwana mobali ya mwasi mosali na Yo. Ofungoli minyololo oyo ekangaki ngai.
Inu Yehova, zoonadi ndine mtumiki wanu: ndine mtumiki wanu, mwana wa mdzakazi wanu; Inu mwamasula maunyolo anga.
17 Nakobonzela Yo mbeka mpo na kozongisa matondi, mpe nakobelela Kombo ya Yawe.
Ndidzapereka nsembe yachiyamiko kwa Inu ndipo ndidzayitanira pa dzina la Yehova.
18 Nakokokisa bandayi na ngai epai na Yawe na miso ya bato na Ye nyonso,
Ndidzakwaniritsa malonjezo anga kwa Yehova pamaso pa anthu ake onse,
19 kati na lopango ya Tempelo ya Yawe; kati na yo, Yelusalemi. Bokumisa Yawe!
mʼmabwalo a nyumba ya Yehova, mʼkati mwako iwe Yerusalemu. Tamandani Yehova.