< Jesajas 14 >

1 Jo Tas Kungs apžēlosies par Jēkabu un atkal izredzēs Israēli un tos pārvedīs savā zemē. Un svešinieki ar tiem biedrosies un pieķersies Jēkaba namam.
Yehova adzachitira chifundo Yakobo; adzasankhanso Israeli ndi kuwalola kuti akhalenso mʼdziko lawo. Alendo adzabwera kudzakhala nawo ndi kudziphatika okha kukhala ngati a mʼnyumba ya Yakobo.
2 Un tautas tos ņems un vadīs uz viņu vietām, un Israēla nams Tā Kunga zemē tos iemantos par kalpiem un kalponēm, un tie tos turēs cietumā, kas viņus bija cietumā turējuši, un valdīs par saviem dzinējiem.
Anthu a mitundu ina adzaperekeza a Israeli ku dziko lawo. Tsono Aisraeli adzasandutsa anthu a mitundu ina aja kukhala antchito awo aamuna ndi aakazi mʼdziko la Yehova. Ndiye kuti Aisraeli adzasandutsa akapolo anthu amene kale anali ambuye awo. Iwo adzasandutsa akapolo anthu amene kale ankawalamulira ndi kuwazunza.
3 Un notiks tai dienā, kad Tas Kungs tev dusu dos no tavām sāpēm un no tavām izbailēm un no tās grūtās kalpošanas, ar ko tie tevi kalpinājuši,
Yehova akadzakupumitsani ku zowawa ndi mavuto, ndiponso kuntchito yakalavulagaga imene ankakugwiritsani,
4 Tad tu šo dziesmu dziedāsi pret Bābeles ķēniņu un sacīsi: Kā tas dzinējs pagalam! Kā tie spaidi pagalam!
mudzayankhula monyogodola mfumu ya Babuloni kuti, Wopsinja uja watha! Ukali wake uja watha!
5 Tas Kungs bezdievīgiem salauzis zizli, valdītājiem rīksti,
Yehova wathyola chikwapu cha anthu oyipa, Iye waphwanya ndodo ya olamulira.
6 Kas ļaudis briesmīgi mocīja ar mokām bez mitēšanās, kas ar bardzību valdīja pār tautām, ar spaidīšanu bez gala.
Mfumu ya ku Babuloni inkakantha mitundu ya anthu mwaukali powamenya kosalekeza, Iyo inkagonjetsa anthu a mitundu ina mwaukali ndikuwazunza kosalekeza.
7 Visa zeme dus un atpūšas, tā skanēt skan no gavilēšanas.
Koma tsopano mayiko onse ali pa mpumulo ndi pa mtendere; ndipo akuyimba mokondwa.
8 Un priedes priecājās par tevi un ciedru koki uz Lībanus (un saka): kamēr tu guli pie zemes, neviens nenāk, mūs nocirst.
Ngakhale mitengo ya payini ndi mikungudza ya ku Lebanoni ikuyimba za iwe mokondwa ndipo ikuti, “Chigwetsedwere chako pansi, palibe wina anabwera kudzatigwetsa.”
9 Elle apakšā tevis dēļ rīb, tev pretim ejot; kad tu nāci, viņa tevis dēļ uzmodina mirušos, visus zemes lielkungus, viņa visiem tautu ķēniņiem liek celties no krēsliem. (Sheol h7585)
Ku manda kwatekeseka kuti akulandire ukamabwera; mizimu ya anthu akufa, aja amene anali atsogoleri a dziko lapansi, yadzutsidwa. Onse amene anali mafumu a mitundu ya anthu ayimiritsidwa pa mipando yawo. (Sheol h7585)
10 Tie visi runā un saka uz tevi: arī tu esi palicis bez spēka tā kā mēs, tu mums palicis līdzīgs.
Onse adzayankha; adzanena kwa iwe kuti, “Iwenso watheratu mphamvu ngati ife; Iwe wafanana ndi ife.”
