< Jesajas 38 >
1 Tanī laikā Hizkija palika slims uz miršanu, un pravietis Jesaja, Amoca dēls, nāca pie tā un uz to sacīja: Tā saka Tas Kungs: Apkopi savu namu, jo tu mirsi un nepaliksi vesels.
Nthawi imeneyo Mfumu Hezekiya anadwala ndipo anali pafupi kufa. Mneneri Yesaya mwana wa Amozi anapita kukamuona ndipo anati “Yehova akuti: Konza bwino nyumba yako, pakuti ukufa; suchira.”
2 Tad Hizkija savu vaigu pagrieza pret sienu un pielūdza To Kungu un sacīja:
Hezekiya anatembenuka nayangʼana kukhoma, napemphera kwa Yehova kuti,
3 Ak Kungs, piemini jel, ka es Tavā priekšā esmu staigājis patiesībā no visas sirds un darījis, kas Tev patīk. Un Hizkija raudāja gauži.
“Inu Yehova, kumbukirani momwe ndayendera pamaso panu mokhulupirika ndi modzipereka ndipo ndakhala ndikuchita zabwino pamaso panu.” Ndipo Hezekiya analira mosweka mtima.
4 Tad Tā Kunga vārds tā notika uz Jesaju:
Ndipo Yehova analamula Yesaya kuti:
5 Ej un saki Hizkijam: Tā saka Tas Kungs, tava tēva Dāvida Dievs: Es tavu lūgšanu esmu klausījis, Es tavas asaras esmu redzējis. Redzi, Es tavām dienām pielikšu vēl piecpadsmit gadus.
“Pita kwa Hezekiya ndipo ukamuwuze kuti, ‘Yehova, Mulungu wa kholo lake Davide akuti: Ndamva pemphero lako ndipo misozi yako ndayiona; ndidzakuwonjezera zaka 15 pa moyo wako.
6 Un tevi un šo pilsētu es izpestīšu no Asīrijas ķēniņa rokas un pasargāšu šo pilsētu.
Ndipo ndidzakupulumutsa, iwe pamodzi ndi mzindawu mʼdzanja la mfumu ya ku Asiriya, Ine ndidzawuteteza mzindawu.
7 Un šī būs tā zīme no Tā Kunga, ka Tas Kungs šo lietu darīs, ko Viņš runājis:
“‘Ichi ndi chizindikiro cha Yehova kwa iwe kutsimikiza kuti Yehova adzachita zimene walonjeza:
8 Redzi, tai ēnai, kas ar sauli pa tiem kāpieniem pie Ahaza saules stundeņa uz priekšu gājusi, Es likšu iet atpakaļ desmit kāpienus. Un saule gāja atpakaļ desmit kāpienus pa tiem pašiem kāpieniem, kā tā bija gājusi uz priekšu.
Chithunzithunzi chimene dzuwa likuchititsa pa makwerero a Ahazi ndidzachibweza mʼmbuyo makwerero khumi.’” Ndipo chithunzithunzi chinabwerera mʼmbuyo makwerero khumi.
9 Šis ir Hizkijas, Jūda ķēniņa, raksts, kad viņš bija slims bijis un no savas slimības palicis vesels.
Ndakatulo ya Hezekiya mfumu ya ku Yuda imene analemba atadwala ndi kuchira:
10 Es sacīju: Pašās savās labākās dienās man jānokāpj kapa vārtos, mani atliekamie gadi man top atņemti. (Sheol )
Ine ndinaganiza kuti ndidzapita ku dziko la akufa pamene moyo ukukoma. (Sheol )
11 Es sacīju: Es vairs neredzēšu To Kungu, To Kungu tai zemē, kur tie dzīvie, es vairs neieraudzīšu cilvēkus tai vietā, kur tie aizmigušie mājo.
Ndinaganiza kuti, “Sindidzaonanso Yehova, mʼdziko la anthu amoyo, sindidzaonanso mtundu wa anthu kapena kukhala pamodzi ndi amene amakhala pa dziko lapansi lino.
