< Jāņa Evaņg̒elijs 16 >
1 To Es jums esmu sacījis, lai jūs neņemat apgrēcību.
“Ine ndakuwuzani zonsezi kuti musadzakhumudwe.
2 Tie jūs izslēgs no draudzes; un nāk laiks, ka tas, kas jūs nokaus, domās, ar to Dievam kalpojis.
Iwo adzakuchotsani mʼsunagoge mwawo. Kunena zoona, nthawi ikubwera imene aliyense amene adzakuphani adzaganiza kuti akutumikira Mulungu.
3 Un to tie darīs, tāpēc ka tie nav atzinuši nedz Manu Tēvu nedz Mani.
Iwo adzachita zoterozo chifukwa sanadziwe Atate kapena Inenso.
4 Bet to Es jums esmu sacījis tāpēc, lai, kad tas laiks būs nācis, jūs pieminat, ka Es jums to esmu sacījis. Bet to Es no iesākuma jums neesmu sacījis, tāpēc ka Es biju pie jums.
Ine ndakuwuzani izi kuti nthawi ikadzafika mudzakumbukire kuti Ine ndinakuchenjezani kale. Ine sindinakuwuzeni izi poyamba paja chifukwa ndinali nanu.”
5 Bet nu Es noeju pie Tā, kas Mani sūtījis, un neviens no jums Mani nejautā: kurp Tu ej?
“Tsopano Ine ndikupita kwa Iye amene anandituma koma palibe wina mwa inu akundifunsa kuti, ‘Kodi mukupita kuti?’
6 Bet kad Es to uz jums esmu runājis, tad jūsu sirds ir palikusi pilna noskumšanas.
Muli ndi chisoni kwambiri chifukwa ndakuwuzani zimene.
7 Bet Es jums saku patiesību: tas jums par labu, ka Es noeju; jo, kad Es nenoeju, tad tas Iepriecinātājs nenāks pie jums; bet kad Es noiešu, tad Es To pie jums sūtīšu.
Komatu ndakuwuzani zoona. Ine ndikuti kuli bwino kwa inu kuti ndichoke. Ngati sindichoka, Nkhosweyo sidzabwera kwa inu, koma ngati Ine ndipita, ndidzamutumiza kwa inu.
8 Un kad Tas būs nācis, Tas pārliecinās pasauli par grēku, par taisnību un par sodu;
Iye akabwera, adzatsutsa dziko lapansi za uchimo, zachilungamo ndi zachiweruzo.
9 Par grēku, ka tie netic uz Mani;
Za uchimo, chifukwa anthu sakhulupirira Ine.
10 Par taisnību, ka Es eju pie Tā Tēva, un jūs Mani vairs neredzēsiet;
Za chilungamo, chifukwa Ine ndi kupita kwa Atate, kumene simudzandionanso.
11 Par sodu, ka šīs pasaules kungs ir notiesāts.
Za chiweruzo, chifukwa wolamulira dziko lino lapansi waweruzidwa tsopano.
12 Man vēl daudz jums jāsaka, bet tagad jūs to nevarat panest.
“Ine ndili ndi zambiri zoti ndiyankhule nanu, koma simungathe kuzilandira tsopano.
13 Bet kad Viņš, Tas Patiesības Gars, nāks, Tas jūs vadīs uz visu patiesību; jo Viņš no Sevis paša nerunās, bet ko Tas dzirdēs, to Tas runās un nākošas lietas jums pasludinās.
Koma pamene Iye, Mzimu wachoonadi, abwera, adzakutsogolerani mʼchoonadi chonse. Iye sadzayankhula mwa Iye yekha, adzayankhula zokhazo zimene wamva ndipo Iye adzakuwuzani zimene zikubwera.
14 Tas Mani pagodinās, jo no Manis Viņš ņems un jums to pasludinās.
Iye adzalemekeza Ine chifukwa adzatenga za Ine nadzakudziwitsani.
15 Viss, kas Tam Tēvam ir, tas ir Mans, tāpēc Es esmu sacījis: Viņš ņems no Manis un jums pasludinās.
Zonse za Atate ndi zanga. Ichi nʼchifukwa chake Ine ndanena kuti Mzimu Woyera adzatenga kwa Ine zanga kuti muzidziwe.”
16 Par mazu brīdi, tad jūs Mani vairs neredzēsiet, un atkal par mazu brīdi, tad jūs Mani redzēsiet,” - jo Es eju pie Tā Tēva.
Yesu anapitiriza kuyankhula kuti, “Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso, ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso.”
17 Tad kādi no Viņa mācekļiem sacīja savā starpā: “Kas tas ir, ko Viņš saka: par mazu brīdi, tad jūs Mani neredzēsiet, un atkal par mazu brīdi, tad jūs Mani redzēsiet;” un: “Es eju pie Tā Tēva?”
Ena a ophunzira ake anati kwa wina ndi mnzake, “Kodi Iye akutanthauza chiyani ponena kuti, ‘Mwa kanthawi kochepa, simudzandionanso,’ ndi ‘ndipo patatha nthawi pangʼono mudzandionanso,’ ndiponso ‘chifukwa ndikupita kwa Atate?’”
18 Un tie sacīja: “Kas tas ir, ko Viņš saka: par mazu brīdi? Mēs nezinām, ko Viņš saka!”
Iwo anapitiriza kufunsana kuti, “Kodi akutanthauza chiyani, ‘kanthawi kochepa?’ Ife sitikumvetsetsa chimene Iye akuyankhula.”
19 Tad Jēzus nomanīja, ka tie Tam gribēja jautāt, un uz tiem sacīja: “Par to jūs apjautājaties savā starpā, ka Es esmu sacījis: par mazu brīdi jūs Mani neredzēsiet, un atkal par mazu brīdi jūs Mani redzēsiet?