11 Tava greznība nogrimusi ellē un tavu kokļu skaņa; kodes būs tavas cisas, un tārpi tavs apsegs. (Sheol h7585)
Ulemerero wako wonse walowa mʼmanda, pamodzi ndi nyimbo za azeze ako; mphutsi zayalana pogona pako ndipo chofunda chako ndi nyongolotsi. (Sheol h7585)
12 Kā tu esi kritis no debesīm, tu rīta zvaigzne, tu ausekļa dēls! Kā tu nocirsts zemē, kas tautas pārvarēji?
Wagwa pansi bwanji kuchoka kumwamba, iwe nthanda, mwana wa mʼbandakucha! Wagwetsedwa pansi pa dziko lapansi, Iwe amene unagonjetsapo mitundu ya anthu!
13 Un tu sacīji savā sirdī: es uzkāpšu debesīs, es paaugstināšu savu goda krēslu pār Dieva zvaigznēm, es apsēdīšos uz saiešanas kalna ziemeļu galā,
Mu mtima mwako unkanena kuti, “Ndidzakwera mpaka kumwamba; ndidzakhazika mpando wanga waufumu pamwamba pa nyenyezi za Mulungu; ndidzakhala pa mpando waufumu pa phiri losonkhanirako, pamwamba penipeni pa phiri la kumpoto.
14 Es uzkāpšu padebešu kalnos, tam Visuaugstajam es līdzināšos.
Ndidzakwera pamwamba pa mitambo; ndidzafanana ndi Wammwambamwamba.”
15 Tiešām, ellē tu esi nogāzts, pašā bedres dziļumā. (Sheol h7585)
Koma watsitsidwa mʼmanda pansi penipeni pa dzenje. (Sheol h7585)
16 Kas tevi redz, tie uz tevi skatās un tevi aplūko: vai šis tas vīrs, kas zemi kustināja un darīja valstis drebam.
Anthu akufa adzakupenyetsetsa nadzamalingalira za iwe nʼkumati, “Kodi uyu ndi munthu uja anagwedeza dziko lapansi ndi kunjenjemeretsa maufumu,
17 Kas pasauli pārvērta par tuksnesi un viņas pilsētas postīja, kas viņas ļaudis no cietuma neatlaida mājās?
munthu amene anasandutsa dziko lonse chipululu, amene anagwetsa mizinda yake ndipo sankalola kuti anthu ogwidwa abwerere kwawo?”
18 Visi tautu ķēniņi, tie visi guļ zemē ar godu, ikviens savā namā.
Mafumu onse a mitundu ya anthu akugona mwaulemu aliyense mʼmanda akeake.
19 Bet tu esi tālu atmests no sava kapa, kā nieka žagars, apklāts ar nokautiem, zobena nodurtiem, kas grimst akmeņu bedrē, - tā kā samīta maita.
Koma iwe watayidwa kunja kwa manda ako, ngati nthambi yowola ndi yonyansa. Mtembo wako waphimbidwa ndi anthu ophedwa; amene anabayidwa ndi lupanga, anatsikira mʼdzenje lamiyala ngati mtembo woponderezedwa.
20 Ar viņiem kopā tu nebūsi kapā; jo savu zemi tu esi postījis un nokāvis savus ļaudis; ļauna darītāju dzimums netiks pieminēts mūžīgi.
Sudzayikidwa nawo mʼmanda mwaulemu, chifukwa unawononga dziko lako ndi kupha anthu ako. Zidzukulu za anthu oyipa sizidzakumbukika nʼpangʼono pomwe.
21 Taisāties kaut viņa bērnus viņu tēvu nozieguma dēļ, ka tie neceļas un zemi neiemanto un nepiepilda pasauli ar pilsētām.
Konzani malo woti muphere ana ake aamuna chifukwa cha machimo a makolo awo; kuti angadzuke ndi kulanda dziko lapansi ndi kulidzaza dziko lonselo ndi mizinda yawo.