12 Mans nams top noplēsts un aizcelts, kā ganu būdiņa; es savu dzīvību satinu kā audējs (savu audekli). Viņš mani nogriež kā no riestavas. Pirms nakts metās, Tu man dari galu.
Nyumba yanga yasasuka ndipo yachotsedwa. Ngati tenti ya mʼbusa mwapindapinda moyo wanga, ngati munthu wowomba nsalu; kuyambira usana mpaka usiku mwakhala mukundisiya.
13 Es gaidīju līdz rītam, bet kā lauva Viņš salauž visus manus kaulus. Pirms nakts metās, Tu man darīsi galu.
Ndinkalira kupempha chithandizo usiku wonse mpaka mmawa; koma Inu Yehova munaphwanya mafupa anga ngati mkango, ndipo mwakhala mukundisiya.
14 Es kliedzu kā dzērve un bezdelīga, es vaidēju kā balodis, manas acis nogura uz augšu skatoties. Ak Kungs, man ir bail, izpestī mani!
Ndinkalira ngati namzeze kapena chumba, ndinkabuwula ngati nkhunda yodandaula. Maso anga anatopa nʼkuyangʼana mlengalenga. Inu Ambuye, ine ndili mʼmavuto bwerani mudzandithandize!”
15 Ko lai es saku? Kā viņš man solījis, tā viņš ir darījis; klusu es nu staigāšu visu savu mūžu manas dvēseles skumju dēļ.
Koma ine ndinganene chiyani? Yehova wayankhula nane, ndipo Iye ndiye wachita zimenezi. Chifukwa cha kuwawa kwa mtima wanga, ine ndidzayenda modzichepetsa masiku amoyo wanga onse.
16 Ak Kungs! No tā cilvēks atdzīvojās, un iekš tā visa stāv mana gara dzīvība, Tu mani atspirdzināsi un mani atkal darīsi dzīvu.
Ambuye, masiku anga ali mʼmanja mwanu. Mzimu wanga upeza moyo mwa Inu. Munandichiritsa ndi kundikhalitsa ndi moyo.
17 Redzi, rūgtums palicis man par svētību, pats rūgtums, bet Tu manu dvēseli mīlīgi esi apkampis, ka tā nenāktu trūdēšanas bedrē, jo Tu visus manus grēkus esi metis aiz Sevi.
Ndithudi, ine ndinamva zowawa zotere kuti ndikhale ndi moyo; Inu munandisunga kuti ndisapite ku dzenje la chiwonongeko chifukwa mwakhululukira machimo anga onse.
18 Jo elle Tevi neteic, un nāve Tevi neslavē; tie, kas grimst bedrē, necerē uz Tavu patiesību. (Sheol )
Pakuti akumanda sangathe kukutamandani, akufa sangayimbe nyimbo yokutamandani. Iwo amene akutsikira ku dzenje sangakukhulupirireni. (Sheol )
19 Tie dzīvie, tie dzīvie, tie Tevi slavē, kā es šodien; tēvs bērniem dara zināmu Tavu patiesību.
Amoyo, amoyo okha ndiwo amakutamandani, monga mmene ndikuchitira ine lero lino; abambo amawuza ana awo za kukhulupirika kwanu.
20 Tas Kungs ir man par pestīšanu, un mēs dziedāsim savas dziesmas, kamēr dzīvosim Tā Kunga namā.
Yehova watipulumutsa. Tiyeni tiyimbe ndi zoyimbira za zingwe masiku onse a moyo wathu mʼNyumba ya Yehova.
21 Un Jesaja sacīja: Lai ņem vienu vīģu rausi un liek plāksteri uz to trumu, tad viņš paliks vesels.
Yesaya anati, “Anthu atenge mʼbulu wankhunyu ndipo apake pa chithupsacho ndipo Hezekiya adzachira.”
22 Un Hizkija sacīja: Kāda ir tā zīme, ka es noiešu Tā Kunga namā?
Hezekiya nʼkuti atafunsa kuti, “Kodi chizindikiro chako nʼchiyani chotsimikiza kuti ndidzapita ku Nyumba ya Yehova?”