< Salamana Pamācības 8 >

1 Vai gudrība nesauc, un atzīšana nepaceļ savu balsi?
Kodi nzeru sikuyitana? Kodi nzeru yomvetsa zinthu sinakweze mawu ake?
2 Kalnu virsgalā tā stāv, ceļmalā uz ceļu jūtīm;
Nzeru imayima pa zitunda mʼmbali mwa njira, imayima pa mphambano ya misewu.
3 Pie vārtiem pilsētas priekšā, kur pa vārtiem ieiet, viņa skaņi sauc:
Imafuwula pafupi ndi zipata zolowera mu mzinda, pa makomo olowera imafuwula kuti,
4 „Uz jums, vīri, es saucu, un mana balss iet pie cilvēku bērniem.
Inu anthu, ndikuyitana inu; ndikuyitanatu anthu onse.
5 Ņemiet vērā, nejēgas, gudrību, un, ģeķi, paliekat prātīgi!
Inu amene simudziwa kanthunu khalani ochenjera; inu amene ndi opusa, khalani ndi mtima womvetsa zinthu.
6 Klausāties, jo es runāšu augstas lietas un atdarīšu savu muti ar skaidriem vārdiem.
Mverani, pakuti ndikukuwuzani zinthu zofunika kwambiri; ndatsekula pakamwa panga ndipo payankhula zolungama.
7 Jo mana mute runās patiesību, un bezdievība manām lūpām ir negantība.
Pakamwa panga pamayankhula zoona ndimanyansidwa ndi kuyankhula zoyipa.
8 Visi manas mutes vārdi stāv taisnībā, iekš tiem nav netiklības, nedz viltības.
Mawu onse a pakamwa panga ndi olungama; mʼmawu angawo mulibe zokhotakhota kapena zopotoka.
9 Tie ir visnotaļ taisni tam, kas tos saprot un skaidri tiem, kas atzīšanu atraduši.
Kwa anthu ozindikira, mawu anga onse ndi woona; kwa anthu amene ali ndi nzeru zomvetsa zinthu, mawu angawo ndi okhoza.
10 Pieņemiet manu mācību labāki nekā sudrabu, un atzīšanu vairāk nekā tīru zeltu;
Landirani malangizo anga mʼmalo mwa siliva, nzeru zomvetsa zinthu mʼmalo mwa golide wabwino.
11 Jo gudrība ir labāka pār pērlēm, un viss, ko tu kārotu, tai netiek līdz.
Paja nzeru ndi yabwino kwambiri kuposa miyala yamtengowapatali, ndipo zonse zimene ungazifune sizingafanane ndi nzeru.
12 Es, tā gudrība, mītu pie samaņas un atrodu vērtīgu padomu.
Ine nzeru, ndimakhala pamodzi ndi kuchenjera. Ine ndimadziwa zinthu ndiponso ndimalingalira zinthu bwino.
13 Tā Kunga bijāšana ir: ienīdēt ļaunu, lepnību, augstprātību un ļaunu ceļu, un es ienīstu netiklu muti.
Kuopa Yehova ndiko kudana ndi zoyipa. Ine ndimadana ndi kunyada, kudzitama, kuchita zoyipa, ndiponso kuyankhula zonyenga.
14 Pie manis ir padoms un palīgs; es esmu atzīšana, man ir spēks.
Ndine mwini uphungu ndi maganizo abwino; ndili ndi nzeru yomvetsa zinthu ndiponso mphamvu.
15 Caur mani valda ķēniņi, un dod taisnus likumus valdītāji;
Ndine amene ndimathandiza mafumu kulamulira. Ndimawathandiza olamulira kukhazikitsa malamulo olungama.
16 Caur mani valda varenie un lielkungi, visi zemes soģi.
Ndine amene ndimathandiza akalonga polamula. Ndinenso amene ndimathandiza akuluakulu onse kulamulira bwino dziko.
17 Es mīlēju tos, kas mani mīl, un kas mani tikuši(centīgi) meklē, tie mani atrod.
Ndimakonda amene amandikonda, ndipo amene amandifunafuna amandipeza.
18 Bagātība un gods ir pie manis, paliekama manta un taisnība.
Ine ndili ndi chuma ndi ulemu, chuma ndi kupindula pa ntchito kokhazikika.
