< Salamana Pamācības 4 >
1 Klausāties, mani bērni, tēva pamācīšanu un meklējiet atzīšanu mācīties;
Ananu, mverani malangizo a abambo anu; tcherani khutu kuti mupeze nzeru zodziwira zinthu.
2 Jo es jums dodu labu mācību, neatmetiet manu bauslību!
Zimene ndikukuphunzitsani ndi zabwino. Choncho musasiye malangizo anga.
3 Jo es biju sava tēva dēls, savai mātei luteklītis un vienīgais;
Paja ndinalinso mwana mʼnyumba mwa abambo anga; mwana mmodzi yekha wapamtima pa amayi anga.
4 Un viņš mani mācīja un sacīja: Lai tava sirds pieņem manus vārdus, turi manus baušļus, tad tu dzīvosi;
Ndipo abambo anandiphunzitsa ndi mawu akuti, “Ugwiritse mawu anga pa mtima pako, usunge malamulo anga kuti ukhale ndi moyo.
5 Manto gudrību, manto atzīšanu; neaizmirsti un negriezies nost no manas mutes vārdiem;
Upeze nzeru, upeze nzeru zomvetsa zinthu; usayiwale mawu anga kapena kutayana nawo.
6 Neatstāj to, tad viņa tevi paglābs; mīļo viņu, tad viņa tevi pasargās.
Usasiye nzeru ndipo idzakusunga. Uziyikonda ndipo idzakuteteza.
7 Gudrības iesākums ir: Manto gudrību un ar visu savu padomu samanto atzīšanu.
Fundo yayikulu pa za nzeru ndi iyi: upeze nzeru. Kaya pali china chilichonse chimene ungapeze, koma upeze nzeru yomvetsa bwino zinthu.
8 Turi viņu augsti, tad viņa tevi paaugstinās, viņa tevi cels godā, ja tu viņu apkampsi.
Uyilemekeze nzeruyo ndipo idzakukweza; ikumbatire nzeruyo ndipo idzakupatsa ulemu.
9 Viņa dos jauku glītumu tavai galvai; krāšņu kroni viņa tev dāvinās.
Idzayika sangamutu yokongola yamaluwa pamutu pako; idzakupatsa chipewa chaufumu chaulemu.”
10 Klausies, mans bērns, un pieņem manus vārdus, tad vairosies tavas dzīvības gadi.
Mwana wanga, umvere ndi kuvomereza zimene ndikunena, ndipo zaka za moyo wako zidzakhala zochuluka.
11 Es tev mācīšu gudrības ceļu, es tevi vadīšu uz taisna ceļa,
Ndakuphunzitsa njira yake ya nzeru. Ndakutsogolera mʼnjira zolungama.
12 Ka staigājot tavi soļi nemetās, un tekot tu nepiedauzies.
Pamene ukuyenda, mapazi ako sadzawombana; ukamadzathamanga, sudzapunthwa.
13 Turies cieti pie pamācības, neatstājies no tās, sargi to; jo tā ir tava dzīvība.
Ugwiritse zimene ndikukuphunzitsazi osazitaya ayi. Uwasamale bwino pakuti moyo wako wagona pamenepa.
14 Uz bezdievīgo tekas nenāc un uz ļauno ceļa neej!
Usayende mʼnjira za anthu oyipa kapena kuyenda mʼnjira ya anthu ochimwa.
15 Stājies no tā, nestaigā uz viņa; raujies no tā un ej garām!
Pewa njira zawo, usayende mʼmenemo; uzilambalala nʼkumangopita.
16 Jo tie neaiziet gulēt, pirms nav ļauna darījuši, un tiem nenāk miegs, pirms nav kādu zemē gāzuši.
Pakuti iwo sagona mpaka atachita zoyipa; tulo salipeza mpaka atapunthwitsa munthu wina.
17 Jo tie ēd bezdievības maizi un dzer negantības vīnu.
Paja chakudya chawo ndicho kuchita zoyipa basi ndipo chakumwa chawo ndi chiwawa.
18 Bet taisno celiņš ir kā spožs gaišums, kas spīd un spīd, līdz diena aust.
Koma njira ya anthu olungama ili ngati kuwala kwa mʼbandakucha kumene kumanka kuwalirawalira mpaka dzuwa litafika pa mutu.
19 Bezdievīgo ceļš ir kā akla tumsība; tie nezin, pār ko tie kritīs.
Koma njira ya anthu oyipa ili ngati mdima wandiweyani; iwo sadziwa chomwe chimawapunthwitsa.
20 Ņem vērā, mans dēls, manus vārdus, griez savu ausi uz manu valodu,
Mwana wanga, mvetsetsa zimene ndikunena; tchera khutu ku mawu anga.
21 Lai tie nezūd no tavām acīm; paglabā tos savā sirds dziļumā;
Usayiwale malangizo angawa, koma uwasunge mu mtima mwako.
22 Jo tie ir dzīvība tiem, kas tos atrod, un visai viņu miesai zāles, kas dziedina.
Pakuti amapatsa moyo kwa aliyense amene awapeza ndipo amachiritsa thupi lake lonse.
23 Pār visu, kas jāsargā, sargi savu sirdi; jo no tās iziet dzīvība.
Ndipotu mtima wako uziwuyangʼanira bwino ndithu pakuti ndiwo magwero a moyo.
24 Atstādini no sevis netiklu muti, un netaisnas lūpas lai ir tālu no tevis.
Usiyiretu kuyankhula zokhotakhota; ndipo ulekeretu kuyankhula zinthu zonyansa.
25 Lai tavas acis taisni skatās, un tavi acu raugi taisni tavā priekšā.
Maso ako ayangʼane patsogolo; uziyangʼana kutsogolo molunjika.
26 Nosver savu kāju soļus, tad visi tavi ceļi labi izdosies.
Uzilingalira bwino kumene kupita mapazi ako ndipo njira zako zonse zidzakhala zosakayikitsa.
27 Negriezies ne uz labo ne kreiso pusi; sargi savu kāju no ļauna.
Usapatukire kumanja kapena kumanzere; usapite kumene kuli zoyipa.