< Jesajas 18 >
1 Ak vai, zeme, kur spārni žvingst, viņpus Kūsa upēm;
Tsoka kwa anthu a ku Kusi. Kumeneko kumamveka mkokomo wa mapiko a dzombe.
2 Tā sūta vēstnešus pār jūru un niedru laivās pār ūdeņiem. Ejat, jūs čaklie vēstneši, pie tautas, kas bijājama tālu tālu, pie tautas, kas pavēlētāja un saminēja, kam upes zemi dala.
Dziko limenelo limatumiza akazembe pa mtsinje wa Nailo, mʼmabwato amabango amene amayandama pa madzi, ndikunena kuti, “Pitani, inu amithenga aliwiro, kwa mtundu wa anthu ataliatali a khungu losalala, ndi woopedwa ndi anthu. Akazembe anatumidwa ku dziko la anthu amphamvu ndi logonjetsa anthu ena. Dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje.”
3 Visi jūs pasaules iedzīvotāji un jūs ļaudis virs zemes, kad karogs taps izcelts kalnos, tad redziet, un kad trumete skanēs, tad dzirdiet!
Inu nonse anthu a pa dziko lonse, inu amene mumakhala pa dziko lapansi, pamene mbendera yakwezedwa pa mapiri yangʼanani, ndipo pamene lipenga lilira mumvere.
4 Jo tā Tas Kungs uz mani sacījis: “Es turēšos klusu un skatīšos no Sava mājokļa, kā karstums spiež saulei spīdot un padebesis raso pļaujama laika karstumā.”
Pakuti Yehova akunena kwa ine kuti, “Ndili chikhalire ku malo anga kuno, ndidzakhala chete, ndi kumangoyangʼana, monga momwe dzuwa limawalira nthawi yotentha, monganso momwe mame amagwera usiku pa nthawi yotentha yokolola.”
5 Jo priekš pašas pļaujas, kad ziedi noziedējuši un kad no ziediem ķekari jau ietekās, tad Viņš stīgas nogriezīs ar dārza nazi un zarus atņems un nokapās.
Pakuti, anthu asanayambe kukolola, maluwa atayoyoka ndiponso mphesa zitayamba kupsa, Iye adzadula mphukira ndi mipeni yosadzira, ndipo adzadula ndi kuchotsa nthambi zotambalala.
6 Tie visi taps atstāti kalnu ērgļiem un zemes zvēriem, un tie ērgļi tur paliek pa vasaru un visi zemes zvēri tur mīt pa ziemu.
Mitembo ya anthu ankhondo adzasiyira mbalame zamʼmapiri zodya nyama ndiponso zirombo zakuthengo; mbalame zidzadya mitemboyo nthawi yonse ya chilimwe, ndipo zirombo zidzayidya pa nthawi yonse yachisanu.
7 Tanī laikā Tam Kungam Cebaot nesīs dāvanas no tās tautas, kas lielu slaiku augumu, un no tās tautas, kas bijājama tālu tālu, no tās tautas, kas pavēlētāja un saminēja, kam upes zemi dala, uz to vietu, kur Tā Kunga Cebaot vārds, uz Ciānas kalnu.
Pa nthawi imeneyo anthu adzabwera ndi mphatso kwa Yehova Wamphamvuzonse, zochokera kwa anthu ataliatali ndi osalala, kuchokera kwa mtundu wa anthu woopedwa ndi anthu apafupi ndi akutali omwe, mtundu wa anthu amphamvu ndi a chiyankhulo chachilendo, anthu amene dziko lawo ndi logawikanagawikana ndi mitsinje. Adzabwera nazo mphatso ku Phiri la Ziyoni, ku malo a Dzina la Yehova Wamphamvuzonse.