< Psalmi 17 >
1 Dāvida lūgšana. Kungs, ņem vērā taisnību, klausies uz manu brēkšanu, griez savas ausis uz manu lūgšanu, kas nenāk no viltīgām lūpām.
Pemphero la Davide. Imvani Inu Yehova pempho langa lachilungamo; mverani kulira kwanga. Tcherani khutu kuti mumve pemphero langa popeza silikuchokera pakamwa pachinyengo.
2 No tava vaiga lai nāk mana tiesa; tavas acis skatās uz to, kas ir taisnība.
Kusalakwa kwanga kuchokera kwa inu; maso anu aone chimene ndi cholungama.
3 Tu pārbaudi manu sirdi, Tu piemeklē to naktīs, Tu mani esi kausējis un nekā neatradis; es esmu apņēmies, ka manai mutei nebūs pārkāpt.
Ngakhale Inu mutafufuza mtima wanga ndi kundisanthula usiku, ngakhale mutandiyesa, simudzapeza kanthu; Ine ndatsimikiza kuti pakamwa panga sipadzachimwa.
4 Pie cilvēku darbiem es sargos caur Tavas mutes vārdu no pārkāpēja pēdām.
Kunena za ntchito za anthu, monga mwa mawu a pakamwa panu, Ine ndadzisunga ndekha posatsata njira zachiwawa.
5 Uzturi manu gājienu uz Taviem ceļiem, ka mani soļi nešaubās.
Mayendedwe anga akhazikika pa njira zanu; mapazi anga sanaterereke.
6 Es Tevi piesaucu, jo Tu mani paklausi, ak Dievs! Griez' Savu ausi pie manis, klausi manu valodu.
Ine ndikuyitana Inu, Mulungu wanga, pakuti mudzandiyankha; tcherani khutu lanu kwa ine ndipo mumve pemphero langa.
7 Parādi brīnišķi Savu žēlastību, Tu, kas glābi no pretiniekiem tos, kas tvērās pie Tavas labās rokas.
Onetsani kudabwitsa kwa chikondi chanu chachikulu, Inu amene mumapulumutsa ndi dzanja lanu lamanja iwo amene amathawira kwa inu kuchoka kwa adani awo.
8 Pasargi mani kā acs raugu acī, apslēp mani savu spārnu pavēnī
Mundisunge ine ngati mwanadiso; mundibise mu mthunzi wa mapiko anu,
9 No bezdievīgo vaiga, kas mani posta, no maniem nikniem ienaidniekiem, kas ap mani apmetās.
kuchoka kwa oyipa amene amandizinga ine, kuchoka kwa anthu amene ndi adani anga, amene andizungulira ine.
10 Savu cieto sirdi tie aizslēguši, ar savu muti tie runā lepni.
Iwo amatseka mitima yawo yopanda chifundo, ndi pakamwa pawo amayankhula modzitamandira.
11 Tie nu ir visapkārt ap mums mūsu ceļos, ar savām acīm tie glūn, mūs gāzt pie zemes.
Andisaka, tsopano andizungulira ndi maso awo atcheru, kuti andigwetse pansi.
12 Viņa ģīmis ir kā lauva, kas tīko saplosīt, un kā jauns lauva, kas sēž paslēpies.
Iwo ali ngati mkango wofuna nyama; ngati mkango waukulu wokhala mobisala.
13 Celies, Kungs, steidzies viņam pretī, nogāz viņu, izglāb ar Savu zobenu manu dvēseli no bezdievīgā,
Dzukani Yehova, mulimbane nawo ndipo muwagwetse pansi; landitseni kuchoka kwa oyipa ndi lupanga lanu.
14 No tiem ļaudīm ar Savu roku, ak Kungs! no šās pasaules ļaudīm, kam sava tiesa ir šai dzīvībā, kam vēderu Tu pildi ar Savu mantu, kam dēlu papilnam, un kas savu mantu atstāj saviem bērniem.
Inu Yehova, pulumutseni ndi dzanja lanu kwa anthu otere, kwa anthu a dziko lino amene mphotho yawo ili mʼmoyo uno. Inu mumaletsa njala kwa amene asangalatsidwa nanu; ana awo aamuna ali ndi zinthu zambiri, ndipo iwo amasunga chuma cha ana awo.
15 Bet es skatīšu Tavu vaigu iekš taisnības, uzmodies mielošos no Tava ģīmja.
Ndipo ine mʼchilungamo ndidzaona nkhope yanu; pamene ndidzadzuka, ndidzakondwera kwambiri poonana nanu.