19 Mani augļi ir labāki nekā zelts un tīrs zelts, un mans ienākums nekā šķīsts sudrabs.
Chipatso changa ndi chabwino kuposa golide, ngakhale golide wosalala; zimene ine ndimabereka zimaposa siliva wabwino kwambiri.
20 Es vadu uz taisnības ceļa, taisnas tiesas pēdās,
Ndimachita zinthu zolungama. Ine sindipatuka mʼnjira za chilungamo.
21 Ka tiem, kas mani mīl, dodu iemantot pilnību un pildu viņu mantu.
Ndimapereka chuma kwa amene amandikonda ndi kudzaza nyumba zawo zosungiramo chuma.
22 Tas Kungs mani nolika par sava ceļa iesākumu, par savu radījumu pirmaju no mūžības.
“Yehova anandilenga ine nzeru monga ntchito yake yoyamba. Mwa ntchito zake zakalekale yoyamba ndinali ine.
23 No mūžības es esmu iecelta, no iesākuma, no pasaules gala.
Ndinapangidwa kalekalelo, pachiyambi penipeni dziko lapansi lisanalengedwe.
24 Kad dziļumi vēl nebija, tad es piedzimu, kad avoti vēl nebija, no ūdeņiem grūti.
Nyanja, akasupe odzaza ndi madzi, zonsezi kulibe pamene ine ndinkabadwa.
25 Pirms kalnu pamati tapa nolikti, priekš pakalniem, tad es piedzimu.
Mapiri asanakhazikitsidwe pa malo awo, mapiri angʼonoangʼono asanakhalepo, ine ndinali nditabadwa kale,
26 Viņš vēl nebija radījis zemi nedz klajumus, nedz sācis pasaules pīšļus;
lisanalengedwe dziko lapansi ndi minda yake; lisanalengedwe dothi loyamba la dziko lapansi.
27 Kad viņš debesis sataisīja, tad es tur biju; kad viņš izplatīja debess velvi pār dziļumiem,
Ine ndinalipo pamene Yehova ankakhazikitsa mlengalenga, pamene ankalemba malire a nyanja yozama,
28 Kad viņš padebešus augšām nostiprināja, kad dziļumu avoti krākdami krāca,
pamene anakhazikitsa mitambo ya mlengalenga ndi kukhazikitsa akasupe a madzi ozama,
29 Kad viņš jūrai lika robežas, ka ūdeņi neplūstu pār viņas malām, kad viņš nostiprināja zemes pamatus:
pamene anayikira nyanja malire kuti madzi asadutse malirewo, ndiponso pamene ankayika malire a dziko lapansi.
30 Tad es biju pie viņa tā izdarītāja un biju viņa prieks dienu dienas un līksmojos viņa priekšā vienmēr:
Tsono ine ndinali pambali pake ngati mmisiri; ndikumukondweretsa tsiku ndi tsiku, kusangalala nthawi zonse pamaso pake.
31 Es līksmojos viņa pasaules virsū un mans prieks ir pie cilvēku bērniem.
Ndinkasangalala ndi dziko lake lonse ndiponso kumakondwera nawo anthu onse.”
32 Tad klausiet nu mani, mani bērni; jo svētīgs, kas manus ceļus sargā.
“Ndiye tsono ana inu, ndimvereni; odala anthu amene amasunga njira zanga.
33 Klausiet pamācīšanai un topiet gudri, un neatmetat viņu.
Mverani malangizo anga kuti mukhale ndi nzeru; musanyozere mawu anga.
34 Svētīgs tas cilvēks, kas mani klausa, kas kavējās pie manām durvīm dienu no dienas, sargāt manu durvju stenderus;
Wodala munthu amene amandimvera, amene amakhala pa khomo panga tsiku ndi tsiku, kudikirira pa chitseko changa.
35 Jo kas mani atrod, tas atrod dzīvību un dabūs žēlastību no Tā Kunga.
Paja aliyense amene apeza ine wapeza moyo ndipo Yehova amamukomera mtima.
36 Bet kas pret mani grēko, tas dara varu savai dvēselei; kas mani ienīst, tie visi līdz mīļo nāvi.“
Koma amene alephera kundipeza, amadzipweteka yekha; onse amene amandida amakonda imfa.”

< Salamana Pamācības 8 >