< Banzembo 101 >

1 Nzembo ya Davidi. Nakoyemba bolingo mpe bosembo; nakoyembela nde Yo, Yawe.
Salimo la Davide. Ndidzayimba za chikondi ndi chiweruzo chanu cholungama; kwa Inu Yehova ndidzayimba matamando.
2 Nakolanda na bokebi nzela ya bato oyo bazangi pamela. Okoya epai na ngai tango nini? Kati na ndako na ngai, nakotambola malamu na motema ezangi pamela.
Ndidzatsata njira yolungama; nanga mudzabwera liti kwa ine? Ndidzayenda mʼnyumba mwanga ndi mtima wosalakwa.
3 Nakotala eloko moko te ya mabe; nayinaka misala ya bato oyo bazangi kondima, ekoki kokangama na ngai te.
Sindidzayika chinthu chilichonse choyipa pamaso panga. Ine ndimadana ndi zochita za anthu opanda chikhulupiriro; iwo sadzadziphatika kwa ine.
4 Mosika na ngai, motema ya kilikili; naboyi kosala mabe.
Anthu a mtima wokhota adzakhala kutali ndi ine; ine sindidzalola choyipa chilichonse kulowa mwa ine.
5 Nakosala ete avanda kimia, moto oyo apanzaka, na nkuku, basango ya lokuta mpo na kobebisa lokumu ya baninga. Nakokoka te kotala moto ya lolendo mpe moto ya lofundu.
Aliyense wosinjirira mnansi wake mseri ameneyo ndidzamuletsa; aliyense amene ali ndi maso amwano ndi mtima wodzikuza, ameneyo sindidzamulekerera.
6 Nakopona nde bato ya sembo kati na mokili mpo ete bavanda pembeni na ngai; moto na etamboli ezanga pamela nde akozala mosali na ngai.
Maso anga adzakhala pa okhulupirika mʼdziko, kuti akhale pamodzi ndi ine; iye amene mayendedwe ake ndi wosalakwa adzanditumikira.
7 Kati na ndako na ngai, mokosi akovanda te; liboso na ngai, mokosi akotelema te.
Aliyense wochita chinyengo sadzakhala mʼnyumba mwanga. Aliyense woyankhula mwachinyengo sadzayima pamaso panga.
8 Tongo nyonso, nakosala ete bato nyonso ya misala mabe kati na mokili bavanda kimia; nakolongola na engumba ya Yawe bato nyonso ya mabe.
Mmawa uliwonse ndidzatontholetsa anthu onse oyipa mʼdziko; ndidzachotsa aliyense wochita zoyipa mu mzinda wa Yehova.

< Banzembo 101 >