< Psalmi 1 >

1 Svētīgs tas cilvēks, kas nestaigā bezdievīgo runās, nedz stāv uz grēcinieku ceļa, nedz sēž mēdītāju biedrībā;
Wodala munthu amene satsatira uphungu wa anthu ochimwa, kapena kuyima mʼnjira ya anthu oyipa, kapena kukhala mʼmagulu a anthu onyoza.
2 Bet kam labs prāts pie Tā Kunga bauslības, un kas Viņa bauslību pārdomā dienās, naktīs.
Koma chikondwerero chake chili mʼmalamulo a Yehova ndipo mʼmalamulo akewo amalingaliramo usana ndi usiku.
3 Jo tas ir kā koks stādīts pie ūdens upēm, kas savus augļus nes savā laikā, un viņa lapas nesavīst, un viss, ko viņš dara, tas labi izdodas.
Iye ali ngati mtengo wodzalidwa mʼmbali mwa mitsinje ya madzi, umene umabereka zipatso zake pa nyengo yake ndipo masamba ake safota. Chilichonse chimene amachita amapindula nacho.
4 Tā nav bezdievīgiem, bet tie ir kā pelus, ko vējš izputina.
Sizitero ndi anthu oyipa! Iwo ali ngati mungu umene umawuluzidwa ndi mphepo.
5 Tāpēc bezdievīgie nepastāvēs sodā, nedz grēcinieki taisno draudzē.
Kotero anthu oyipa sadzatha kuyima pa chiweruzo, kapena anthu ochimwa mu msonkhano wa anthu olungama.
6 Jo Tas Kungs pazīst taisno ceļu, bet bezdievīgo ceļš ies bojā.
Pakuti Yehova amayangʼanira mayendedwe a anthu olungama, koma mayendedwe a anthu oyipa adzawonongeka.

< Psalmi 1 >