< Salamana Pamācības 22 >

1 Laba slava der vairāk, nekā liela bagātība; mīlestība pie ļaudīm labāka, nekā sudrabs un zelts.
Mbiri yabwino ndi yofunika kuposa chuma chambiri; kupeza kuyanja nʼkwabwino kuposa siliva kapena golide.
2 Bagāts sastopas ar nabagu; Tas Kungs viņus visus radījis.
Wolemera ndi wosauka ndi ofanana; onsewa anawalenga ndi Yehova.
3 Gudrais paredz nelaimi un paglābjas; bet neprāta ļaudis skrien vien un dabū ciest.
Munthu wochenjera akaona choopsa amabisala, koma munthu wopusa amangopitirira ndipo amadzanongʼoneza bondo.
4 Pazemības, proti Dieva bijības alga ir bagātība un gods un dzīvība.
Mphotho ya munthu wodzichepetsa ndi woopa Yehova ndi chuma, ulemu ndi moyo.
5 Ērkšķi un valgi ir netiklam ceļā; kas savu dvēseli sargā, paliks tālu no tiem.
Mʼnjira za anthu oyipa muli minga ndi misampha, koma amene amasala moyo wake adzazipewa zonsezo.
6 Māci bērnam viņa ceļu, tad viņš, arī vecs palicis, no tā neatkāpsies.
Mwana muzimuphunzitsa njira yake, ndipo akadzakalamba sadzachokamo.
7 Bagātais valda pār nabagiem, un kas aizņēmās, ir aizdevēja kalps.
Wolemera amalamulira wosauka, ndipo wokongola zinthu amakhala kapolo wa womukongozayo.
8 Kas netaisnību sēj, tas bēdas pļaus un ies bojā caur savas blēdības rīksti.
Amene amafesa zoyipa amakolola mavuto, ndipo ndodo yaukali wake idzathyoka.
9 Žēlīga acs taps svētīta; jo viņa no savas maizes dod nabagam.
Amene ali ndi diso lachifundo adzadalitsika, pakuti iye amagawana chakudya chake ndi anthu osauka.
10 Izdzen garzobi, tad aizies ķilda, un riešana mitēsies un kauns.
Chotsani munthu wonyoza, ndipo kukangana kudzatha; mapokoso ndi zonyoza zidzaleka.
11 Kam šķīsta sirds un mute mīlīga, tam ķēniņš ir par draugu.
Amene amakonda kukhala woyera mtima ndi kumayankhula mawu abwino, adzakhala bwenzi la mfumu.
12 Tā Kunga acis pasargā, kam atzīšana; bet nelieša vārdus viņš izdeldē.
Maso a Yehova amakhala pa anthu odziwa bwino zinthu, koma Iye adzalepheretsa mawu a anthu osakhulupirika.
13 Slinkais saka: „Lauva ir ārā; ielas vidū mani saplosīs!“
Munthu waulesi amati, “Kunjaku kuli mkango. Ine ndidzaphedwa mʼmisewu!”
14 Maukas mute ir dziļa bedre; ko Tas Kungs ienīst, tas krīt tur iekšā.
Pakamwa pa mkazi wachigololo pali ngati dzenje lozama; amene Yehova wamukwiyira adzagwamo.
15 Blēņas līp bērna sirdī; bet pārmācības rīkste tās izdzen tālu.
Uchitsiru umakhala mu mtima mwa mwana, koma ndodo yomulangira mwanayo idzachotsa uchitsiruwo.
16 Kas no nabaga plēš, savu mantu vairot, tas to atkal dos bagātam līdz pat trūcībai.
Amene amapondereza anthu osauka kuti awonjezere chuma chake, ndiponso amene amapereka mphatso kwa anthu olemera onsewa adzasauka.
17 Griez savu ausi un klausies gudro vārdu un loki savu sirdi pie manas atzīšanas.
Utchere khutu lako ndipo umvere mawu anzeru; uyike mtima wako pa zimene ndikukuphunzitsa kuti udziwe.
18 Jo tas būs jaukums, ja tu tos sirdī pasargāsi un tos visnotaļ stādīsi uz savām lūpām.
Zidzakhala zokondweretsa ngati uzisunga mu mtima mwako ndi wokonzeka kuziyankhula.
19 Lai tava cerība stāv uz To Kungu. Šodien es tevi mācu, tiešām tevi!
Ndakuphunzitsa zimenezi lero koma makamaka uziopa Yehova.
20 Vai tev jau sen to neesmu rakstījis ar padomiem un mācībām,
Kodi suja ndinakulembera malangizo makumi atatu okuchenjeza ndi okupatsa nzeru,
21 Ka tev rādītu taisnus un patiesīgus vārdus, atbildēt patiesības vārdus tiem, kas tevi sūta.
malangizo okudziwitsa zolungama ndi zoona ndi kuti ukawayankhe zoona amene akutumawo?
22 Neaplaupi nabagu, tādēļ ka tas nabags, un nenospaidi sērdieni tiesas priekšā;
Mʼmphawi usamubere chifukwa ndi osauka, ndipo usawapondereze anthu osowa mʼbwalo la milandu,
23 Jo Tas Kungs iztiesās viņu tiesu un laupīs dvēseli tiem, kas tos laupa.
pakuti Yehova adzawateteza pa mlandu wawo ndipo adzalanda moyo onse amene amawalanda iwo.
24 Netinies ar bargu, un nesameties ar to, kam ātras dusmas,
Usapalane naye ubwenzi munthu wosachedwa kupsa mtima ndipo usayanjane ndi munthu amene sachedwa kukwiya
25 Ka tu nemācies viņa tekas un nesavaldzini savu dvēseli.
kuopa kuti iwe ungadzaphunzire njira zake ndi kukodwa mu msampha.
26 Neturies pie tiem, kas ar roku apsolās un par parādu galvo;
Usakhale munthu wopereka chikole kapena kukhala mboni pa ngongole;
27 Kad tev nebūs ko maksāt, tad noņems tavu gultu apakš tevis.
ngati ulephera kupeza njira yolipirira adzakulanda ngakhale bedi lako lomwe.
28 Neatcel vecās robežas, ko tavi tēvi likuši.
Usasunthe mwala wamʼmalire akalekale amene anayikidwa ndi makolo ako.
29 Ja tu vīru redzi, kas tikuši(prasmīgi) savu darbu dara, tas stāvēs ķēniņu priekšā, un nestāvēs šādu tādu ļaužu priekšā.
Kodi ukumuona munthu waluso pa ntchito yake? Iye adzatumikira mafumu; sadzatumikira anthu wamba.

< Salamana Pamācības 22 >