< Salamana Pamācības 12 >

1 Kas labprāt panes pārmācīšanu, tas mīļo atzīšanu, bet kas nepanes rājienu, tas paliek muļķis.
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
2 Kas labs, tas Tam Kungam patīkams, bet vīru, kas viltu perē viņš pazudina.
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
3 Cilvēks nepastāvēs, kad ir bezdievīgs, bet taisno sakne netaps kustināta.
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
4 Tikla sieva ir sava vīra kronis, bet netikla ir kā puve viņa kaulos.
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
5 Taisno domas ir tiesa, bet bezdievīgo padomi viltība.
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
6 Bezdievīgo vārdi glūn uz asinīm; bet taisno mute tos izpestī.
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
7 Bezdievīgie top iznīcināti, ka to vairs nav; bet taisno nams pastāvēs.
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
8 Kā kuram saprašana, tā viņam slava; bet par apsmieklu būs, kam netikla sirds.
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
9 Labāks tas zemais, kas sev pašam par kalpu, nekā kas lepojās, un maizes nav.
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
10 Taisnais gādā par sava lopa dzīvību, bet bezdievīgo sirds ir nežēlīga.
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
11 Kas savu zemi kopj, būs maizes paēdis, bet kas niekus triec, tam nav jēgas.
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
12 Bezdievīgais traucās pēc blēžu medījuma; bet taisno sakne nes augļus.
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
13 Ļaunais savaldzinājās savas mutes grēkos; bet taisnais izies no bēdām.
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
14 Pēc savas mutes augļiem ikviens top pieēdināts ar labumu, un cilvēkam top maksāts pēc viņa roku darbiem.
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
15 Ģeķa ceļš ir taisns paša acīs, bet kas padomam klausa, tas ir gudrs.
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
16 Ģeķa apskaišanās tūdaļ top zināma; bet kas slēpj, ka ir apkaunots, tas ir gudrs.
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
17 Kas patiesību runā, tas saka taisnību; bet nepatiess liecinieks teic melus.
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
18 Dažs aplam runājot kā ar zobenu iedur; bet gudro mēle ir zāles, kas dziedina.
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
19 Patiesa mute pastāvēs mūžīgi, bet viltīga mēle tik acumirkli.
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
20 Viltība ir sirdī tiem, kas ļaunu perē; bet kas dod miera padomu, dara prieku.
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
21 Taisnam nekāds ļaunums nenotiks, bet bezdievīgiem ļaunuma uzies papilnam.
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
22 Viltīgas lūpas Tam Kungam ir negantība; bet kas uzticību dara, tas viņam labi patīk.
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
23 Gudrs cilvēks neizteic savu padomu; bet nejēgu sirds izkliedz ģeķību.
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
24 Čakla roka valdīs, bet slinka dos meslus.
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
25 Raizes sirdī nospiež cilvēku, bet labs vārds to iepriecina.
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
26 Taisnais savam tuvākam rāda ceļu, bet bezdievīgo ceļš maldina.
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
27 Sliņķis neceps savu medījumu, bet uzcītīgam cilvēkam ir skaista manta.
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
28 Uz taisnības ceļa ir dzīvība, un uz viņas ceļa tekām nav nāve.
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

< Salamana Pamācības 12 >