< Ecechiela 3 >
1 Un Viņš sacīja uz mani: Cilvēka bērns, ēd, kas tavā priekšā, ēd šo satīto grāmatu, un ej un runā uz Israēla namu.
Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
2 Tad es atdarīju savu muti, un Viņš man deva ēst to satīto grāmatu.
Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
3 Un Viņš sacīja uz mani: Cilvēka bērns, dod savam vēderam ēst un pildi savas iekšas ar šo satīto grāmatu, ko Es tev dodu. Tad es ēdu, un tas bija manā mutē tik salds kā medus.
Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
4 Un Viņš sacīja uz mani: Cilvēka bērns, ej pie Israēla nama un runā uz tiem Manus vārdus.
Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
5 Jo tu netopi sūtīts pie ļaudīm, kam tumša valoda un grūta mēle, bet uz Israēla namu,
Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
6 Ne pie lielām tautām, kam tumšas valodas un grūtas mēles, kuru vārdus tu nevari saprast; bet pie tiem Es tevi esmu sūtījis, tie tevi var saprast.
Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
7 Bet Israēla nams negribēs tevi klausīt, tāpēc ka tie Mani negrib klausīt. Jo visam Israēla namam ir bieza piere un cieta sirds.
Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
8 Redzi, tavu vaigu Es daru cietu kā viņu vaigu, un tavu pieri biezu kā viņu pieri
Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
9 Tavu pieri Es esmu darījis kā dimantu, cietāku pār klinti. Nebīsties no tiem un neiztrūksties no viņu vaiga; jo tie ir atkāpēju suga.
Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
10 Un Viņš sacīja uz mani: Cilvēka bērns, ņem pie sirds visus Manus vārdus, ko Es uz tevi runāšu, un klausies tos ar savām ausīm.
Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
11 Un ej pie tiem aizvestiem, pie savu ļaužu bērniem, un runā uz tiem un saki uz tiem: tā saka Tas Kungs Dievs; - vai tie nu klausa, vai neklausa.
Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
12 Tad Tas Gars mani pacēla, un es dzirdēju aiz sevis liela trokšņa balsi, kad Tā Kunga godība pacēlās no savas vietas,
Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
13 Un (es dzirdēju) to dzīvo spārnus, kas viens pie otra sniedzās, un to skrituļu rībēšanu viņiem līdzās un liela trokšņa skaņu.
Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
14 Tad Tas Gars mani pacēla un mani aizņēma, un es gāju rūgts sava gara karstumā, bet Tā Kunga roka bija pār mani stipra.
Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
15 Un es nonācu uz Telabību pie tiem aizvestiem, kas dzīvoja pie Ķebaras upes, un paliku tur, kur tie dzīvoja, un paliku tur viņu vidū septiņas dienas ļoti noskumis.
Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
16 Un pēc septiņām dienām Tā Kunga vārds uz mani notika sacīdams:
Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
17 Cilvēka bērns, Es tevi esmu licis par sargu Israēla namam, ka tev no Manas mutes būs klausīties to vārdu un viņiem no Manas puses piekodināt.
“Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
18 Kad Es saku uz bezdievīgo: tu mirdams mirsi, - un tu viņu nepamāci un nerunā, ka tu bezdievīgo atgriezi no viņa bezdievīgā ceļa un viņu paturi dzīvu, tad bezdievīgais nomirs savā noziegumā, bet viņa asinis Es prasīšu no tavas rokas.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
19 Bet kad tu bezdievīgo pamāci un viņš neatgriežas no savas bezdievības un no sava bezdievīgā ceļa, tad viņš nomirs savā noziegumā, bet tu savu dvēseli esi izglābis.
Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
20 Un kad taisnais nogriežas no savas taisnības un dara ļaunu, tad Es viņam likšu piedauzīties, un tas mirs; kad tu viņu neesi pamācījis, tad viņš nomirs savos grēkos, un viņa taisnība, ko viņš darījis, netaps pieminēta, bet viņa asinis Es prasīšu no tavas rokas.
“Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
21 Bet kad tu taisno pamāci, ka tam taisnam nebūs grēkot, un viņš negrēko, tad viņš tiešām dzīvos, tāpēc ka tas ir tapis pamācīts, un tu savu dvēseli esi izglābis.
Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
22 Un Tā Kunga roka bija tur uz manis, un Viņš uz mani sacīja: celies, ej ārā ielejā, un tur Es ar tevi runāšu.
Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
23 Tad es cēlos un izgāju ielejā, un redzi, tur stāvēja Tā Kunga godība, tā kā tā godība, ko es biju redzējis pie Ķebaras upes. Un es nokritu uz savu vaigu.
Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
24 Tad gars nāca iekš manis un mani cēla kājās, un Viņš runāja uz mani un sacīja uz mani: ej, ieslēdzies savā namā.
Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
25 Un redzi, tu cilvēka bērns, tev apliks virves, un tevi ar tām saistīs, un tu no tām nevarēsi noiet viņu vidū.
Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
26 Un Es tavai mēlei likšu pielipt pie zoda, un tu paliksi mēms un tiem nebūsi par pārmācītāju; jo tie ir atkāpēju suga.
Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
27 Bet kad Es ar tevi runāšu, tad Es atdarīšu tavu muti, un tev būs sacīt uz tiem: tā saka Tas Kungs Dievs! Kas klausa, lai klausa, un kas neklausa, lai neklausa; jo tie ir atkāpēju suga.
Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”