22 Jo Es celšos pret tiem, saka Tas Kungs Cebaot, un izdeldēšu no Bābeles vārdu un dzimumu un bērnu un bērna bērnu, saka Tas Kungs.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Ine ndidzathira nkhondo mzinda wa Babuloni. Ndidzachotseratu mu Babuloni dzina lake ndi onse otsaliramo. Ndiye kuti sipadzakhala ana kapena zidzukulu,” akutero Yehova.
23 Un Es to došu par īpašumu ežiem un par ūdens purvu, un Es tos izmēzīšu ar izdeldēšanas slotu, saka Tas Kungs Cebaot.
“Ndidzawusandutsa mzindawo malo okhalamo anungu ndiponso dambo lamatope; ndidzawusesa ndi tsache lowononga,” akutero Yehova Wamphamvuzonse.
24 Tas Kungs Cebaot ir zvērējis un sacījis: tiešām, kā Es esmu nodomājis, tā notiks, un kā Es esmu nospriedis, tā būs,
Yehova Wamphamvuzonse walumbira kuti, “Ndithudi, monga ndaganizira ndidzachitadi choncho, ndipo monga momwe ndatsimikizira zidzakhala momwemo ndithu.
25 Ka Es Asuru satriekšu Savā zemē, un uz Saviem kalniem viņu samīdīšu, ka viņa jūgs no tiem top atņemts un viņa nasta zūd no viņu pleciem.
Ndidzawawononga Asiriya mʼdziko langa; ndidzawapondereza ndi mapazi pa mapiri anga; ndidzachotsa goli lawo pa anthu anga, ndipo ndidzachotsa katundu wawo pa mapewa awo.”
26 Šis ir tas padoms, kas nospriests pār visu zemi, un šī ir tā roka, kas izstiepta pār visām tautām.
Izi ndizo ndakonza kuti zichitike pa dziko lonse lapansi, ndatambasula dzanja pa anthu a mitundu yonse.
27 Jo Tas Kungs Cebaot to nodomājis; kas to iznīcinās? Un Viņa roka ir izstiepta, kas to novērsīs?
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse watsimikiza, ndipo ndani angamuletse? Dzanja lake latambasulidwa ndipo ndani angalibweze?
28 Tai gadā, kad ķēniņš Ahazs nomira, notika šis spriedums:
Uthenga uwu unabwera chaka chimene mfumu Ahazi anamwalira:
29 Nepriecājies, visa Fīlistu zeme, ka tā rīkste salauzta, kas tevi sita. Jo no čūskas saknes nāk odze, un viņas auglis būs spārnains pūķis.
Musakondwere inu Afilisti nonse kuti Asiriya amene anali ngati ndodo yokukanthani anathedwa; chifukwa kuchokera ku njoka yomweyi (mfumu ya Aasiriya) mudzatuluka mphiri, ndipo chipatso chake chidzakhala njoka yaliwiro ndiponso yaululu.
30 Jo visupēdīgie nabagi baudīs pilnību, un tukšinieki apgulsies ar mieru. Bet tavu sakni Es nokaušu caur badu, un tavus atlikušos viņš kaus zemē.
Osaukitsitsa adzapeza chakudya ndipo amphawi adzakhala mwamtendere. Koma anthu ako ndidzawawononga ndi njala, ndipo njalayo idzapha ngakhale opulumuka ako.
31 Kauciet, vārti! Kliedz, pilsēta! Izkūsti, visa Fīlistu zeme! Jo no ziemeļa puses nāk dūmi, un neviens no viņa pulkiem nenoklīst.
Lirani kwambiri, anthu a pa chipata! Fuwulani kwambiri, anthu a mu mzinda! Njenjemerani ndi mantha, inu Afilisti nonse! Mtambo wa utsi ukuchokera kumpoto, ndipo palibe wamantha pakati pa ankhondo ake.
32 Un ko tad atbildēs tautu vēstnešiem? Ka Tas Kungs Ciānu stiprinājis un Viņa ļaužu bēdīgie tur atrod patvērumu.
Kodi tidzawayankha chiyani amithenga a ku Filisitiya? “Yehova wakhazikitsa Ziyoni, ndipo mu mzinda wakewu, anthu ozunzika apeza populumukira.”

< Jesajas 14 >