Yesu anadziwa kuti ankafuna kuti amufunse za zimenezi, choncho anawafunsa kuti, “Kodi mukufunsana wina ndi mnzake chimene Ine ndimatanthauza pamene ndinati, ‘Mwa kanthawi kochepa simudzandionanso,’ ndi ‘patatha nthawi pangʼono mudzandionanso?’
20 Patiesi, patiesi, Es jums saku: jūs raudāsiet un vaidēsiet, un pasaule priecāsies; bet jūs noskumsiet; - tomēr jūsu noskumšana paliks par prieku.
Zoonadi, Ine ndikukuwuzani kuti inu mudzalira ndi kubuma pomwe dziko lapansi lidzakhale likukondwera. Inu mudzamva chisoni, koma chisoni chanu chidzasandulika chimwemwe.
21 Kad sieva dzemdē, tad tā noskumusi, jo viņas stunda nākusi; bet kad tai tas bērns dzimis, tad viņa tās sāpes vairs nepiemin tās līksmības dēļ, ka cilvēks dzimis pasaulē.
Mayi akamabereka mwana amamva ululu chifukwa nthawi yake yafika; koma mwana wake akabadwa amayiwala ululu wake chifukwa cha chimwemwe chake chakuti mwana wabadwa mʼdziko lapansi.
22 Tā arī jūs tagad esat noskumuši, bet Es jūs atkal redzēšu, un jūsu sirds līksmosies, un jūsu prieku neviens no jums neatņems. Un tanī dienā jūs Man nenieka nejautāsiet.
Chimodzimodzinso ndi inu. Tsopano ino ndi nthawi yanu yomva chisoni, koma Ine ndidzakuonaninso ndipo inu mudzasangalala, ndipo palibe amene adzachotsa chimwemwe chanu.
23 Patiesi, patiesi, Es jums saku: ko vien jūs Tam Tēvam lūgsiet Manā Vārdā, to Viņš jums dos.
Tsiku limenelo inu simudzandipemphanso kalikonse. Ine ndikukuwuzani zoona kuti Atate anga adzakupatsani chilichonse chimene mudzapempha mʼdzina langa.
24 Līdz šim jūs neko neesat lūguši Manā Vārdā; lūdziet, tad jūs ņemsiet, lai jūsu līksmība ir pilnīga.
Mpaka tsopano simunapemphe kalikonse mʼdzina langa. Pemphani ndipo mudzalandira, ndipo chimwemwe chanu chidzakhala chathunthu.
25 To Es uz jums esmu runājis caur līdzībām, bet laiks nāk, kad Es ar jums vairs nerunāšu caur līdzībām, bet jums skaidri pasludināšu par To Tēvu.
“Ngakhale ndakhala ndikuyankhula mʼmafanizo, nthawi ikubwera imene Ine sindidzagwiritsanso ntchito mafanizo otere koma ndidzakuwuzani momveka za Atate anga.
26 Tajā dienā jūs lūgsiet Manā Vārdā; un Es jums nesaku, ka Es To Tēvu lūgšu jūsu dēļ.
Tsiku limenelo inu mudzapempha mʼdzina langa. Ine sindikunena kuti ndidzapempha Atate mʼmalo mwanu ayi.
27 Jo pats Tas Tēvs jūs mīl, tāpēc ka jūs Mani mīlējuši un ticējuši, ka Es esmu izgājis no Tā Tēva.
Atate mwini anakukondani chifukwa inu mwandikonda Ine ndipo mwakhulupirira kuti Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate.
28 Es esmu izgājis no Tā Tēva un nācis šinī pasaulē; atkal Es atstāju šo pasauli un eju pie Tā Tēva.”
Ine ndinabwera kuchokera kwa Atate ndi kulowa mʼdziko lapansi. Tsopano ndikulisiya dziko lapansi kubwerera kwa Atate.”
29 Tad Viņa mācekļi uz To sacīja: “Redzi, tagad Tu runā skaidri un nesaki nekādu līdzību
Kenaka ophunzira ake anati, “Tsopano mukuyankhula momveka bwino ndi mopanda mafanizo.
30 Tagad mēs zinām, ka Tu visu zini, un nevienam nevajag Tevi jautāt; tāpēc mēs ticam, ka Tu esi izgājis no Dieva.”
Tsopano ife tikuona kuti Inu mumadziwa zinthu zonse ndi kuti sipafunika wina aliyense kukufunsani. Mwa ichi ife takhulupirira kuti Inu munachokera kwa Mulungu.”
31 Tad Jēzus tiem atbildēja: “Tagad jūs ticat?
Yesu anawafunsa kuti, “Kodi tsopano mwakhulupirira?”
32 Redzi, tas laiks nāk un jau ir nācis, ka jūs izklīdīsiet, ikviens uz savu vietu, un Mani pametīsiet vienu pašu. Un Es neesmu viens, jo Tas Tēvs ir ar Mani.
Koma nthawi ikubwera ndipo yafika, pamene inu mudzabalalitsidwa, aliyense ku nyumba yake. Inu mudzandisiya ndekhandekha. Koma Ine sindili ndekha, pakuti Atate anga ali nane.
33 To Es uz jums esmu runājis, lai jums miers būtu iekš Manis. Pasaulē jums būs bēdas; bet turat drošu prātu, Es pasauli esmu uzvarējis.”
“Ine ndakuwuzani izi kuti mwa Ine mukhale nawo mtendere. Mʼdziko lapansi mudzakhala nawo mavuto. Koma limbikani mtima! Ine ndaligonjetsa dziko lapansi.”