< Salamana Pamācības 19 >

1 Nabags savā vientiesībā staigādams ir labāks, nekā ģeķis ar netiklu muti.
Ndi wabwino munthu wosauka amene amayenda mu ungwiro, aposa munthu wopusa woyankhula zokhota.
2 Arī pārsteigšanās bez ziņas nav laba, un ātri skrejot klūp.
Si bwino kuti munthu akhale wopanda nzeru; ndipo munthu woyenda mofulumira amaphonya njira.
3 Ģeķība cilvēkam sajauc ceļus, ka viņa sirds kurn pret To Kungu.
Uchitsiru wa munthu umamubweretsera zovuta, mtima wake umakwiyira Yehova.
4 Manta pieved daudz draugu, bet nabagu draugs atstāj.
Chuma chimachulukitsa abwenzi; koma munthu wosauka bwenzi lake limamuthawa.
5 Nepatiess liecinieks nesodīts nepaliks, un kas melus runā, neizglābsies.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa; ndipo iye amene amanena mabodza sadzapulumuka.
6 Augstam kungam daudz pieglaužas, un ikkatrs ir devīgam vīram draugs.
Anthu ambiri amafuna munthu wopatsa kuti awakomere mtima, ndipo munthu amene amapereka mphatso ndi bwenzi la munthu aliyense.
7 Nabagu ienīst visi viņa brāļi, cik vairāk viņa draugi no viņa atraujas; meklē tos pirmos vārdus, to nav.
Ngati munthu wosauka abale ake omwe amadana naye, nanji abwenzi ake tsono! Iwo adzamuthawa kupita kutali. Amayesa kuwatsatira mowapembedza koma iwo samapezeka konse.
8 Kas gudrību panāk, mīl savu dvēseli; kas ar prātu dzīvo, atrod labumu.
Iye amene amapeza nzeru ndiye kuti amakonda moyo wake. Wosamalitsa kukhala wanzeru, zinthu zimamuyendera bwino.
9 Nepatiess liecinieks nesodīts nepaliks, un kas droši melus runā, aizies postā.
Mboni yonama sidzalephera kulangidwa, ndipo iye amene amanena mabodza adzawonongeka.
10 Ģeķim nepieder kārumā dzīvot, ne vēl kalpam pār kungiem valdīt.
Nʼkosayenera kuti chitsiru chizikhala ndi moyo wamanyado, nanjinso kuti kapolo azilamulira akalonga!
11 Prātīgs cilvēks ir lēns uz dusmām, un viņa rota ir, kaitināšanu aizmirst.
Nzeru zimapangitsa munthu kukhala wosakwiya msanga; ulemerero wake uli posalabadira kuchitiridwa zoyipa.
12 Ķēniņa dusmība ir kā jauna lauvas rūkšana; bet Viņa žēlastība kā rasa uz zāles.
Mkwiyo wa mfumu uli ngati kubangula kwa mkango, koma kukoma mtima kwake kuli ngati mame pa udzu.
13 Ģeķīgs dēls ir tēvam par sirdēstiem, un sievas riešana ir pilēšana bez gala.
Mwana wopusa ndiye tsoka la abambo ake ndipo mkazi wolongolola ndi wotopetsa ngati mvula yamvumbi.
14 Namu un mantu manto no vecākiem, bet prātīgu sievu no Tā Kunga.
Nyumba ndi chuma ndiye cholowa chochokera kwa makolo; koma mkazi wanzeru ndi wochokera kwa Yehova.
15 Slinkums iemidzina miegā, un kūtra dvēsele cietīs badu.
Ulesi umagonetsa tulo tofa nato ndipo munthu wosatakataka amakhala ndi njala.
16 Kas mācību sargā, tas sargā savu dvēseli; kas savu ceļu neņem vērā, tas mirs.
Amene amamvera malangizo amasunga moyo wake, koma amene sasamala malamulo a Yehova adzafa.
17 Kas par nabagu apžēlojās, tas aizdod Tam Kungam, un tas tam atmaksās viņa labdarīšanu.
Amene amakomera mtima osauka amachita ngati wakongoletsa Yehova, ndipo Yehovayo ndiye adzamubwezere.
18 Pārmāci savu dēlu, kamēr vēl cerība, bet nedod savai dvēselei vaļas, viņu nokaut.
Langa mwana wako, chiyembekezo chikanalipo; ngati sutero udzawononga moyo wake.
19 Kam liela sirds, tam jācieš sods; jo gribi novērst, jo iet vairumā.
Munthu waukali woopsa ayenera kulandira chilango; pakuti akamulekelera ndiye zidzayipa kuposa kale.
20 Klausi padomam un pieņem mācību, ka tu pēcgalā palieci gudrs.
Mvera uphungu ndipo landira malangizo; pa mapeto pake udzakhala wanzeru.
21 Cilvēka sirdī ir daudz nodomu, bet Tā Kunga padoms, tas pastāv.
Munthu amakonzekera zambiri mu mtima mwake, koma cholinga cha Yehova ndiye chidzachitike.
22 Cilvēka gods ir labu darīt, un nabags ir labāks, nekā melkulis.
Chimene munthu amafuna ndi chikondi chosatha; nʼkwabwino kukhala wosauka kusiyana ndi kukhala wabodza.
23 Tā Kunga bijāšana ir uz dzīvību; jo tāds būs paēdis un dzīvos, ļauna neaizskarts.
Kuopa Yehova kumabweretsa moyo; wotereyo amakhala mu mtendere; ndiye kuti choyipa sichidzamugwera.
24 Sliņķis slēpj roku azotē, pat pie mutes viņš to neliek.
Munthu waulesi amapisa dzanja lake mʼmbale; koma sangathe kufikitsa dzanja lakelo pakamwa pake.
25 Per garzobi, tad tas nejēga atjēgs, un pamāci prātīgo, tad viņš atzīs, kas der.
Menya munthu wonyoza, ndipo anthu opanda nzeru adzachenjererapo; dzudzula munthu wozindikira zinthu, ndipo iye adzapezapo chidziwitso.
26 Kas tēvu posta un māti izdzen, tas ir bezkaunīgs un negants bērns.
Mwana wochita ndewu ndi abambo ake ndi kuthamangitsa amayi ake, ndi mwana wochititsa manyazi ndi wonyozetsa.
27 Neklausi, mans bērns, mācībai, kas nomaldina no gudrības vārdiem.
Mwana wanga, ukaleka kumvera malangizo, udzapatukana ndi mawu opatsa nzeru.
28 Nelieša liecinieks apsmej tiesu, un bezdievīgo mute ierij netaisnību.
Mboni yopanda pake imanyoza cholungama, ndipo pakamwa pa anthu oyipa pamameza zoyipa.
29 Garzobiem sodība gatava un pēriens ģeķu mugurai.
Chilango chakonzedwa kale kuti chigwere anthu oyipa, ndipo mkwapulo wakonzedwa kale kuti ukwapule misana ya anthu opusa.

< Salamana Pamācības 19 >