< Cakarijas 12 >
1 Tā Kunga vārda spriedums par Israēli. Tā saka Tas Kungs, kas debesis izpletis un zemi dibinājis un radījis cilvēka garu iekš viņa:
Uthenga wa Yehova kwa Israeli. Yehova, amene amayala mlengalenga, amene amayika maziko a dziko lapansi, ndiponso amene amalenga mzimu wokhala mwa munthu, akunena kuti,
2 Redzi, Jeruzālemi Es darīšu par straipalējamo biķeri visām tautām visapkārt, un tas nāks arī pār Jūdu, kad Jeruzālemi apsēdīs.
“Taonani, ndidzasandutsa Yerusalemu kukhala chakumwa choledzeretsa chimene chidzasokoneza mitundu yonse ya anthu yomuzungulira. Yuda adzazingidwa pamodzinso ndi Yerusalemu.
3 Un notiks tai dienā, Es Jeruzālemi darīšu par nastas akmeni visām tautām; visi, kas viņu grib uzcelt, tie ievainosies, un visas pasaules tautas pret viņu sapulcēsies.
Pa tsiku limenelo, pamene mitundu yonse ya anthu a dziko lapansi idzasonkhana kulimbana naye, ndidzasandutsa Yerusalemu thanthwe losatheka kusunthidwa ndi mitundu yonse ya anthu. Onse oyesa kumusuntha adzadzipweteka.
4 Tai dienā, saka Tas Kungs, Es visus zirgus sitīšu ar bailību un viņu jātniekus ar bezprātību, bet pār Jūda namu Es atvēršu savas acis un tautām sitīšu visus zirgus ar aklību.
Pa tsiku limenelo kavalo aliyense ndidzamuchititsa mantha kuti asokonezeke, ndipo wokwerapo wake ndidzamuchititsa misala,” akutero Yehova. “Ndidzayangʼanira nyumba ya Yuda koma ndidzachititsa khungu akavalo onse a anthu a mitundu ina.
5 Tad Jūda virsnieki savā sirdī sacīs: stiprums man ir Jeruzālemes iedzīvotāji iekš Tā Kunga Cebaot, sava Dieva.
Pamenepo atsogoleri a Yuda adzayankhula mʼmitima mwawo kuti, ‘Anthu a ku Yerusalemu ndi amphamvu, chifukwa Yehova Wamphamvuzonse ndiye Mulungu wawo.’
6 Tai dienā Es Jūda virsniekus celšu kā degošu ugunskuru malkā un kā degošu lāpu kūlīšos, un pa labo un kreiso pusi tie aprīs visas tautas visapkārt, un Jeruzāleme vēl paliks savā vietā Jeruzālemē.
“Pa tsiku limenelo ndidzasandutsa atsogoleri a Yuda kukhala ngati mbawula yotentha pakati pa nkhuni, ngati sakali yoyaka pa mitolo ya tirigu. Adzatentha mitundu yonse ya anthu yowazungulira, kumanja ndi kumanzere, koma Yerusalemu sadzasuntha pa malo ake.
7 Un Tas Kungs papriekš izpestīs Jūda dzīvokļus, lai Dāvida nama augstība un Jeruzālemes iedzīvotāju godība nelielās pret Jūdu.
“Yehova adzapulumutsa malo okhala Yuda poyamba, kuti ulemu wa nyumba ya Davide ndi wa anthu okhala mu Yerusalemu usapambane ulemu wa Yuda.
8 Tai dienā Tas Kungs pasargās Jeruzālemes iedzīvotājus, un pats nespēcīgākais viņu starpā tai dienā būs kā Dāvids, un Dāvida nams būs kā Dievs, kā Tā Kunga eņģelis viņu priekšā.
Pa tsiku limenelo Yehova adzatchinjiriza onse okhala mu Yerusalemu, kotero kuti anthu ofowoka kwambiri pakati pawo adzakhala ngati Davide, ndipo nyumba ya Davide idzakhala ngati Mulungu, ngati mngelo wa Yehova wowatsogolera.
9 Un tai dienā Es meklēšu izdeldēt pagānus, kas ceļas pret Jeruzālemi.
Pa tsiku limenelo ndidzawononga mitundu yonse yofuna kuthira nkhondo Yerusalemu.
10 Bet pār Dāvida namu un pār Jeruzālemes iedzīvotājiem Es izliešu žēlastības un lūgšanas garu. Un tie uz Mani raudzīsies, ko tie ir cauri dūruši. Un par Viņu tie žēlosies, kā žēlojās par vienīgo, un tie gauži par Viņu vaimanās, ka vaimanā par pirmdzimto.
“Ndipo pa nyumba ya Davide ndi pa anthu okhala mu Yerusalemu ndidzakhuthulirapo mzimu wachisomo ndi wopemphera. Iwo adzandiyangʼana Ine, amene anamubaya, ndipo adzamulirira kwambiri monga momwe munthu amalirira mwana wake mmodzi yekhayo, ndiponso adzamva chisoni kwambiri monga momwe amachitira ndi mwana woyamba kubadwa.
11 Tai dienā Jeruzālemē būs lielas raudas, kā raudāja pie HadadRimona Meģidus lejā.
Pa tsiku limenelo mudzakhala kulira kwakukulu mu Yerusalemu, monga kulira kwa ku Hadadi-Rimoni ku chigwa cha Megido.
12 Un zeme žēlosies, ikviena cilts par sevi, Dāvida nama cilts sevišķi un viņu sievas sevišķi, un Nātana nama cilts sevišķi un viņu sievas sevišķi, Levja nama cilts sevišķi un viņu sievas sevišķi.
Dziko lidzalira kwambiri, fuko lililonse pa lokha, akazi awo pa okhanso: fuko la Davide pamodzi ndi akazi awo, fuko la Natani pamodzi ndi akazi awo,
13 Šimejus cilts sevišķi un viņu sievas sevišķi, -
nyumba ya Levi pamodzi ndi akazi awo, fuko la Simei pamodzi ndi akazi awo,
14 Visas citas ciltis, ikviena par sevi, un viņu sievas par sevi.
ndiponso mafuko onse pamodzi ndi akazi awo.