< Salamana Pamācības 25 >

1 Šie arīdzan ir Salamana sakāmie vārdi, ko Hizkijas, Jūda ķēniņa, vīri ir sakrājuši.
Iyi ndi miyambo inanso ya Solomoni, imene anthu a Hezekiya mfumu ya ku Yuda analemba.
2 Dieva gods ir, kādu lietu apslēpt, bet ķēniņu gods ir, kādu lietu izdibināt.
Ulemerero wa Mulungu uli pa kubisa zinthu; ulemerero wa mafumu uli pa kufufuza zinthuzo.
3 Debess ir augsta, un zeme dziļa, un ķēniņu sirds neizdibinājama.
Monga momwe kwatalikira kumwamba ndi momwe kulili kuzama kwa dziko lapansi, ndi momwemonso alili maganizo a mfumu kusadziwika kwake.
4 Atšķir sārņus no sudraba, tad tiek kausētājam trauks;
Chotsa zoyipa mʼsiliva ndipo wosula adzapanga naye ziwiya.
5 Atšķir bezdievīgo nost no ķēniņa, tad viņa goda krēsls ar taisnību top stiprināts.
Chotsa munthu woyipa pamaso pa mfumu; ndipo ufumu wake udzakhazikika mu chilungamo.
6 Nelielies ķēniņa priekšā un nestājies lielu kungu vietā.
Usamadzikuze ukakhala pamaso pa mfumu, ndipo usamakhale pamalo pa anthu apamwamba;
7 Jo tas ir labāki, ka tev saka: „Virzies augšup!“nekā ka tevi pazemo vareno priekšā, ko tavas acis redz.
paja ndi bwino kuti mfumu ichite kukuwuza kuti, “Bwera pamwamba pano,” kulekana ndi kuti ikuchititse manyazi chifukwa cha wina wokuposa. Chimene wachiona ndi maso ako,
8 Nepārsteidzies strīdēties; jo citādi, ko tu galā darīsi, kad tavs tuvākais tevi gānījis.
usafulumire kupita nacho ku bwalo la milandu nanga udzachita chiyani pa mapeto pake ngati mnansi wako adzakuchititsa manyazi?
9 Izšķir pats savas ķildas ar savu tuvāko un neatklāj cita noslēpumu,
Kamba mlandu ndi mnansi wako, koma osawulula chinsinsi cha munthu wina
10 Ka tevi nerāj, kas to dzird, un tavam kaunam nav gala.
kuopa kuti wina akamva mawu ako adzakuchititsa manyazi ndipo mbiri yako yoyipa sidzatha.
11 Vārds īstenā laikā runāts ir zelta āboli sudraba traukos.
Mawu amodzi woyankhulidwa moyenera ali ngati zokongoletsera zagolide mʼzotengera zasiliva.
12 Gudrs pamācītājs paklausīgām ausīm ir zelta gredzens un zelta ķēdes.
Kwa munthu womvetsa bwino, kudzudzula kwa munthu wanzeru kuli ngati ndolo zagolide kapena chodzikongoletsera china cha golide wabwino kwambiri.
13 Kā sniega dzestrums pļaujamā laikā, tāds ir uzticams kalps tam, kas to sūta; jo tas atspirdzina sava kunga dvēseli.
Wamthenga wodalirika ali ngati madzi ozizira pa nthawi yokolola kwa anthu amene amutuma; iye amaziziritsa mtima bwana wake.
14 Kas ar dāvanām lielās melodams, ir kā mākoņi un vējš bez lietus.
Munthu wonyadira mphatso imene sayipereka ali ngati mitambo ndi mphepo yopanda mvula.
15 Ar lēnu garu pierunā valdnieku un ar mīkstu mēli lauž kaulus.
Kupirira ndiye kumagonjetsa mfumu, ndipo kufewa mʼkamwa kutha kumafatsitsa munthu wowuma mtima.
16 Medu atradis, ēd savu tiesu, ka tu pārēdies to neizvem.
Ngati upeza uchi, ingodya okukwanira, kuopa ungakoledwe nawo ndi kuyamba kusanza.
17 Reti vien cel savu kāju tuvākā namā, ka viņš tevis neapnīkst un tevis neienīst.
Uzipita kamodzikamodzi ku nyumba ya mnzako ukawirikiza kupita, udzadana naye.
18 Kas pret savu tuvāko dod nepatiesu liecību, ir kā veseris un zobens un asa bulta.
Munthu wochitira mnzake umboni wonama, ali ngati chibonga kapena lupanga kapena muvi wakuthwa.
19 Uz neuzticamu paļauties bēdu dienā ir izlūzis zobs un kliba kāja.
Kudalira munthu wosankhulupirika pa nthawi ya mavuto, kuli ngati dzino lobowoka kapena phazi lolumala.
20 Kas noskumušai sirdij dziesmas dzied, ir kā kad drēbes novelk ziemas laikā un kā etiķis uz sāls.
Kuyimbira nyimbo munthu wachisoni kuli ngati kuvula zovala pa nyengo yozizira kapena kuthira mchere pa chilonda.
21 Kad tavs ienaidnieks izsalcis, ēdini viņu ar maizi, un kad izslāpis, dzirdini viņu ar ūdeni;
Ngati mdani wako ali ndi njala, mupatse chakudya kuti adye; ngati ali ndi ludzu mupatse madzi kuti amwe.
22 Jo tā tu sakrāsi kvēlošas ogles uz viņa galvas, un Tas Kungs tev to atmaksās.
Pochita izi, udzamusenzetsa makala a moto pa mutu pake, ndipo Yehova adzakupatsa mphotho.
23 Ziemelis dzemdē lietu, un glūnētāja mēle skābu ģīmi.
Monga momwe mphepo yampoto imabweretsera mvula, chonchonso mjedu umadzetsa mkwiyo.
24 Nama augšā kaktiņā dzīvot ir labāki, nekā namā kopā ar rējēju sievu.
Nʼkwabwino kukhala pa ngodya ya denga kuposa kukhala mʼnyumba ndi mkazi wolongolola.
25 Laba ziņa no tālas zemes ir dzestrs ūdens izslāpušai dvēselei.
Mthenga wabwino wochokera ku dziko lakutali ali ngati madzi ozizira kwa munthu waludzu.
26 Taisnais, kas bezdievīga priekšā lokās, ir sajukusi aka un sajaukts avots.
Munthu wolungama amene amagonjera munthu woyipa ali ngati kasupe wodzaza ndi matope kapena chitsime cha madzi oyipa.
27 Daudz medus ēst nav labi, un savu paša godu meklēt nav gods.
Sibwino kudya uchi wambiri, sibwinonso kudzifunira wekha ulemu.
28 Kas prātu nemāk valdīt, ir izlauzta pilsēta bez mūriem.
Munthu amene samatha kudziretsa ali ngati mzinda umene adani awuthyola ndi kuwusiya wopanda malinga.

< Salamana Pamācības 25 >